詩篇 6 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 6:1-10

6

1主よ、お願いです。

御怒りのままに私を罰しないでください。

2ああ主よ、あわれんでください。

私は弱い者です。どうかいやしてください。

私は病んでいるのです。

3狼狽し、心がかき乱されています。

不安に駆られ、

気分がすっかりめいっています。

ああ、私を早く元どおりにしてください。

4ああ主よ、帰って来て、私を健康にしてください。

あわれんで、お救いください。

5死んでしまっては、

友の前であなたをほめたたえることもできません。

6痛みのため、私はやせ細りました。

夜ごと涙で枕をぬらします。

7敵のために嘆き、そのために目も衰え、

かすんできました。

8不法を行う者ども、私から離れて行け。

私の泣き声は天に届き、

9訴えも聞き届けられた。

主は私の祈りにすべて答えてくださる。

10敵はみな、恥を見、

恐れにわななき、恥辱を受ける。

神は彼らに恥をかかせて

追い返します。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 6:1-10

Salimo 6

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

kapena kundilanga mu ukali wanu.

2Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka;

Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.

3Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu.

Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?

4Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse;

pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

5Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira;

Amakutamandani ndani ali ku manda?

6Ine ndatopa ndi kubuwula;

usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga;

ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.

7Maso anga atupa chifukwa cha chisoni;

akulephera kuona chifukwa cha adani anga.

8Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa,

pakuti Yehova wamva kulira kwanga.

9Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo;

Yehova walandira pemphero langa.

10Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha;

adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.