Yobu 34 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Yobu 34:1-37

1Awo Eriku ne yeeyongera okwogera nti,

2“Muwulire ebigambo byange, mmwe abasajja ab’amagezi;

mumpulirize mmwe abayivu.

3Kubanga okutu kugezesa ebigambo

ng’olulimi bwe lugezesa emmere.

4Leka twesalirewo ekituufu;

muleke tulondewo ekisaanidde.

5“Yobu agamba nti, ‘Siriiko musango,

naye Katonda agaanye okusala omusango gwange mu mazima.

6Wadde nga ndi mutuufu,

ntwalibwa okuba omulimba,

wadde nga siriiko musango,

akasaale ke kanteseeko ekiwundu ekitawonyezeka.’

7Musajja ki ali nga Yobu,

anywa okunyoomebwa ng’anywa amazzi?

8Atambula n’abakozi b’ebibi,

mukwano gw’abo abakola ebitali bya butuukirivu.

9Kubanga agambye nti, ‘Omuntu talina kyaganyulwa

bw’agezaako okusanyusa Katonda.’

10Noolwekyo mumpulirize mmwe abasajja abalina okutegeera.

Kikafuuwe Katonda okukola ebibi,

wadde Ayinzabyonna okukola ebikyamu.

11Asasula omuntu olw’ekyo ky’aba akoze;

n’amutuusaako ebyo ebimusaanidde olw’empisa ze.

12Weewaawo amazima gali nti, Katonda tasobya.

Ayinzabyonna tasaliriza musango.

13Obuyinza yabuggya eri ani okukulembera ensi?

Ani eyamuwa olukusa okufuga ensi yonna?

14Singa asalawo n’atwala omwoyo gw’omuntu

awamu n’omukka gwe,

15abantu bonna bandizikiriridde wamu,

era omuntu yandizzeeyo mu nfuufu.

16“Bw’oba olina okutegeera, wuliriza kino;

wuliriza kye ŋŋamba.

17Oyo atayagala bwenkanya asobola okufuga?

Onoosalira abatuukirivu n’oyo ow’amaanyi omusango?

18Oyo si ye agamba bakabaka nti, ‘Tolina mugaso,’

n’abakungu nti, ‘Oli mukozi wa bibi,’

19atattira balangira ku liiso

era nga tafa ku bagagga kusinga bw’afa ku baavu,

kubanga egyo gye mirimu gy’emikono gye?

20Mu kaseera buseera baba bafiiridde wakati mu ttumbi.

Abantu banyeenyezebwa ne baggyibwawo.

Abo ab’amaanyi batwalibwa n’omukono ogutali gw’abantu.

21“Amaaso ge gatunuulira amakubo g’abantu;

atunuulira buli kigere kye batambula.

22Teri kifo kikwafu wadde ekisiikirize eky’amaanyi,

ababi gye bayinza okwekweka.

23Katonda teyeetaaga kwongera kwekebejja bantu

okulabika mu maaso ge okusalirwa omusango.

24Awatali kwebuuza ku muntu yenna, amenyaamenya ab’amaanyi

n’ateekawo abalala mu kifo kyabwe.

25Olw’okubanga amanyi ebikolwa byabwe,

abamalamu amaanyi ekiro ne babetentebwa.

26Ababonereza olw’ebikolwa byabwe ebibi

abantu bonna nga balaba,

27kubanga baamuvaako ne balekeraawo okumugoberera

ne bataddayo kufaayo n’akatono ku makubo ge gonna.

28Baleetera abaavu okukaaba, ne kumutuukako

era n’awulira okukaaba kw’abanyigirizibwa.

29Naye bw’asalawo obutabaako ky’ayogera, ani ayinza okumunenya?

Bwakweka amaaso ge ani ayinza okumulaba?

Eggwanga n’omuntu abalinako obuyinza bwe bumu;

30aziyiza omuntu atatya Katonda okufuga,

aleme okutega abantu emitego.

31“Singa omuntu agamba Katonda nti,

gunsinze, sikyaddayo kwonoona,

32kye sitegeera kinjigirize,

bwe mba nga nsobezza sikyaddayo kukikola,

33olwo Katonda akuddemu nga bw’oyagala,

akuleke ng’ogaanye okwenenya?

Kaakano ggwe olina okusalawo, so sinze;

noolwekyo mbuulira ggwe ky’omanyi.

34“Abantu abalina okutegeera mumbuulire,

abasajja abagezi abawulira muntegeeze,

35‘Yobu ayogeza butamanya

ebigambo bye tebiriimu kwolesebwa.’

36Singa Yobu agezesebbwa okutuusa ku nkomerero,

olw’okwogera ng’abasajja abakozi b’ebibi!

37Kubanga ku kibi kye ayongeddeko obujeemu,

n’akuba mu ngalo wakati mu ffe,

n’ayongera okwogera ng’awakanya Katonda.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 34:1-37

1Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,

2“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;

tcherani khutu inu anthu ophunzira.

3Pakuti khutu limayesa mawu

monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.

4Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;

tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.

5“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,

koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.

6Ngakhale ndine wolungama mtima,

akundiyesa wabodza;

ngakhale ndine wosachimwa,

mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’

7Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,

amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?

8Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;

amayanjana ndi anthu oyipa mtima.

9Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu

poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’

10“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.

Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe,

Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.

11Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;

Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.

12Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,

kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.

13Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?

Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?

14Mulungu akanakhala ndi maganizo

oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,

15zamoyo zonse zikanawonongekeratu

ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.

16“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;

mvetserani zimene ndikunena.

17Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?

Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?

18Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’

ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’

19Iye sakondera akalonga

ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka,

pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?

20Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;

anthu amachita mantha ndipo amamwalira;

munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.

21“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;

amaona mayendedwe ake onse.

22Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani

kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.

23Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,

kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.

24Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu

ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.

25Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo

amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.

26Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,

pamalo pamene aliyense akuwaona;

27Chifukwa anasiya kumutsata

ndipo sasamaliranso njira zake zonse.

28Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,

kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.

29Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?

Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe?

Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,

30kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,

kuti asatchere anthu misampha.

31“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,

‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,

32ndiphunzitseni zimene sindikuziona

ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’

33Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,

pamene inu mukukana kulapa?

Chisankho nʼchanu, osati changa;

tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.

34“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,

anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,

35‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;

mawu ake ndi opanda fundo.’

36Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto

chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!

37Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;

amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu,

ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”