Zabbuli 34 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 34:1-22

Zabbuli 34

Ya Dawudi. Bwe yeefuula okuba omugu w’eddalu mu maaso ga Abimereki, oluvannyuma eyamugoba, era naye n’amuviira.

1Nnaagulumizanga Mukama buli kiseera,

akamwa kange kanaamutenderezanga bulijjo.

2Omwoyo gwange guneenyumiririzanga mu Mukama;

ababonyaabonyezebwa bawulire bajaguzenga.

3Kale tutendereze Mukama,

ffenna tugulumizenga erinnya lye.

4Nanoonya Mukama, n’annyanukula;

n’ammalamu okutya kwonna.

5Abamwesiga banajjulanga essanyu,

era tebaaswalenga.

6Omunaku ono yakoowoola Mukama n’amwanukula,

n’amumalako ebyali bimuteganya byonna.

7Malayika wa Mukama yeebungulula abo abatya Mukama,

n’abawonya.

8Mulegeeko mulabe nga Mukama bw’ali omulungi!

Balina omukisa abaddukira gy’ali.

9Musseemu Mukama ekitiibwa mmwe abatukuvu be,

kubanga abamutya tebaajulenga.

10Empologoma zirumwa enjala ne ziggwaamu amaanyi;

naye abo abanoonya Mukama, ebirungi tebiibaggwengako.

11Mujje wano baana bange, mumpulirize;

mbayigirize okutya Mukama.

12Oyagala okuwangaala mu bulamu obulungi,

okuba mu ssanyu emyaka emingi?

13Olulimi lwo lukuumenga luleme okwogera ebitasaana,

n’akamwa ko kaleme okwogera eby’obulimba.

14Lekeraawo okukola ebibi, okolenga ebirungi;

noonya emirembe era ogigobererenga.

15Amaaso ga Mukama gatunuulira abo abatuukirivu,

n’amatu ge gawulira okukaaba kwabwe.

16Mukama amaliridde okumalawo abakola ebibi,

okubasaanyizaawo ddala n’obutaddayo kujjukirwa ku nsi.

17Abatuukirivu bakoowoola Mukama n’abawulira

n’abawonya mu byonna ebiba bibateganya.

18Mukama abeera kumpi n’abalina emitima egimenyese, era alokola abo abalina emyoyo egyennyise.

19Omuntu omutuukirivu ayinza n’okuba n’ebizibu bingi,

naye byonna Mukama abimuyisaamu.

20Amagumba ge gonna Mukama agakuuma,

ne watabaawo na limu limenyeka.

21Ekibi kiritta abakola ebibi,

n’abalabe b’abatuukirivu balibonerezebwa.

22Mukama anunula abaweereza be;

so tewali n’omu ku abo abaddukira gy’ali alibonerezebwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 34:1-22

Salimo 34

Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.

1Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;

matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.

2Moyo wanga udzanyadira Yehova;

anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.

3Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;

tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

4Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;

anandilanditsa ku mantha anga onse.

5Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;

nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.

6Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;

Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.

7Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye

ndi kuwalanditsa.

8Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;

wodala munthu amene amathawira kwa Iye.

9Wopani Yehova inu oyera mtima ake,

pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.

10Mikango itha kulefuka ndi kumva njala

koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.

11Bwerani ana anga, mundimvere;

ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.

12Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake

ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,

13asunge lilime lake ku zoyipa

ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.

14Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

funafuna mtendere ndi kuwulondola.

15Maso a Yehova ali pa olungama

ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;

16nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,

kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.

17Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;

Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.

18Yehova ali pafupi kwa osweka mtima

ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.

19Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,

Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,

20Iye amateteza mafupa ake onse,

palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.

21Choyipa chidzapha anthu oyipa;

adani a olungama adzapezeka olakwa.

22Yehova amawombola atumiki ake;

aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.