Psalm 23
A psalm of David.
1The Lord is my shepherd. He gives me everything I need.
2He lets me lie down in fields of green grass.
He leads me beside quiet waters.
3He gives me new strength.
He guides me in the right paths
for the honor of his name.
4Even though I walk
through the darkest valley,
I will not be afraid.
You are with me.
Your shepherd’s rod and staff
comfort me.
5You prepare a feast for me
right in front of my enemies.
You pour oil on my head.
My cup runs over.
6I am sure that your goodness and love will follow me
all the days of my life.
And I will live in the house of the Lord
forever.
Salimo 23
Salimo la Davide.
1Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
2Amandigoneka pa msipu wobiriwira,
amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
3amatsitsimutsa moyo wanga.
Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo
chifukwa cha dzina lake.
4Ngakhale ndiyende
mʼchigwa cha mdima wakuda bii,
sindidzaopa choyipa,
pakuti Inu muli ndi ine;
chibonga chanu ndi ndodo yanu
zimanditonthoza.
5Mumandikonzera chakudya
adani anga akuona.
Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta;
chikho changa chimasefukira.
6Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata
masiku onse a moyo wanga,
ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova
kwamuyaya.