Mwana Ni Mkuu Kuliko Malaika
11:1 Efe 3:1; 2Kor 1:1; Hes 12:6, 8; Yn 9:29; Ebr 2:3; 4:8; 12:25; Lk 1:70; Mdo 2:30Zamani Mungu alisema na baba zetu kwa njia ya manabii mara nyingi na kwa njia mbalimbali, 21:2 Kum 4:30; Ebr 9:26; 1Pet 1:20; Ebr 1:5; Mt 3:17; Ebr 3:6; 5:8; 7:28; Za 2:8; Mt 28:18; Yn 1:3; Ebr 11:3lakini katika siku hizi za mwisho anasema nasi kwa njia ya Mwanawe, ambaye amemweka kuwa mrithi wa vitu vyote, na ambaye kupitia kwake aliuumba ulimwengu. 31:3 Yn 1:14; 14:9; Kol 1:17; Tit 2:14; Ebr 7:27; Mk 16:19Mwana ni mngʼao wa utukufu wa Mungu na mfano halisi wa nafsi yake, akivihifadhi vitu vyote kwa neno lake lenye uweza. Akiisha kufanya utakaso kwa ajili ya dhambi, aliketi mkono wa kuume wa Aliye Mkuu huko mbinguni. 41:4 Efe 1:21; Flp 2:9, 10; Ebr 8:6Kwa hiyo alifanyika bora kuliko malaika, kama jina alilorithi lilivyo bora kuliko lao.
51:5 Za 2:7; Mt 3:17; 2Sam 7:14Kwa maana ni malaika yupi ambaye wakati wowote Mungu alipata kumwambia,
“Wewe ni Mwanangu;
leo mimi nimekuzaa?”
Au tena,
“Mimi nitakuwa Baba yake,
naye atakuwa Mwanangu?”
61:6 Yn 3:16; Kol 1:18; Ebr 10:5; Kum 32:43; Za 97:7Tena, Mungu amletapo mzaliwa wake wa kwanza ulimwenguni, anasema,
“Malaika wote wa Mungu na wamsujudu.”
71:7 Za 104:4Anenapo kuhusu malaika asema,
“Huwafanya malaika wake kuwa pepo,
watumishi wake kuwa miali ya moto.”
81:8 Lk 1:33; Za 45:6, 7Lakini kwa habari za Mwana asema,
“Kiti chako cha enzi, Ee Mungu,
kitadumu milele na milele,
nayo haki itakuwa fimbo ya utawala
ya ufalme wako.
91:9 Flp 2:9; Isa 61:1, 3; Za 45:6, 7; Mdo 4; 27; 10:38Umependa haki na kuchukia uovu;
kwa hiyo Mungu, Mungu wako,
amekuweka juu ya wenzako
kwa kukupaka mafuta ya furaha.”
101:10 Za 8:6; 102:25; Zek 12:1Pia asema,
“Hapo mwanzo, Ee Bwana, uliweka misingi ya dunia,
nazo mbingu ni kazi ya mikono yako.
111:11 Isa 34:4; 51:6; Ebr 12:27; Mt 24:35; 2Pet 3:7; 3:10; Ufu 21:1Hizo zitatoweka, lakini wewe utadumu;
zote zitachakaa kama vazi.
121:12 Ebr 13:8; Za 102:25, 27Utazikungʼutakungʼuta kama joho,
nazo zitachakaa kama vazi.
Lakini wewe hubadiliki,
nayo miaka yako haikomi kamwe.”
131:13 Ebr 1:3; Mk 16:19; Yos 10:24; Ebr 10:13; Za 110:1; Mt 22:44Je, ni kwa malaika yupi ambaye Mungu amepata kumwambia wakati wowote,
“Keti mkono wangu wa kuume,
hadi nitakapowaweka adui zako
chini ya miguu yako”?
141:14 Za 91:11; 103:20; Dan 7:10; Mt 25:34; Mk 10:17; Mdo 20:32; Rum 11:14; Ebr 2:3; 5:9; 9:28Je, malaika wote si roho watumikao, waliotumwa kuwahudumia wale watakaourithi wokovu?
Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo
1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,
“Iwe ndiwe mwana wanga;
Ine lero ndakhala Atate ako.”
Kapena kunenanso kuti,
“Ine ndidzakhala abambo ake;
iye adzakhala mwana wanga.”
6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,
“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
7Iye ponena za angelo akuti,
“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,
amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
8Koma za Mwana wake akuti,
“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,
ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.
9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu
pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
10Mulungu akutinso,
“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;
ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.
Izo zidzatha ngati zovala.
12Mudzazipindapinda ngati chofunda;
ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.
Koma Inu simudzasintha,
ndipo zaka zanu sizidzatha.”
13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,
“Khala kudzanja langa lamanja
mpaka nditapanga adani ako
kukhale chopondapo mapazi ako.”
14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?