ኢሳይያስ 59 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 59:1-21

ኀጢአት፣ ንስሓና መቤዠት

1እነሆ፤ የእግዚአብሔር እጅ ከማዳን አላጠረችም፤

ጆሮውም መስማት አልተሳናትም።

2ነገር ግን በደላችሁ

ከአምላካችሁ ለይቷችኋል፤

ኀጢአታችሁ ፊቱን ከእናንተ ሰውሮታል፤

በዚህም ምክንያት አይሰማም።

3እጆቻችሁ በደም፣

ጣቶቻችሁ በበደል ተነክረዋል፤

ከንፈሮቻችሁ ሐሰትን ተናገሩ፤

ምላሶቻችሁ ክፉ ነገርን አሰሙ።

4ፍትሕን የሚጠራ ማንም የለም፤

ጕዳዩን በቅንነት የሚያቀርብ የለም፤

በከንቱ ነገር ታመኑ፤ ሐሰትን ተናገሩ፤

ሁከትን ፀነሱ፤ ክፋትንም ወለዱ።

5የእባብ ዕንቍላል ታቀፉ፤

የሸረሪት ድር ዐደሩ፤

ዕንቍላሎቻቸውን የሚበላ ሁሉ ይሞታል፤

አንዱ በተሰበረ ጊዜም እፉኝት ይወጣል።

6ድሮቻቸው ልብስ አይሆኑም፤

በሚሠሩትም ሰውነታቸውን መሸፈን አይችሉም፤

ሥራቸው ክፉ ነው፤

እጃቸውም በዐመፅ ሥራ የተሞላ ነው።

7እግሮቻቸው ወደ ኀጢአት ይሮጣሉ፤

ንጹሕ ደም ለማፍሰስ ይፈጥናሉ፤

የሚያስቡት ክፉ ሐሳብ ነው፤

ማጥፋትና ማፈራረስም የመንገዳቸው ምልክት ነው።

8የሰላምን መንገድ አያውቁም፤

በጐዳናቸውም ፍትሕ የለም፤

መንገዳቸውን ጠማማ አድርገውታል፤

በዚያም የሚሄድ ሰላም አያገኝም።

9ስለዚህ ፍትሕ ከእኛ ርቋል፤

ጽድቅም ወደ እኛ አይመጣም፤

ብርሃንን ፈለግን፤ ነገር ግን ሁሉ ጨለማ ነው፤

የብርሃንን ጸዳል ፈለግን፤ የምንሄደው ግን በድንግዝግዝታ ነው።

10በቅጥሩ ላይ እንደ ዕውር ተደናበርን፤

አካሄዳችንም ዐይን እንደሌላቸው በዳበሳ ሆነ፤

ጀንበር በምትጠልቅበት ጊዜ እንደሚሆነው በእኩለ ቀን ተደናበርን፤

በብርቱዎች መካከልም እንደ ሙታን ሆንን።

11ሁላችን እንደ ድቦች እናላዝናለን፤

እንደ ርግቦችም በመቃተት እንጮኻለን፤

ፍትሕን ፈለግን፤ ግን አላገኘንም፤

ትድግናን ፈለግን፤ ነገር ግን ከእኛ ርቋል።

12በደላችን በፊትህ በዝቷል፤

ኀጢአታችን መስክሮብናል፤

በደላችን ከእኛ አልተለየም፤

ዐመፀኝነታችንንም እናውቃለን።

13በእግዚአብሔር ላይ ዐምፀናል፤ ሐሰት ተናግረናል፤

አምላካችንን ከመከተል ዘወር ብለናል፤

ዐመፃንና ግፍን አውርተናል፤

ልባችን የፀነሰውን ውሸት ተናግረናል።

14ስለዚህ ፍትሕ ከእኛ ርቋል፤

ጽድቅም በሩቁ ቆሟል፤

እውነት በመንገድ ላይ ተሰናክሏል፤

ቅንነትም መግባት አልቻለም።

15እውነት የትም ቦታ አይገኝም፤

ከክፋት የሚርቅ ለጥቃት የተጋለጠ ነው።

እግዚአብሔር ተመለከተ፤

ፍትሕ በመታጣቱም ዐዘነ።

16ማንም እንደሌለ አየ፤

ወደ እርሱ የሚማልድ ባለመኖሩ ተገረመ፤

ስለዚህ የገዛ ክንዱ ድነት አመጣለት፤

የራሱም ጽድቅ ደግፎ ያዘው።

17ጽድቅን እንደ ጥሩር አጠለቀ፤

የድነትን ቍር በራሱ ላይ ደፋ፤

የበቀልንም ልብስ ለበሰ፤

መጐናጸፊያ እንደሚደረብም ቅናትን ደረበ።

18እንደ ሥራቸው መጠን፣

ቍጣን ለባላጋራዎቹ፣

ፍዳን ለጠላቶቹ፣

እንደዚሁ ይከፍላቸዋል፤

ለደሴቶችም የእጃቸውን ይሰጣቸዋል።

19በምዕራብ ያሉት የእግዚአብሔርን ስም ይፈራሉ፤

በፀሓይ መውጫ ያሉት ለክብሩ ይገዛሉ፤

የእግዚአብሔር እስትንፋስ እንደ ተቋተ፣

እንደ ተከማቸም ጐርፍ ይመጣልና።59፥19 ወይም፣ ጠላት እንደ ጐርፍ በሚመጣበት ጊዜ/የእግዚአብሔር መንፈስ በውጊያ ያዋርደዋል

20“አዳኝ ወደ ጽዮን፣

ኀጢአታቸውንም ወደ ተናዘዙት ወደ ያዕቆብ ቤት ይመጣል”

ይላል እግዚአብሔር።

21“በእኔ በኩል፣ ከእነርሱ ጋር ያለኝ ቃል ኪዳን ይህ ነው” ይላል እግዚአብሔር፤ “በአንተም ላይ ያለው መንፈሴ፣ በአፍህ ያስቀመጥሁት ቃሌ ከአፍህ፣ ከልጆችህ አፍ፣ ከዘር ዘሮቻቸውም አፍ ከዛሬ ጀምሮ እስከ ዘላለም አይለይም” ይላል እግዚአብሔር

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 59:1-21

Tchimo, Kuvomereza ndi Chipulumutso

1Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa,

kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.

2Koma zoyipa zanu zakulekanitsani

ndi Mulungu wanu;

ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu,

kotero Iye sadzamva.

3Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi.

Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu.

Pakamwa panu payankhula zabodza,

ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.

4Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama,

palibe amene akupita ku mlandu moona mtima.

Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza;

amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.

5Iwo amayikira mazira a mamba

ndipo amaluka ukonde wakangawude.

Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa,

ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.

6Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala;

ndipo chimene apangacho sangachifunde.

Ntchito zawo ndi zoyipa,

ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.

7Amathamangira kukachita zoyipa;

sachedwa kupha anthu osalakwa.

Maganizo awo ndi maganizo oyipa;

kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.

8Iwo sadziwa kuchita za mtendere;

zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo.

Njira zawo zonse nʼzokhotakhota;

aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.

9Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;

ndipo chipulumutso sichitifikira.

Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;

tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.

10Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,

kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.

Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;

timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.

11Tonse timabangula ngati zimbalangondo:

Timalira modandaula ngati nkhunda.

Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.

Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”

12Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,

ndipo machimo athu akutsutsana nafe.

Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse

ndipo tikuvomereza machimo athu:

13Tawukira ndi kumukana Yehova.

Tafulatira Mulungu wathu,

pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,

ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.

14Motero kuweruza kolungama kwalekeka

ndipo choonadi chili kutali ndi ife;

kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,

ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.

15Choonadi sichikupezeka kumeneko,

ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.

Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa

kuti panalibe chiweruzo cholungama.

16Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe,

Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera;

Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza,

ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;

17Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa,

ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso;

anavala kulipsira ngati chovala

ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.

18Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake

molingana ndi zimene anachita,

adzaonetsa ukali kwa adani ake

ndi kubwezera chilango odana naye.

Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.

19Choncho akadzabwera ngati madzi

oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho.

Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa

adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.

20“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni

kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,”

akutero Yehova.

21Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,”

akutero Yehova.