Zefaniya 3 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

Asante Twi Contemporary Bible

Sefania 3:1-20

Yerusalem Daakye

1Nnome nka nhyɛsofoɔ kuropɔn

atuateɛ kuropɔn a ɛho agu fi!

2Ɔnnyɛ ɔsetie mma obiara

ɔnnye nteɛsoɔ biara nto mu.

Ɔmfa ne ho nto Awurade so.

Ɔntwi mmɛn ne Onyankopɔn.

3Nʼakandifoɔ yɛ agyata a wɔbobɔ mu,

ne sodifoɔ yɛ mpataku a wɔnam anadwo,

a wɔnnya biribiara mma adekyeɛ.

4Ne nkɔmhyɛfoɔ yɛ ahantan;

wɔyɛ afatwafoɔ.

Nʼasɔfoɔ gu kronkronbea ho fi.

Wɔnam mmara no so di nsɛmmɔne.

5Awurade a ɔte ne mu no yɛ ɔteneneeni;

ɔnnyɛ mfomsoɔ biara.

Adekyeeɛ biara ɔda ne tenenee adi,

na ɔnni hwammɔ da,

nanso amumuyɛfoɔ deɛ wonnim aniwuo.

6“Masɛe amanaman;

madwiri wɔn abandenden agu.

Wɔn mmorɔno so adeda mpan,

a obiara ntwa mu hɔ.

Wɔaseɛ wɔn nkuropɔn;

a obi biara renka.

7Meka kyerɛɛ kuropɔn no sɛ,

‘ampa ara wobɛsuro me

na woagye nteɛsoɔ ato mu!’

Na afei ne tenaberɛ rensɛe,

na mʼasotwe biara nso remma ne so.

Nanso, wɔn ho peree wɔn

sɛ wɔbɛkɔso ayɛ bɔne wɔn nneyɛeɛ nyinaa mu.

8Enti, twɛn me,” sɛdeɛ Awurade seɛ nie,

“na ɛda no mɛsɔre adi adanseɛ.

Mayɛ mʼadwene sɛ mɛboaboa amanaman

ne ahennie ano

na mahwie mʼabufuo agu wɔn so

mʼabufuhyeɛ nyinaa.

Me ninkuntwe abufuo ogya mu no,

asase nyinaa bɛhye.

9“Afei mɛdwira nnipa no ano,

na wɔn nyinaa abɔ Awurade din

na wɔaka abɔ mu asom no.

10Mʼasomfoɔ, me nkurɔfoɔ a wɔabɔ ahwete no

bɛfiri nsubɔntene a ɛwɔ Kus nohoa

de wɔn afɔrebɔdeɛ abrɛ me.

11Saa ɛda no, wo Yerusalem, wɔrengu wʼanim ase

wɔ nneyɛeɛ bɔne a woayɛ atia me ho,

ɛfiri sɛ mɛyi afiri saa kuropɔn yi mu,

wɔn a wodi ahantan mu ahurisie

na worenyɛ ahantan bio

wɔ me bepɔ kronkron no so.

12Nanso mɛgya wɔ wo mu

wɔn a wɔdwo na wɔbrɛ wɔn ho ase,

na wɔde wɔn ho to Awurade so.

13Israel nkaeɛfoɔ renyɛ bɔne

Wɔrenka nkontonpo nsɛm,

na wɔn ano renka nnaadaa nsɛm

wɔbɛdidi na wɔada

na obiara renyi wɔn hu.”

14To dwom Ao, Ɔbabaa Sion;

team denden Ao, Israel!

Ma wʼani nnye, na di ahurisie wɔ wʼakoma nyinaa mu,

Ao, Ɔbabaa Yerusalem!

15Ɛfiri sɛ, Awurade ayi wʼasotweɛ afiri wo so,

wama wo ɔtamfoɔ asane nʼakyi.

Awurade Israelhene ka wo ho;

worensuro ɔhaw biara bio.

16Saa ɛda no, wɔbɛka akyerɛ Yerusalem sɛ,

“Mma nsuro, Ao Sion!

Mma wo nsa mu nhodwo.

17Awurade wo Onyankopɔn ne wo wɔ hɔ,

Ɔyɛ ɔgyefoɔ ɔhoɔdenfoɔ.

Nʼani bɛgye wo ho

ɔfiri ne dɔ mu bɛdwodwo wo,

ɔde nnwontoɔ bɛma nʼani agye wo ho.

18“Mo awerɛhoɔ to bɛtwa

ɛfiri sɛ mobɛnya ɛkwan adi mo afahyɛ no;

mo anim rengu ase bio.

19Saa ɛberɛ no me ne wɔn

a wɔhyɛɛ wo so nyinaa bɛdi;

Mɛgye mmerɛyɛfoɔ

na mɛboaboa wɔn a wɔabɔ wɔn ahwete no ano.

Mɛkamfo wɔn ahyɛ wɔn animuonyam

asase biara a wɔguu wɔn anim ase wɔ so no so.

20Saa ɛda no, mɛboaboa wo ano,

na mede wo aba fie.

Mɛhyɛ wo animuonyam na makamfo wo

wɔ asase so nnipa nyinaa mu

na mede wʼahonyadeɛ bɛsane ama wo

na wode wʼani bɛhunu,”

sɛdeɛ Awurade ka nie.