Obadia 1 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Obadia 1:1-21

11:1 Mwa 25:14; Isa 1:1; 21:11; Yoe 3:19; Mal 1:3; Eze 25:12-14; Yer 6:4-5; 49:7-22; Isa 11:14; 18:2; 34:11Maono ya Obadia.

Hili ndilo asemalo Bwana Mwenyezi kuhusu Edomu:

Tumesikia ujumbe kutoka kwa Bwana:

Mjumbe alitumwa kwa mataifa kusema,

“Inukeni, twendeni tukapigane vita dhidi yake.”

2“Angalieni, nitawafanya wadogo miongoni mwa mataifa,

mtadharauliwa kabisa.

31:3 Isa 14:13; 16:6; 2Fal 14:7; 2Nya 25:11-12; Ufu 18:7Kiburi cha moyo wako kimekudanganya,

wewe unayeishi katika majabali ya miamba

na kufanya makao yako juu,

wewe unayejiambia mwenyewe,

‘Ni nani awezaye kunishusha chini?’

41:4 Isa 10:14; 14:13; 14:14, 15; Ay 20:6; Amo 9:2; Yer 49:16; Hab 2:9Ingawa unapaa juu kama tai

na kufanya kiota chako kati ya nyota,

nitakushusha chini kutoka huko,”

asema Bwana.

51:5 Isa 24:13; Kum 4:27; 24:21“Ikiwa wevi wangekuja kwako,

ikiwa wanyangʼanyi wangekujia usiku:

Lo! Tazama ni maafa kiasi gani yangekuwa yanakungojea:

je, si wangeiba tu kiasi ambacho wangehitaji?

Kama wachuma zabibu wangekuja kwako,

je, wasingebakiza zabibu chache?

6Lakini tazama jinsi Esau atakavyotekwa,

jinsi hazina zake zilizofichwa zitatekwa nyara!

71:7 Yer 30:14; Za 41:9Wote ulioungana nao watakufukuza hadi mpakani,

rafiki zako watakudanganya na kukushinda,

wale wanaokula mkate wako watakutegea mtego,

lakini hutaweza kuugundua.

81:8 Ay 5:12; Isa 29:14“Katika siku hiyo,” asema Bwana,

“je, sitaangamiza watu wenye hekima wa Edomu,

watu wenye ufahamu katika milima ya Esau?

91:9 Mwa 36:11, 34; Amo 2:16; Za 76:5; Yer 49:22; Nah 3:13Ee Temani, mashujaa wako watatiwa hofu,

kila mmoja katika milima ya Esau

ataangushwa chini kwa kuchinjwa.

101:10 Yoe 3:19; Amo 1:11-12; Za 137:7; Mwa 47:21; Eze 35:5, 15; Mal 1:4; Eze 25:12-14; 35:9Kwa sababu ya jeuri uliyofanya dhidi ya ndugu yako Yakobo,

aibu itakufunika;

utaangamizwa milele.

111:11 Ay 6:27; Nah 3:10; Eze 24:6Siku ile ulisimama mbali ukiangalia

wakati wageni walipojichukulia utajiri wake

na watu wa nchi nyingine walipoingia malango yake

wakipiga kura kwa ajili ya Yerusalemu,

ulikuwa kama mmoja wao.

121:12 Eze 25:6; 35:15; Mit 17:5; 24:17; Mik 4:11; Ay 31:29Usingemdharau ndugu yako

katika siku ya msiba wake,

wala kufurahia juu ya watu wa Yuda

katika siku ya maangamizi yao,

wala kujigamba sana

katika siku ya taabu yao.

131:13 Eze 35:5Usingeingia katika malango ya watu wangu

katika siku ya maafa yao,

wala kuwadharau katika janga lao

katika siku ya maafa yao,

wala kunyangʼanya mali zao

katika siku ya maafa yao.

14Usingengoja kwenye njia panda

na kuwaua wakimbizi wao,

wala kuwatoa watu wake waliosalia

katika siku ya shida yao.

151:15 Yer 46:10; 50:29; Hab 2:8; Amu 1:7; Za 137:8; Eze 35:15; Yoe 2:31; 3:7-8; Eze 30:3; Amo 5:8“Siku ya Bwana iko karibu

kwa mataifa yote.

