አሞጽ 6 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

አሞጽ 6:1-14

ተዘልላ ላለችው እስራኤል የተሰጠ ማስጠንቀቂያ

1በጽዮን ተዘልላችሁ የምትቀመጡ፣

በሰማርያ ተራራ ያለ ሥጋት የምትኖሩ፣

የእስራኤልም ሕዝብ ለርዳታ ወደ እናንተ የሚመጡባችሁ፣

እናንት የአሕዛብ አለቆች ሆይ፤ ወዮላችሁ!

2ወደ ካልኔ ሂዱ፤ እርሱንም ተመልከቱ፤

ከዚያም ወደ ታላቂቱ ሐማት ሂዱ፤

ወደ ፍልስጥኤም ከተማ ወደ ጌትም ውረዱ፤

እነዚህ ከሁለቱ መንግሥታታችሁ ይሻላሉን?

የምድራቸውስ ስፋት ከእናንተ ይበልጣልን?

3ክፉውን ቀን ለምታርቁ፣

የግፍንም ወንበር ለምታቀርቡ ወዮላችሁ!

4በዝኆን ጥርስ ባጌጠ ዐልጋ ላይ ለምትተኙ፤

በድንክ ዐልጋችሁ ላይ ለምትዝናኑ፣

ከበጎች መንጋ ጠቦትን፣

ከጋጣም ጥጃን ለምትበሉ፤

5ባልተቃኘ በገና ለምትዘፍኑ፣

በሙዚቃ መሣሪያ ለመጫወት ለምትሹ፣

6በፋጋ የወይን ጠጅ ለምትጠጡ፣

ምርጥ ሽቱም ለምትቀቡ፣

ስለ ዮሴፍ መከራ ግን ለማታዝኑ ወዮላችሁ!

7ስለዚህ እናንተ በመጀመሪያ በምርኮ ከሚወሰዱት መካከል ናችሁ፤

መፈንጠዛችሁና መዝናናታችሁም ያበቃል።

እግዚአብሔር የእስራኤልን ትዕቢት ይጸየፋል

8ጌታ እግዚአብሔር

“የያዕቆብን ትዕቢት ተጸይፌአለሁ፤

ምሽጎቹንም ጠልቻለሁ፤

ከተማዪቱንና በውስጧ ያለውን ሁሉ፣

አሳልፌ እሰጣለሁ”

ሲል በራሱ ምሏል፤ ይላል የሰራዊት አምላክ እግዚአብሔር

9በአንድ ቤት ውስጥ ዐሥር ሰዎች ቢቀሩ እነርሱም ይሞታሉ። 10በድኖቹንም ከቤት አውጥቶ ማቃጠል ያለበት አንድ ዘመድ መጥቶ ተደብቆ ያለውን ሰው፣ “ከአንተ ጋር የቀረ ሌላ ሰው አለን?” ሲለው፣ እርሱም “የለም” ይለዋል፤ ከዚያም በኋላ፣ “ዝም በል፤ የእግዚአብሔርን ስም መጥራት አይገባንም” ይለዋል።

11እነሆ፤ እግዚአብሔር ትእዛዝ ሰጥቷልና፤

ታላላቅ ቤቶችን ያወድማቸዋል፤

ትንንሾቹንም ያደቅቃቸዋል።

12ፈረሶች በጭንጫ ላይ ይሮጣሉን?

ሰውስ እዚያ ላይ በበሬ ያርሳልን?

እናንተ ግን ፍትሕን ወደ መርዝነት፣

የጽድቅንም ፍሬ ወደ መራራነት ለወጣችሁ።

13እናንተ ሎዶባርን6፥13 ትርጕሙ ምንም ማለት ነው። በማሸነፋችሁ ደስ ያላችሁ፣

“ቃርናይምን6፥13 ቃርናይም ትርጕሙ ቀንዶች ማለት ነው፤ ቀንድ የጥንካሬ ምልክት ነው። በራሳችን ብርታት ይዘናል” የምትሉ።

14ሁሉን የሚገዛ አምላክ እግዚአብሔር እንዲህ ይላልና፣

“የእስራኤል ሕዝብ ሆይ፤ እነሆ፤ እኔ ከሐማት መግቢያ6፥14 ወይም ከመግቢያው ጀምሮ እስከ ዓረባ ሸለቆ ድረስ፣

የሚያስጨንቃችሁን ሕዝብ፣ በእናንተ

ላይ አስነሣለሁ።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 6:1-14

Tsoka kwa Osalabadira Kanthu

1Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,

ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,

inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,

kumene Aisraeli amafikako!

2Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;

mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,

ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.

Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?

Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?

3Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,

zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.

4Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,

mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.

Mumadya ana ankhosa onona

ndi ana angʼombe onenepa.

5Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka

nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.

6Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza

ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,

koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.

7Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;

maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.

Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli

8Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,

“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,

ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;

Ine ndidzawupereka mzindawu

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”

9Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu. 10Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”

11Pakuti Yehova walamula kuti

nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula,

ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.

12Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?

Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja?

Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha

ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.

13Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara

ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”

14Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,

“Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu

umene udzakuzunzani

kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”