Yuda Abwerera kwa Yehova
1Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu. 3Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 4Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova. 5Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya? 6Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu?
“Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’ ”
Munthu Pakati pa Mitengo ya Mchisu
7Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?”
Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?” 13Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni, 15koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’ ”
Nyanga Zinayi ndi Amisiri Azitsulo Anayi
18Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi. 19Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?”
Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi. 21Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?”
Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”
Et kald til folket om at vende om til Gud
1I den ottende måned i kong Dareios1,1 Dareios Hystaspes, konge i Persien fra 522-486 f.Kr. af Persiens andet regeringsår talte Herren til Israels folk gennem profeten Zakarias, der var søn af Berekja og barnebarn af Iddo:
2-4„Hør, hvad jeg, Herren den Almægtige, siger: Hvis I vil vende om og komme til mig, vil jeg komme jer i møde. Vær ikke som jeres forfædre, som jeg var nødt til at straffe hårdt. Jeg advarede dem gennem mine profeter om at vende om fra deres ugudelige levemåde og onde handlinger, men de nægtede at lytte til mig. 5Nu er de alle sammen borte, og profeterne er døde. 6Men det, jeg sagde til dem gennem mine tjenere, profeterne, gik i opfyldelse, og de måtte angrende erkende: ‚Herren straffede os for vores onde levevis og handlinger, akkurat som han sagde, at han ville!’ ”
Herren opmuntrer Israels folk
7Den 24. dag i den 11. måned1,7 Teksten tilføjer: „Shebat måned”. samme år, talte Herren til mig i et syn om natten. 8Jeg så en mand sidde på en rød hest mellem nogle myrtebuske i en kløft. Bag ham var der mange ryttere på røde, brune og hvide heste. 9Ved siden af mig stod en engel. „Hvad betyder alle de heste?” spurgte jeg englen. „Det vil du få at se!” svarede han.
10„Herren sendte dem ud for at inspicere hele jorden,” forklarede englen på den røde hest, 11der stod mellem myrtebuskene. Derefter aflagde de øvrige ryttere rapport: „Vi har været overalt på jorden, og alle vegne er der fred og ro.” 12Da sagde englen på den røde hest: „Almægtige Herre, i 70 år har du været vred på de landflygtige fra Jerusalem og Judas byer. Hvornår vil du gribe ind og vise dem barmhjertighed?”
13Herren talte nu til englen, som stod ved min side, 14hvorpå englen henvendte sig til mig og sagde: „Forkynd følgende budskab fra Herren, den Almægtige: ‚Jerusalem og Zions bjerg har en særlig plads i mit hjerte. 15Jeg er vred på de selvsikre, gudløse folkeslag, for selv om jeg brugte dem til at straffe mit folk, gik de alt for langt i deres skånselsløse opførsel. 16Derfor erklærer jeg, Herren: Jeg kommer Jerusalem i møde med barmhjertighed. Mit tempel skal genrejses, og hele Jerusalem skal genopbygges. Ja, siger jeg, Herren den Almægtige: 17Jeg vil igen velsigne Israels byer med velstand, trøste Jerusalems indbyggere og bosætte mig på Zions bjerg.’ ”