Habakuki 3 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Habakuki 3:1-19

Maombi Ya Habakuki

1Sala ya nabii Habakuki iliyoimbwa kwa shigionothi.3:1 Ni kifaa cha uimbaji chenye nyuzi; pia maombi kutumia kifaa hiki.

23:2 Ay 26:14; Za 119:120; 90:16; 44:1; 85:6; Isa 54:8Bwana, nimezisikia sifa zako;

nami naogopa kwa matendo yako, Ee Bwana.

Fufua kazi yako katikati ya miaka,

katikati ya miaka tangaza habari yako;

katika ghadhabu kumbuka rehema.

33:3 Mwa 36:11, 15; Isa 31:1; Hes 10:12; Za 48:10Mungu alitoka Temani,

yeye Aliye Mtakatifu kutoka Mlima Parani.

Utukufu wake ulifunika mbingu,

na sifa zake zikaifunika dunia.

43:4 Isa 18:4; Ay 9:6Mngʼao wake ulikuwa kama jua lichomozalo;

mionzi ilimulika kutoka mkononi mwake,

ambako nguvu zake zilifichwa.

53:5 Law 26:25Tauni ilimtangulia;

maradhi ya kuambukiza yalifuata nyayo zake.

63:6 Za 46:2; 114:1-6; 18:7; Kut 19:18; 23:31; Kum 32:8; Hes 21:24, 34; Mwa 49:26; 21:33Alisimama, akaitikisa dunia;

alitazama, na kuyafanya mataifa yatetemeke.

Milima ya zamani iligeuka mavumbi

na vilima vilivyozeeka vikaanguka.

Njia zake ni za milele.

73:7 Mwa 25:2; Hes 25:15; Amu 7:24-25; Kut 15:14Niliona watu wa Kushani katika dhiki,

na makazi ya Midiani katika maumivu makali.

83:8 Kut 7:20; 14:21, 22; 2Fal 2:11; Za 77:16; 68:17Ee Bwana, uliikasirikia mito?

Je, ghadhabu yako ilikuwa dhidi ya vijito?

Je, ulighadhibikia bahari

ulipoendesha farasi wako

na magari yako ya ushindi?

93:9 Kum 32:23; Za 7:12-13Uliufunua upinde wako

na kuita mishale mingi.

Uliigawa dunia kwa mito;

103:10 Za 77:16; 98:7; 93:3milima ilikuona ikatetemeka.

Mafuriko ya maji yakapita huko;

vilindi vilinguruma

na kuinua mawimbi yake juu.

113:11 Yos 10:13; Za 18:14; 144:6; Zek 9:14Jua na mwezi vilisimama kimya mbinguni

katika mngʼao wa mishale yako inayoruka,

na katika mngʼao wa mkuki wako umeremetao.

123:12 Za 44:2, 3; Mik 4:13; Isa 41:15Kwa ghadhabu ulipita juu ya dunia,

na katika hasira ulikanyaga mataifa.

133:13 Kut 13:21; Za 20:6; 28:8; 68:21; 2Sam 5:20; 23:1Ulikuja kuwaokoa watu wako,

kumwokoa uliyemtia mafuta.

Ulimponda kiongozi wa nchi ya uovu,

ukamvua toka kichwani hadi wayo.

143:14 Amu 7:22; Za 64:2-5Kwa mkuki wake mwenyewe ulitoboa kichwa chake

wakati mashujaa wake walifurika nje kwa kishindo kututawanya,

wakifurahi kama walio karibu kutafuna

wale wanyonge waliokuwa mafichoni.

153:15 Ay 9:8; Kut 15:8Ulikanyaga bahari kwa farasi wako,

ukisukasuka maji makuu.

163:16 Ay 4:14; Za 37:7Nilisikia na moyo wangu ukagonga kwa nguvu,

midomo yangu ikatetemeka kwa hofu niliposikia sauti;

uchakavu ukanyemelea mifupa yangu,

na miguu yangu ikatetemeka.

Hata hivyo nitasubiri kwa uvumilivu siku ya maafa

kuyajilia mataifa yaliyotuvamia.

173:17 Yoe 1:10-18; 2Kor 4:8, 9; Yer 5:17Ingawa mtini hauchanui maua

na hakuna zabibu juu ya mizabibu,

ingawaje mzeituni hauzai,

na hata mashamba hayatoi chakula,

iwapo hakuna kondoo katika banda,

wala ngʼombe katika zizi,

183:18 Za 42:5; 97:12; Isa 61:10; Kut 15:2; Lk 1:47; Flp 4:4hata hivyo nitashangilia katika Bwana,

nitamfurahia Mungu Mwokozi wangu.

193:19 Kum 32:13; 33:29; Za 27:1; 46:1-5; 18:33Bwana Mwenyezi ni nguvu yangu;

huifanya miguu yangu kama miguu ya ayala,

huniwezesha kupita juu ya vilima.

Kwa kiongozi wa uimbaji. Kwa vinanda vyangu vya nyuzi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 3:1-19

Pemphero la Habakuku

1Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

2Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;

Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.

Muzichitenso masiku athu ano,

masiku athu ano zidziwike;

mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

3Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,

Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.

Sela

Ulemerero wake unaphimba mlengalenga

ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.

4Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;

kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,

mʼmene anabisamo mphamvu zake.

5Patsogolo pake pankagwa mliri;

nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.

6Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;

anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.

Mapiri okhazikika anagumuka

ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.

Njira zake ndi zachikhalire.

7Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,

mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

8Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?

Kodi munakalipira timitsinje?

Kodi munapsera mtima nyanja

pamene munakwera pa akavalo anu

ndiponso magaleta anu achipulumutso?

9Munasolola uta wanu mʼchimake,

munayitanitsa mivi yambiri.

Sela

Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;

10mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.

Madzi amphamvu anasefukira;

nyanja yozama inakokoma

ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,

pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,

pa kunyezimira kwa mkondo wanu.

12Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,

ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.

13Munapita kukalanditsa anthu anu,

kukapulumutsa wodzozedwa wanu.

Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,

munawononga anthu ake onse.

Sela

14Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake

pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,

ankasangalala ngati kuti akudzawononga

osauka amene akubisala.

15Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,

kuvundula madzi amphamvu.

16Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,

milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;

mafupa anga anaguluka,

ndipo mawondo anga anawombana.

Komabe ndikuyembekezera mofatsa,

tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.

17Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,

ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.

Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,

ndipo mʼminda musatuluke kanthu.

Ngakhale nkhosa

ndi ngʼombe zithe mʼkhola,

18komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;

amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,

amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.