역대하 3 – KLB & CCL

Korean Living Bible

역대하 3:1-17

솔로몬의 성전 건축

1마침내 성전 건축 공사가 시작되었다. 그 위치는 예루살렘의 모리아산이었다. 이 곳은 여호와께서 솔로몬의 아버지 다윗에게 나타났던 곳으로 여부스 사람 오르난의 타작 마당이었으나 다윗이 성전 부지로 선정한 곳이었다.

2성전 건축 공사가 시작된 날은 솔로몬왕 4년 2월 2일이었다.

3성전 지대는 3:3 히 ‘길 60규빗, 폭 20규빗’길이가 27미터, 폭이 9미터이며

4현관의 폭과 높이는 성전의 폭과 같이 각각 3:4 원문에는 ‘현관의높이 120규빗’ 54미터로되어있다.9미터였고 현관 내부는 순금으로 입혔다.

5성전 본당은 백향목으로 만들고 그 위에 순금을 입혔으며 거기에 종려나무와 사슬 모양의 형상을 새겼다.

6또 아름다운 보석을 벽에 박아 한층 돋보이게 하고 바르와임에서 수입해 온 금으로 성전을 화려하게 장식했는데

7성전 벽 전체와 들보와 문과 문지방을 금으로 입히고, 벽에는 그룹 천사를 아로새겼다.

8그리고 성전 안에 길이와 폭이 다 같이 9미터 되는 지성소를 만들고 순금 3:8 히 ‘600달란트’약 20톤으로 그 벽을 입혔고

9또 금 3:9 히 ‘50세겔’570그램으로 지성소에 쓸 못을 만들었으며 다락도 역시 금으로 입혔다.

10지성소 안에는 조각하여 만든 두 그룹 천사를 금으로 입혀 놓았으며

11-13그 두 그룹 천사는 정면을 향해 서로 나란히 서 있게 하였다. 이 그룹 천사들의 날개는 각각 두 개씩이며 각 날개의 길이는 약 2.3미터였다. 이 날개들은 지성소 중앙에서 한쪽 끝을 서로 맞대고 다른 한쪽 끝은 각각 성전 벽에 닿았는데 두 그룹 천사의 날개가 뻗어 있는 전체 길이는 9미터였다.

14그리고 지성소의 휘장은 청색, 자색, 홍색 실과 고운 베로 만들었으며 그 위에 그룹 천사를 수놓았다.

15성전 정면에는 높이 3:15 원문에는 ‘35규빗’ 곧 16미터로되어있다.8.1미터 되는 두 기둥을 세웠으며 이 기둥에는 약 2.3미터 되는 기둥머리를 씌웠고,

16또 그 기둥머리를 사슬로 장식하여 그 사슬에 놋으로 만든 석류 100개를 달았다.

17이 기둥은 성전 입구 양쪽에 세웠으며 오른쪽에 세운 것을 3:17 ‘하나님이세우신다’ 는뜻.‘야긴’ 이라 부르고 왼쪽에 세운 것을 3:17 ‘그의힘으로’ 라는뜻.‘보아스’ 라고 불렀다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 3:1-17

Solomoni Amanga Nyumba ya Mulungu

1Pamenepo Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu pa Phiri la Moriya, pamene Yehova anaonekera Davide abambo ake. Panali pabwalo lopunthirapo tirigu la Arauna Myebusi, malo amene anapereka Davide. 2Iye anayamba kumanga pa tsiku lachiwiri la mwezi wachiwiri mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake.

3Maziko amene Solomoni anayika pomanga Nyumba ya Mulungu ndi awa: Mulitali munali mamita 27, mulifupi munali mamita asanu ndi anayi (potsata miyeso yakale). 4Chipinda cha polowera mulitali mwake chinali mamita asanu ndi anayi ofanana ndi mulifupi mwake mwa nyumbayo. Msinkhu wake unali mamita 54.

Iye anakuta nyumbayo mʼkati mwake ndi golide woyengeka bwino. 5Chipinda chachikulu, khoma lake anakhomera matabwa a payini ndipo analikutira ndi golide wabwino ndi kulikongoletsa ndi zithunzi za kanjedza ndi maunyolo. 6Iye anakongoletsa Nyumba ya Mulunguyo ndi miyala yokongola. Ndipo golide amene anagwiritsa ntchito anali golide wa ku Paravaimu. 7Iye anakutira ndi golide mitanda ya ku denga, maferemu a zitseko, makoma ndi zitseko za Nyumba ya Mulungu, ndipo anajambula Akerubi mʼmakoma mwake.

8Iye anamanga Malo Opatulika Kwambiri ndipo mulitali mwake munali mofanana ndi mulifupi mwa Nyumba mamita asanu ndi anayi. Anakuta mʼkati mwake ndi golide wosalala wolemera matani makumi awiri. 9Misomali yagolide imalemera magalamu 570. Anakutanso ndi golide zipinda zapamwamba.

10Ku Malo Opatulika Kwambiri iye anapangako Akerubi awiri achitsulo ndipo anawakuta ndi golide. 11Kutalika kwa mapiko onse a Akerubi kunali mamita asanu ndi anayi. Phiko la Kerubi woyamba linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza khoma la Nyumba ya Mulungu, pamene phiko linalo, lotalikanso koposerapo mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi winayo. 12Chimodzimodzinso phiko la Kerubi wachiwiri linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza mbali ina ya khoma la Nyumba ya Mulungu, ndipo linalo limene linalinso loposera mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi woyamba uja. 13Mapiko a Akerubiwa akawatambasula amatalika mamita asanu ndi anayi. Akerubiwa anayimirira pa mapazi awo, kuyangʼana chipinda chachikulu.

14Solomoni anapanga nsalu zotchingira zobiriwira, zapepo ndi zofiira ndi nsalu zofewa zosalala, atajambulapo Akerubi.

15Kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu anamangako zipilala ziwiri, zimene zonse pamodzi zinali zotalika mamita khumi ndi asanu ndi theka; chipilala chilichonse chinali ndi mutu woposera mamita awiri. 16Iye anapanga maunyolo olumikizanalumikizana ndipo anawayika pamwamba pa zipilalazo. Anapanganso makangadza 100 ndipo anawalumikiza ku maunyolo aja. 17Solomoni anayimika nsanamirazo kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu, imodzi mbali ya kummwera ndi inayo mbali ya kumpoto. Nsanamira ya kummwera anayitcha Yakini ndipo ya kumpoto anayitcha Bowazi.