Yobu 26 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Yobu 26:1-14

Yobu Ayanukula

1Awo Yobu n’addamu nti,

2“Ng’oyambye oyo atalina maanyi!

Ng’oyambye omukono ogwo ogutalina maanyi!

3Ng’amagezi ga kitalo ago g’owadde oyo atalina magezi!

Ng’owadde okuluŋŋamizibwa okuyitirivu!

4Ani akuyambye okwogera ebigambo ebyo?

Era mwoyo ki ogwogeredde mu kamwa ko?

5“Abafu kye balimu tekigumiikirizika,

n’abo abali wansi w’amazzi ne bonna abagabeeramu.

6Amagombe gali bwereere mu maaso ga Katonda;

n’okuzikiriza tekulina kikubisse.

7Ayanjuluza eggulu ery’obukiikakkono mu bbanga ejjereere,

awanika ensi awatali kigiwanirira.

8Asiba amazzi mu bire bye;

ate ebire tebyabika olw’okuzitoowererwa.

9Abikka obwenyi bw’omwezi,

agwanjululizaako ebire bye.

10Ateekawo ekipimo ekiraga waggulu amazzi g’ennyanja we gayita,

ng’ensalo eyawula ekitangaala n’ekizikiza.

11Empagi z’eggulu zikankana,

zeewuunya olw’okunenya kwe.

12Afuukuula ennyanja n’obuyinza bwe,

n’asalaasala Lakabu mu bitundutundu n’amagezi ge.

13Yafuuwa omukka ogwatereeza eggulu,

omukono gwe gwafumita omusota oguwulukuka.

14Naye nga bino katundu butundu ku bye yakola.

Nga kye tumuwulirako katundu butundu ku ekyo ky’ali!

Ani ayinza okutegeera okubwatuka kw’obuyinza bwe?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 26:1-14

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu!

Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!

3Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru!

Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!

4Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa?

Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?

5“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi,

ndi zonse zokhala mʼmadzimo.

6Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu;

chiwonongeko ndi chosaphimbidwa.

7Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho;

Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.

8Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake,

koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.

9Iye amaphimba mwezi wowala,

amawuphimba ndi mitambo yake.

10Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta,

kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.

11Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera,

ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.

12Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja;

ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.

13Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga,

dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.

14Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake;

tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona!

Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”