Yoswa 7 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 7:1-26

Tchimo la Akani

1Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.

2Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.

3Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.” 4Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai. 5Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.

6Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo. 7Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani! 8Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake? 9Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”

10Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere? 11Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo. 12Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.

13“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’

14“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi. 15Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”

16Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa. 17Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa. 18Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.

19Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”

20Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi: 21Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”

22Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake. 23Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.

24Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori. 25Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.”

Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo. 26Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.

New International Reader’s Version

Joshua 7:1-26

Achan Sins Against the Lord

1But the Israelites weren’t faithful to the Lord. They didn’t destroy what had been set apart to him. So they did not do what they had been told to do. Achan had taken some of those things. So the Lord became very angry with Israel. Achan was the son of Karmi. Karmi was the son of Zimri. And Zimri was the son of Zerah. Achan and all his relatives were from the tribe of Judah.

2Joshua sent men from Jericho to Ai. Ai is near Beth Aven east of Bethel. Joshua told the men, “Go up and check out the area around Ai.” So the men went up and checked it out.

3Then they returned to Joshua. They said, “The whole army doesn’t have to go up and attack Ai. Send only two or three thousand men. They can take the city. Don’t make the whole army go up there. Only a few people live in Ai.” 4So only about 3,000 troops went up. But the men of Ai drove them away. 5They chased the Israelites from the city gate all the way to Shebarim. They killed about 36 of them on the way down. So the Israelites were terrified.

6Joshua and the elders of Israel became sad. Joshua tore his clothes. He fell in front of the ark of the Lord with his face to the ground. He remained there until evening. The elders did the same thing. They also sprinkled dust on their heads. 7Joshua said, “Lord and King, why did you ever bring these people across the Jordan River? Did you want to hand us over to the Amorites? Did you want them to destroy us? I wish we had been content to stay on the other side of the Jordan! 8Lord, our enemies have driven us away. What can I say? 9The Canaanites will hear about it. So will everyone else in the country. They will surround us. They’ll erase any mention of our name from the face of the earth. Then what will you do when people don’t honor your great name anymore?”

10The Lord said to Joshua, “Get up! What are you doing down there on your face? 11Israel has sinned. I made a covenant with them. I commanded them to keep it. But they have broken it. They have taken some of the things that had been set apart to me in a special way to be destroyed. They have stolen. They have lied. They have taken the things they stole and have put them with their own things. 12That is why the Israelites can’t stand up against their enemies. They turn their backs and run. That’s because I have decided to let them be destroyed. You must destroy the things you took that had been set apart to me. If you do not, I will not be with you anymore.

13“Go and set the people apart. Tell them, ‘Make yourselves pure. Get ready for tomorrow. Here is what the Lord, the God of Israel, wants you to do. He says, “People of Israel, you have kept some of the things that had been set apart to me to be destroyed. You can’t stand up against your enemies until you get rid of those things.”

14“ ‘In the morning, come forward tribe by tribe. The tribe the Lord chooses will come forward group by group. The group the Lord chooses will come forward family by family. And the men in the family the Lord chooses will come forward one by one. 15Whoever is caught with the things that had been set apart to the Lord will be destroyed by fire. Everything that belongs to that person will also be destroyed. He has broken the Lord’s covenant. He has done a very terrible thing in Israel!’ ”

16Early the next morning Joshua had Israel come forward by tribes. The tribe of Judah was chosen. 17The groups of Judah came forward. The group of Zerah was chosen. Joshua had the group of Zerah come forward by families. The family of Zimri was chosen. 18He had their men come forward one by one. Achan was chosen. Achan was the son of Karmi. Karmi was the son of Zimri. And Zimri was the son of Zerah. Zerah was from the tribe of Judah.

19Joshua said to Achan, “My son, the Lord is the God of Israel. So give him glory and honor him by telling the truth! Tell me what you have done. Don’t hide it from me.”

20Achan replied, “It’s true! I’ve sinned against the Lord, the God of Israel. Here is what I’ve done. 21I saw a beautiful robe from Babylonia among the things we had taken. I saw five pounds of silver. And I saw a gold bar that weighed 20 ounces. I wanted them, so I took them. I hid them in the ground inside my tent. The silver is on the bottom.”

22So Joshua sent some messengers. They ran to Achan’s tent. And there was everything, hidden in his tent! The silver was on the bottom. 23They brought the things out of the tent. They took them to Joshua and all the Israelites. And they spread them out in the sight of the Lord.

24Then Joshua and all the people grabbed Achan, the son of Zerah. They took the silver, the robe and the gold bar. They took Achan’s sons and daughters. They took his cattle, donkeys and sheep. They also took his tent and everything he had. They carried all of it out to the Valley of Achor. 25Joshua said to Achan, “Why have you brought this trouble on us? The Lord will bring trouble on you today.”

Then all the people killed Achan by throwing stones at him. They also killed the rest of his family with stones. They burned all of them up. 26They placed a large pile of rocks on top of Achan’s body. The place has been called the Valley of Achor ever since. That pile is still there to this day. After the people killed Achan, the Lord was no longer angry with them.