Yuda 1 – CCL & PCB

The Word of God in Contemporary Chichewa

Yuda 1:1-25

1Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo.

Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.

2Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.

Tchimo ndi Kuwonongeka kwa Osapembedza

3Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima. 4Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.

5Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire. 6Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. 7Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha.

8Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba. 9Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!” 10Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.

11Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.

12Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu. 13Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya.

14Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka 15kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.” 16Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.

Awalimbikitsa kuti Apirire

17Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu. 18Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.” 19Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.

20Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera. 21Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha.

22Muwachitire chifundo amene akukayika. 23Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.

Mawu Olemekeza Mulungu

24Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa, 25kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni.

Persian Contemporary Bible

یهودا 1:1-25

1این نامه از طرف یهودا، خدمتگزار1‏:1 یا «غلام». عیسی مسیح و برادر یعقوب است.

این نامه را به همۀ کسانی می‌نویسم که از جانب خدای پدر که شما را دوست دارد و در عیسی مسیح محفوظ نگه می‌دارد، فرا خوانده شده‌اید.

2از خدا، خواستار رحمت و آرامش و محبت روزافزون برای شما هستم.

گناه و هلاکت بی‌دینان

3ای عزیزان، اشتیاق بسیار داشتم تا دربارهٔ نجاتی که خداوند به ما بخشیده، مطالبی برایتان بنویسم. اما اکنون لازم می‌بینم، مطلب دیگری به جای آن بنویسم تا شما را ترغیب نمایم از آن ایمانی که خدا یکبار برای همیشه به مقدّسین خود سپرده، با جدیت تمام دفاع کنید. 4زیرا عده‌ای خدانشناس با نیرنگ وارد کلیسا شده‌اند و تعلیم می‌دهند که ما پس از مسیحی شدن، می‌توانیم هر چه دلمان می‌خواهد انجام دهیم بدون آنکه از مجازات الهی بترسیم. عاقبت هولناک این معلمین دروغین و گمراه از مدتها پیش تعیین شده است، زیرا با سرور و خداوند یگانهٔ ما عیسی مسیح، سر به مخالفت برداشته‌اند.

5گرچه این حقایق را به خوبی می‌دانید، اما می‌خواهم برخی نکات را بار دیگر یادآوری نمایم. همان‌گونه که می‌دانید، خداوند پس از آنکه قوم اسرائیل را از سرزمین مصر رهایی بخشید، تمام کسانی را که بی‌ایمان شده بودند و از خدا سرپیچی می‌کردند، هلاک ساخت. 6همچنین به یاد آورید فرشتگانی را که در محدودۀ اختیارات خود نماندند، بلکه جایگاه خود را ترک کردند، و خدا آنها را در تاریکی مطلق محبوس فرمود تا روز عظیم داوری فرا برسد. 7در ضمن، شهرهای «سدوم» و «عموره» را نیز به یاد داشته باشید. اهالی آنجا و شهرهای مجاور، به انواع شهوات و انحرافات جنسی آلوده بودند. بنابراین، همهٔ آنها نابود شدند تا برای ما درس عبرتی باشند و بدانیم که آتش ابدی وجود دارد که در آنجا گناهکاران مجازات می‌شوند.

8با وجود همهٔ اینها، این معلمین گمراه که از خوابهای خود الهام می‌گیرند، به زندگی فاسد و بی‌بند و بار خود ادامه می‌دهند، و بدن خود را آلوده می‌سازند؛ در ضمن مطیع هیچ مرجع قدرتی نیز نیستند و موجودات آسمانی را به باد مسخره می‌گیرند. 9در حالی که «میکائیل»، رئیس فرشتگان، وقتی با ابلیس بر سر جسد موسی بحث می‌کرد، به خود اجازه نداد به او تهمت بزند و اهانت کند؛ بلکه فقط گفت: «خداوند تو را توبیخ فرماید!» 10اما این اشخاص هر چه را که نمی‌فهمند مسخره می‌کنند و ناسزا می‌گویند؛ ایشان همچون حیوانات بی‌فهم، دست به هر کاری که دلشان می‌خواهد می‌زنند، و به این ترتیب، به سوی نابودی و هلاکت می‌شتابند.

