መዝሙር 61 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 61:1-8

መዝሙር 61

የግዞተኛ ጸሎት

ለመዘምራን አለቃ፤ በበገናዎች የሚዘመር፤ የዳዊት መዝሙር።

1እግዚአብሔር ሆይ፤ ጩኸቴን ስማ፤

ጸሎቴንም አድምጥ።

2ልቤ በዛለ ጊዜ፣

ከምድር ዳርቻ ወደ አንተ እጣራለሁ፤

ከእኔ ይልቅ ከፍ ወዳለው ዐለት ምራኝ።

3አንተ መጠጊያዬ፣

ከጠላትም የምተገንብህ ጽኑ ግንብ ሆነኸኛልና።

4በድንኳንህ ለዘላለም ልኑር፤

በክንፎችህም ጥላ ልከለል። ሴላ

5አምላክ ሆይ፤ ስእለቴን ሰምተሃልና፤

ስምህን የሚፈሩትንም ሰዎች ርስት ለእኔ ሰጠህ።

6የንጉሡን ዕድሜ አርዝምለት፤

ዘመኑንም እስከ ብዙ ትውልድ ጨምርለት፤

7በእግዚአብሔር ፊት ለዘላለም ይንገሥ፤

ይጠብቁት ዘንድ ምሕረትህንና ታማኝነትህን አዘጋጅለት።

8ስለዚህ ለስምህ ዘወትር ውዳሴ አቀርባለሁ፤

ስእለቴንም በየጊዜው እፈጽማለሁ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 61:1-8

Salimo 61

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

1Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;

mvetserani pemphero langa.

2Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu

ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;

tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.

3Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,

nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

4Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya

ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.

5Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;

mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

6Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,

zaka zake kwa mibado yochuluka.

7Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;

ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

8Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu

ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.