Abramu Na Loti Watengana
113:1 Mwa 45:25; 12:9; 11:27Hivyo Abramu akakwea kutoka Misri kwenda Negebu, yeye na mkewe na kila kitu alichokuwa nacho, pia Loti akaenda pamoja naye. 213:2 Mwa 12:5; 26:13; 32:15; Mit 10:22; Ay 1:3; 42:12Wakati huo Abramu alikuwa tajiri sana wa mifugo, fedha na dhahabu.
313:3 Mwa 12:8-9Kutoka Negebu, akapita mahali hadi mahali, hadi akafika Betheli, mahali hapo ambapo mwanzoni alipiga hema lake kati ya Betheli na Ai 413:4 Mwa 12:7; 4:26hapo ambapo alikuwa amejenga madhabahu ya kwanza. Huko Abramu akaliitia jina la Bwana.
513:5 Mwa 11:27Basi Loti, ambaye alikuwa anafuatana na Abramu, alikuwa pia na makundi ya mbuzi, kondoo, ngʼombe na mahema. 613:6 Mwa 12:5; 33:9; 36:7Lakini nchi haikuwatosha kukaa pamoja kwa ajili ya wingi wa mali zao. 713:7 Mwa 26:20-21; 10:18; 15:20; 12:6; 34:30; Hes 20:3; Kut 3:8; Amu 1:4Ukazuka ugomvi kati ya wachunga mifugo wa Abramu na wale wa Loti. Wakati huo, Wakanaani na Waperizi ndio waliokuwa wenyeji wa nchi hiyo.
813:8 Mwa 11:27; 19:9; Mit 15:18; 20:3; Kut 2:14; Hes 16:13; Za 133:1Hivyo Abramu akamwambia Loti, “Pasiwe na ugomvi wowote kati yangu na wewe, wala kati ya wachungaji wangu na wako, kwa kuwa sisi ni ndugu. 913:9 Mwa 20:15; 34:10; 47:6; Yer 40:4Je, nchi yote haiko mbele yako? Tutengane. Kama ukielekea kushoto, nitakwenda kulia; kama ukielekea kulia, mimi nitakwenda kushoto.”
1013:10 1Fal 7:47; 2Nya 4:17; Hes 13:29; 33:48; Mwa 19:22; 2:8-10; 46:7; 14:2, 8Loti akatazama akaona lile bonde lote la Yordani kuwa lilikuwa na maji tele, kama bustani ya Bwana, kama nchi ya Misri, kuelekea Soari. (Hii ilikuwa kabla Bwana hajaharibu Sodoma na Gomora.) 11Hivyo Loti akajichagulia bonde lote la Yordani, akaelekea upande wa mashariki. Watu hao wawili wakatengana: 1213:12 Mwa 10:19; 11:27; 19:17-29; 14:12Abramu akaishi katika nchi ya Kanaani, wakati Loti aliishi miongoni mwa miji ya lile bonde na kupiga mahema yake karibu na Sodoma. 1313:13 Mwa 18:20; 19:4; 19:5; 20:6; 39:9; Isa 1:10; 3:9; Hes 32:23; 1Sam 12:23; 2Sam 12:13; Za 51:4; Eze 16:49-50; 2Pet 2:8Basi watu wa Sodoma walikuwa waovu, wakifanya sana dhambi dhidi ya Bwana.
1413:14 Mwa 28:14; 32:12; 48:16; Kum 3:27; 13:17; Isa 54:3Baada ya Loti kuondoka Bwana akamwambia Abramu, “Ukiwa hapo ulipo, inua macho yako utazame kaskazini na kusini, mashariki na magharibi. 1513:15 Mwa 12:7; Gal 3:16Nchi yote unayoiona nitakupa wewe na uzao wako hata milele. 1613:16 Mwa 12:2; 16:10; 17:20; 21:13-18; 25:16; Hes 23:10Nitaufanya uzao wako uwe mwingi kama mavumbi ya nchi, hivyo kama kuna yeyote awezaye kuhesabu mavumbi, basi uzao wako utahesabika. 1713:17 Mwa 12:7; 15:7; Hes 13:17-25Ondoka, tembea katika marefu na mapana ya nchi, kwa maana ninakupa wewe.”
1813:18 Mwa 8:20; 14:13; 18:1; 23:2, 17, 19; 25:9; 49:30; 50:13; 35:27; Hes 13:22; Yos 10:3, 36; Amu 1:10; 1Sam 30:31; 2Sam 2:1-11; 1Nya 11:1Basi Abramu akaondoa mahema yake, akaenda kuishi karibu na mialoni ya Mamre huko Hebroni, huko akamjengea Bwana madhabahu.
Abramu Asiyana ndi Loti
1Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo. 2Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
3Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba, 4ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
5Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti. 6Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi. 7Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
8Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale. 9Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
10Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora). 11Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana. 12Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu. 13Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
14Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo. 15Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya. 16Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako. 17Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
18Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.