Isaaya 54 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 54:1-17

Ekitiibwa Kya Sayuuni eky’Oluvannyuma

1“Yimba ggwe omugumba

atazaalanga;

tandika okuyimbira mu ddoboozi ery’omwanguka osanyukire ddala

ggwe atalumwanga kuzaala.

Kubanga ggwe eyalekebwa

ojja kuba n’abaana bangi okusinga oyo akyalina bba,”

bw’ayogera Mukama.

2“Gaziya weema yo, owanvuye emiguwa gyayo,

tokwata mpola;

nyweza enkondo zo.

3Kubanga olisaasaanira

ku mukono gwo ogwa ddyo

era n’ogwa kkono,

n’ezzadde lyo lirirya amawanga,

era abantu bo balituula mu bibuga ebyalekebwa awo ebyereere.

4“Totya kubanga toliddayo kukwatibwa nsonyi.

Toggwaamu maanyi kubanga togenda kuswazibwa.

Olyerabira ensonyi z’obuvubuka bwo,

n’ekivume ky’obwannamwandu bwo tolikijjukira nate.

5Kubanga Omutonzi wo ye balo,

Mukama Katonda ow’Eggye lye linnya lye.

Omutukuvu wa Isirayiri ye Mununuzi wo,

Katonda ow’ensi yonna, bw’ayitibwa.

6Kubanga Mukama Katonda yakuyita okomewo,

ng’omukazi eyali alekeddwawo ng’alina ennaku ku mutima;

omukazi eyafumbirwa ng’akyali muto, n’alekebwawo,”

bw’ayogera Katonda wo.

7“Nakulekako akaseera katono nnyo;

naye ndikukuŋŋaanya n’okusaasira okungi.

8Obusungu obubuubuuka bwe bwankwata

nakweka amaaso gange okumala ekiseera,

naye ndikukwatirwa ekisa n’okwagala okutaliggwaawo,”

bw’ayogera Mukama Katonda,

Omununuzi wo.

9“Kubanga gye ndi,

bino biri nga bwe byali mu biseera bya Nuuwa.

Nga bwe nalayira nti amazzi ga Nuuwa tegagenda kuddamu kulabikako ku nsi,

bwe ntyo ndayira nti siriddayo kukusunguwalira wadde okukunenya.

10Kubanga ensozi ziyinza okuvaawo n’obusozi okuggyibwawo

naye okwagala kwange okutaggwaawo tekulisagaasagana

so n’endagaano yange ey’emirembe

teriggyibwawo,”

bw’ayogera Mukama Katonda akusaasira.

Yerusaalemi eky’Ebiro Ebijja

11Mukama agamba nti,

“Ggwe Yerusaalemi ekibuga ekibonyaabonyezebwa, ekisuukundibwa emiyaga awatali kulaba ku mirembe;

laba ndikuzimba buto n’amayinja ag’amabala amalungi,

emisingi gyo ne gizimbibwa ne safiro.

12Ebitikkiro byo ndibikola n’amayinja amatwakaavu,

n’emiryango gyo ne ngikola ne kabunkulo,

ne bbugwe yenna ne mwetoolooza amayinja ag’omuwendo.

13N’abaana bo bonna baliyigirizibwa Mukama;

n’emirembe gy’abaana bo giriba mingi.

14Olinywezebwa mu butuukirivu

era toojoogebwenga,

kubanga tolitya,

onoobanga wala n’entiisa kubanga terikusemberera.

15Omuntu yenna bwakulumbanga kiriba tekivudde gye ndi.

Buli anaakulumbanga anaawangulwanga ku lulwo.

16Laba nze natonda omuweesi,

awujja amanda agaliko omuliro

n’aweesa ekyokulwanyisa olw’omugaso gwakyo.

Era nze natonda abazikiriza abakozesa ekyokulwanyisa okumalawo obulamu.

17Naye teri kyakulwanyisa kye baliweesa ekirikwolekera ne kikusobola,

era oliwangula buli lulimi olulikuvunaana era oluwoza naawe.

Guno gwe mugabo gw’abaddu ba Mukama,

n’obutuukirivu bwabwe obuva gye ndi,”

bw’ayogera Mukama.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 54:1-17

Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni

1“Sangalala, iwe mayi wosabala,

iwe amene sunabalepo mwana;

imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,

iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;

chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri

kuposa mkazi wokwatiwa,”

akutero Yehova.

2Kulitsa malo omangapo tenti yako,

tambasula kwambiri nsalu zake,

usaleke;

talikitsa zingwe zako,

limbitsa zikhomo zako.

3Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;

ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina

ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.

4“Usachite mantha; sadzakunyozanso.

Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.

Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako

ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.

5Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;

dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.

6Yehova wakuyitananso,

uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,

mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”

akutero Mulungu wako.

7“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,

koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.

8Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa

ndili wokwiya kwambiri.

Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,

ndidzakuchitira chifundo,”

akutero Yehova Mpulumutsi wako.

9“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa.

Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi.

Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima,

sindidzakudzudzulaninso.

10Ngakhale mapiri atagwedezeka

ndi zitunda kusunthidwa,

koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha.

Pangano langa lamtendere silidzasintha,”

akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.

11“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza,

Ine ndidzakongoletsa miyala yako.

Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.

12Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi.

Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto,

ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.

13Yehova adzaphunzitsa ana ako onse,

ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.

14Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni:

Sudzakhalanso wopanikizika,

chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse.

Sudzakhalanso ndi mantha

chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.

15Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa;

aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.

16“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo

amene amakoleza moto wamakala

ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito.

Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;

17palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke,

ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa.

Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova.

Chipambano chawo chichokera kwa Ine,”

akutero Yehova.