Kama ulivyofanya, nawe utafanyiwa vivyo hivyo,

matendo yako yatakurudia juu ya kichwa chako.

161:16 Yer 25:15; 49:12; Mao 4:21-22; Isa 51:17; Kut 15:17; Eze 25:12-14Kama vile ulivyokunywa juu ya mlima wangu mtakatifu,

vivyo hivyo mataifa yote watakunywa mfululizo,

watakunywa na kunywa,

nao watatoweka kana kwamba hawajawahi kuwepo.

171:17 Za 69:35; 74:2; Isa 14:1-2; Amo 9:11-15; Zek 8:12Lakini katika Mlima Sayuni kutakuwepo

na wale watakaookoka;

nao utakuwa mtakatifu,

nayo nyumba ya Yakobo

itamiliki urithi wake.

181:18 Zek 12:6; Yer 49:10; Isa 1:31Nyumba ya Yakobo itakuwa moto,

na nyumba ya Yosefu itakuwa mwali wa moto;

nayo nyumba ya Esau itakuwa bua kavu,

nao wataiwasha moto na kuiteketeza.

Hakutakuwa na watakaosalimika

kutoka nyumba ya Esau.”

Bwana amesema.

191:19 Isa 11:14; Sef 2:7; Yer 31:5; Hes 1:36Watu kutoka nchi ya Negebu

wataikalia milima ya Esau,

na watu kutoka miteremko ya vilima

watamiliki nchi ya Wafilisti.

Watayakalia mashamba ya Efraimu na Samaria,

naye Benyamini atamiliki Gileadi.

201:20 Lk 4:26; Yer 33:13; 1Fal 17:9-10Kundi la Waisraeli walioko uhamishoni Kanaani

watarudi na kumiliki nchi mpaka Sarepta.

Walioko uhamishoni Sefaradi kutoka Yerusalemu

watamiliki miji ya Negebu.

211:21 Dan 2:24, 44; Ufu 11:15; Zek 14:9; Isa 19:20; Amu 3:9; Za 22:28; 47:9Waokoaji watakwea juu ya Mlima Sayuni

kutawala milima ya Esau.

Nao ufalme utakuwa wa Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Obadiya 1:1-21

Masomphenya a Obadiya

1Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,

“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;

udzanyozedwa kwambiri.

3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe

ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,

iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,

‘Ndani anganditsitse pansi?’

4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga

ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,

kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,

aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!

Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

Ngati anthu othyola mphesa akanafika,

kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,

chuma chake chobisika chidzabedwa!

7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;

abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;

amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,

koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,

kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,

anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?

9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,

ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau

adzaphedwa pa nkhondo.

10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,

udzakhala wamanyazi;

adzakuwononga mpaka muyaya.

11Pamene adani

ankamulanda chuma chake

pamene alendo analowa pa zipata zake

ndi kuchita maere pa Yerusalemu,

pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.

12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako

pa nthawi ya tsoka lake,

kapena kunyogodola Ayuda

chifukwa cha chiwonongeko chawo,

kapena kuwaseka pa nthawi ya

mavuto awo.

13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga

pa nthawi ya masautso awo,

kapena kuwanyogodola

pa tsiku la tsoka lawo,

kapena kulanda chuma chawo

pa nthawi ya masautso awo.

14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu

kuti uphe Ayuda othawa,

kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka

pa nthawi ya mavuto awo.”

15“Tsiku la Yehova layandikira

limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.

Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;

zochita zako zidzakubwerera wekha.

16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,

koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;

iwo adzamwa ndi kudzandira

ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;

phirilo lidzakhala lopatulika,

ndipo nyumba ya Yakobo

idzalandira cholowa chake.

18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto

ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;

nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,

ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.

Sipadzakhala anthu opulumuka

kuchokera mʼnyumba ya Esau.”

Yehova wayankhula.

19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala

ku mapiri a Esau,

ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri

adzatenga dziko la Afilisti.

Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,

ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.

20Aisraeli amene ali ku ukapolo

adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;

a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi

adzalandira mizinda ya ku Negevi.

21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni

ndipo adzalamulira mapiri a Esau.

Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.