Ayubu 32 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 32:1-22

Sehemu Ya Tatu: Mazungumzo Ya Elihu

(Ayubu 32–37)

Elihu Awakemea Rafiki Za Ayubu

132:1 Ay 2:3; 10:7Basi watu hawa watatu wakaacha kumjibu Ayubu, kwa kuwa alikuwa mwadilifu machoni pake mwenyewe. 232:2 Mwa 22:21; Ay 13:19; 35:2Lakini Elihu mwana wa Barakeli, wa kabila la Buzi wa jamaa ya Ramu, akamkasirikia sana Ayubu, kwa sababu ya kujihesabia haki mwenyewe badala ya Mungu. 332:3 Ay 42:7; 32:12-13; 15:13Pia aliwakasirikia hao rafiki watatu wa Ayubu, kwa sababu hawakuweza kupata njia ya kuthibitisha ya kuwa hayo maneno ya Ayubu hayakuwa ya kweli, nao bado walikuwa wamemlaumu. 432:4 Law 19:32Basi Elihu alikuwa amesubiri kwanza waongee na Ayubu kwa sababu walikuwa na umri mkubwa kumliko yeye. 5Lakini alipoona watu hao watatu hawakuwa na kitu zaidi cha kusema, hasira yake ikaamka.

632:6 Ay 15:10Basi Elihu mwana wa Barakeli wa kabila la Buzi akasema:

“Mimi ni mdogo kwa umri,

nanyi ni wazee;

ndiyo sababu niliogopa,

sikuthubutu kuwaambia kile ninachojua.

732:7 1Nya 29:15; 2Nya 10:6Nilifikiri, ‘Yafaa umri useme,

nao wingi wa miaka ungefundisha hekima.’

832:8 Ay 27:3; 33:4; Mit 2:6; 1Fal 3:9Lakini ni Roho iliyoko ndani ya mwanadamu,

pumzi ya Mwenyezi, ndiyo impayo yeye ufahamu.

932:9 1Kor 1:21-26Sio wazee peke yao walio na hekima,

sio wenye umri mkubwa peke yao wanaofahamu lililo sawa.

1032:10 Ay 33:1; 31:33; Za 34:11; Ay 5:27“Kwa hiyo nasema: Nisikilizeni mimi;

mimi nami nitawaambia lile ninalojua.

11Nilingojea mlipokuwa mnaongea,

nilizisikiliza hoja zenu;

mlipokuwa mkitafuta maneno ya kusema,

1232:12 Ay 32:3niliwasikiliza kwa makini.

Lakini hakuna hata mmoja wenu

aliyethibitisha kwamba Ayubu amekosa;

hakuna hata mmoja wenu

aliyeweza kujibu hoja zake.

1332:13 Mhu 9:11; Yer 9:23Msiseme, ‘Tumepata hekima;

Mungu na amthibitishe kuwa mwongo,

wala si mwanadamu.’

1432:14 Ay 23:4Lakini Ayubu hajayapanga maneno yake dhidi yangu,

nami sitamjibu kwa kutumia hoja zenu.

1532:15 Ay 32:1“Wametiwa hofu na hawana la zaidi la kusema;

maneno yamewaishia.

16Je, ningoje sasa kwa sababu wamekuwa kimya,

kwa vile sasa wanasimama bila kuwa na la kujibu?

1732:17 Ay 5:27; 33:3; 36:4Mimi nami nitakuwa na la kusema;

mimi nami nitasema lile nilijualo.

1832:18 Mdo 4:20; 1Kor 9:16; 2Kor 5:14Kwa kuwa nimejawa na maneno,

nayo Roho iliyomo ndani yangu yanisukuma;

1932:19 Yer 20:9; Amo 3:8; Mt 9:17ndani yangu niko kama chupa iliyojazwa divai,

kama kiriba kipya cha divai kilicho tayari kupasuka.

2032:20 Ay 4:2; Yer 6:11Ni lazima niseme ili niweze kutulia;

ni lazima nifumbue midomo yangu nipate kujibu.

2132:21 Law 19:15; 2Nya 19:7; Mt 22:16Sitampendelea mtu yeyote,

wala sitajipendekeza kwa mtu yeyote;

2232:22 Ay 4:17; 9:9; Za 12:2-4kwa kuwa kama ningekuwa stadi wa kujipendekeza,

Muumba wangu angeniondolea mbali kwa upesi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 32:1-22

Mawu a Elihu

1Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. 2Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. 3Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. 4Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. 5Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

6Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,

inuyo ndinu akuluakulu,

nʼchifukwa chake ndimaopa,

ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.

7Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;

anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’

8Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,

mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.

9Si okalamba amene ali ndi nzeru,

si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;

inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’

11Ndadikira nthawi yonseyi,

ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,

pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,

12ineyo ndinakumvetseranidi.

Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;

palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.

13Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;

Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’

14Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,

ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;

mawu awathera.

16Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,

pakuti angoyima phee wopanda yankho?

17Inenso ndiyankhulapo tsopano;

nanenso ndinena zimene ndikudziwa.

18Pakuti ndili nawo mawu ambiri,

ndipo mtima wanga ukundikakamiza;

19mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,

ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.

20Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;

ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.

21Sindidzakondera munthu wina aliyense,

kapena kuyankhula zoshashalika,

22pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,

Mlengi wanga akanandilanga msanga.”