11وای به حال آنان، زیرا از قائن سرمشق می‌گیرند که برادرش را کشت، و مانند بلعام رفتار می‌کنند که به خاطر پول، دست به هر کاری می‌زد. پس آنها مانند قورح در عصیان خود هلاک خواهند شد.

12این اشخاص که در ضیافتهای کلیسایی، به جمع شما می‌پیوندند، لکه‌های ناپاکی هستند که شما را آلوده می‌کنند. با بی‌شرمی می‌خندند و شکم خود را سیر می‌کنند، بدون آنکه رعایت حال دیگران را بنمایند. همچون ابرهایی هستند که از زمینهای خشک عبور می‌کنند، بدون آنکه قطره‌ای باران ببارانند. قولهای آنان اعتباری ندارد. درختانی هستند که در موسم میوه، ثمر نمی‌دهند. اینان دو بار طعم مرگ را چشیده‌اند؛ یک بار زمانی که در گناه بودند، و بار دیگر وقتی از مسیح روگردان شدند. از این رو، باید منتظر داوری خدا باشند. 13تنها چیزی که از خود برجای می‌گذارند، ننگ و رسوایی است، درست مانند کف ناپاک دریا که از موجهای خروشان بر ساحل باقی می‌ماند. درخشان همچون ستارگان، اما سرگردان هستند و به سوی ظلمت و تاریکی مطلق ابدی می‌شتابند.

14خَنوخ، که هفت نسل بعد از آدم زندگی می‌کرد، دربارۀ همین اشخاص نبوّت کرده، می‌گوید: «بدانید که خداوند با هزاران هزار از مقدّسین خود می‌آید، 15تا مردم دنیا را داوری کند. او همه بدکاران را به سبب تمامی کارهای زشتی که انجام داده‌اند، و گناهکاران فاسدی را که سخنان زشت بر ضد خدا گفته‌اند محکوم خواهد کرد.» 16این افراد گله‌مند و عیب‌جو هستند و تنها برای ارضای شهوات خود زندگی می‌کنند. آنها جسور و خودنما هستند و فقط به کسی احترام می‌گذارند که بدانند سودی از او عایدشان می‌شود.

دعوت به پایداری

17ای عزیزان، پیشگویی رسولان خداوند ما عیسی مسیح را به یاد آورید. 18ایشان می‌گفتند که در زمانهای آخر اشخاصی پیدا خواهند شد که مطابق امیال ناپاک خود رفتار خواهند کرد و حقیقت را مسخره خواهند نمود. 19همینها هستند که بین شما تفرقه و جدایی ایجاد می‌کنند. آنان فقط به دنبال هوسهای خود هستند و روح خدا در وجود ایشان ساکن نیست.

20اما شما ای عزیزان، یکدیگر را در ایمان بس مقدّس خود بنا نمایید، در روح‌القدس دعا کنید، 21و منتظر رحمت خداوند عیسی مسیح باشید، که شما را به حیات جاویدان خواهد رساند. بدین ترتیب شما خود را در محبت خدا محفوظ نگاه خواهید داشت. 22با کسانی که در تردید به سر می‌برند رحیم باشید. 23گمراهان را از آتش مجازات رهایی دهید، اما مراقب باشید که خودتان نیز به سوی گناه کشیده نشوید. در همان حال که دلتان بر این گناهکاران می‌سوزد، از اعمال گناه‌آلود ایشان متنفر باشید.

حمد و ستایش

24و حال، تمامی جلال و عزت، بر خدایی باد که قادر است شما را از لغزش محفوظ بدارد. او شما را بی‌عیب و با شادی عظیم به حضور پرجلال خود حاضر خواهد ساخت. 25تمامی جلال بر آن خدای یکتا و نجات‌دهندۀ ما، به واسطۀ عیسی مسیح، خداوند ما، باد. تمامی جلال، شکوه، توانایی و اقتدار از ازل، حال، و تا ابد برازندۀ اوست! آمین.