Malaki 3 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Malaki 3:1-18

13:1 Hes 27:21; 2Nya 36:15; Isa 40:3; 63:9; Mt 11; 10; 3:3; Lk 7:27; Mik 5:2; 1Sam 9:20; Mdo 7:38; Hag 2:7“Angalieni, nitamtuma mjumbe wangu, atakayeiandaa njia mbele yangu. Ndipo ghafula Bwana mnayemtafuta atakuja hekaluni mwake. Mjumbe wa Agano, ambaye mnamwonea shauku, atakuja,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

23:2 Eze 7:7; 22:14; Ufu 6:17; Dan 7:13; Yoe 2:31; Mt 16:27; Yak 5:8; 2Pet 3:4; 1Sam 6:20; Isa 1:31; 30:30; 4:4; Zek 13:9; Mt 3:10-12; Ay 9:30Lakini ni nani atakayeweza kustahimili hiyo siku ya kuja kwake? Ni nani awezaye kusimama atakapotokea? Kwa kuwa atakuwa kama moto wa mfua fedha au kama sabuni ya afuaye nguo. 33:3 Eze 12:10; 1Kor 3:13; 1Nya 23:28; Isa 1:25; Ay 28:1; Za 12:6; 132:9; Ufu 3:18; Zek 13:9; Rum 15:16; 1Pet 2:5Ataketi kama mfuaji na asafishaye fedha. Atawatakasa Walawi, naye atawasafisha kama dhahabu na fedha. Kisha Bwana atakuwa na watu watakaoleta sadaka katika haki, 43:4 2Nya 7:3; 7:12; Za 51:19; Eze 20:40; Mal 1:11nazo sadaka za Yuda na Yerusalemu zitakubalika kwa Bwana, kama katika siku zilizopita, kama katika miaka ya zamani.

53:5 Kut 7:11; 20:14; Yak 2:11; 5:4-9; Isa 1:2; 47:9; 2Pet 2:12-14; Law 19:11-13; Yer 7:9; Yak 5:4; Kut 22:21-22; Kum 24:19; 31:12; Eze 22:7“Basi nitakuja karibu nanyi ili kuhukumu. Nami nitakuwa mwepesi kushuhudia dhidi ya wachawi, wazinzi, waapao kwa uongo, wanaopunja vibarua malipo yao, wanaowaonea wajane na yatima, na wanaowanyima wageni haki, lakini hawaniogopi mimi,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

Kumwibia Mungu

63:6 Hes 23:19; Ebr 7:21; Yak 1:17; Ay 34:15; Hos 11:9; 1Sam 15:29; Rum 11:29; Mao 3:22“Mimi Bwana sibadiliki. Kwa hiyo ninyi, enyi uzao wa Yakobo, hamjaangamizwa. 73:7 Kut 32:8; Mdo 7:51; Yer 7:26; Isa 44:22; Kum 30:1-4; Isa 55:6-7; Eze 18:32; Yak 4:8; Zek 1:3Tangu wakati wa baba zenu mmegeukia mbali na amri zangu nanyi hamkuzishika. Nirudieni mimi, nami nitawarudia ninyi,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

“Lakini mnauliza, ‘Tutarudi kwa namna gani?’

83:8 Zek 5:3; Law 27:30; Hes 18:21; Neh 13:10-12; Lk 18:12“Je, mwanadamu atamwibia Mungu? Hata hivyo mnaniibia mimi.

“Lakini mnauliza, ‘Tunakuibia kwa namna gani?’

“Mnaniibia zaka na dhabihu. 93:9 Kum 28:15-68; 11:26; Zek 5:3Mko chini ya laana, ninyi taifa lote, kwa sababu mnaniibia mimi. 103:10 Kut 22:29; Neh 13:12; 2Fal 7:2; Isa 44:3; Yoe 2:14, 24; 2Kor 9:8-11; Law 25:21; Mit 3:9; Mwa 7:11; 1Nya 26:29Leteni zaka kamili ghalani, ili kuwe na chakula katika nyumba yangu. Nijaribuni katika hili,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote, “nanyi mwone kama sitawafungulia madirisha ya mbinguni na kuwamwagieni baraka nyingi mpaka mkose nafasi ya kutosha. 113:11 Kut 10:15; 23:26; Kum 28:39; Amo 4:9Nami kwa ajili yenu nitamkemea yeye alaye, wala hataharibu mazao ya ardhi yenu, wala mzabibu wenu hautapukutisha matunda yake kabla ya wakati wake,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote. 123:12 Kum 28:3-12; Isa 61:9; 62:4; Eze 20:6; Dan 8:9; 2Nya 31:10“Ndipo mataifa yote yatawaita mliobarikiwa, kwa maana nchi yenu itakuwa ya kupendeza sana,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

133:13 Mal 2:17“Mmesema vitu vigumu dhidi yangu,” asema Bwana.

“Hata hivyo mnauliza, ‘Tumesema nini dhidi yako?’

143:14 Za 73:13; 100:2; Isa 1:14; 57:10; 58:3; Yn 12:26; Rum 12:11; Yos 22:5; Sef 1:12; Ay 21:14“Mmesema, ‘Ni bure kumtumikia Mungu. Tumepata faida gani kwa kushika maagizo yake na kwenda kama waombolezaji mbele za Bwana Mwenye Nguvu Zote? 153:15 Za 119:21; 14:1; 36:1-2; Yer 7:10; Ay 21:7Lakini sasa wenye kiburi wanabarikiwa. Hakika watenda mabaya wanastawi, pia hata wale wanaoshindana na Mungu ndio wanaosalimika.’ ”

163:16 Za 34:15; 56:8; 87:6; 33:18; Kut 32:32; Lk 10:20; Mit 1:7; Ebr 3:13; Kum 31:12; Ufu 11:18; Mwa 22:12; 1Fal 18:3, 12Ndipo wale waliomcha Bwana wakasemezana wao kwa wao, naye Bwana akasikiliza na akasikia. Kitabu cha kumbukumbu kikaandikwa mbele yake kuhusu wale ambao walimcha Bwana na kuliheshimu jina lake.

173:17 Isa 43:21; 26:20; Kut 8:22; Kum 7:6; Tit 2:14; Neh 13:22; Rum 8:14, 32; Za 103:13; Lk 15:1-32“Nao watakuwa watu wangu,” asema Bwana Mwenye Nguvu Zote, “katika siku ile nitakapowafanya watu kuwa hazina yangu. Nitawahurumia, kama vile kwa huruma mtu amhurumiavyo mwanawe anayemtumikia. 183:18 Mwa 18:25; Kum 32:4; Mt 25:32-33Kwa mara nyingine tena utaona tofauti kati ya wenye haki na waovu, kati ya wale wanaomtumikia Mungu na wale wasiomtumikia.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 3:1-18

1Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”

2Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa. 3Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo, 4ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.

5Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”

Kuba za Mulungu

6“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe. 7Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’

8“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera.

“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’

“Pa zakhumi ndi pa zopereka. 9Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera. 10Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo. 11Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. 12“Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

13Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine.

“Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’

14“Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse? 15Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’ ”

16Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.

17Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira. 18Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”