Yoswa 19 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 19:1-51

Dziko la Simeoni

1Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda. 2Dzikolo linaphatikiza zigawo izi:

Beeriseba (ndi Seba), Molada, 3Hazari-Suwali, Bala, Ezemu, 4Elitoladi, Betuli, Horima, 5Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa, 6Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.

7Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo. 8Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera.

Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo. 9Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.

Dziko la Zebuloni

10Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni:

Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi. 11Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu. 12Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya. 13Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni. 14Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli. 15Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.

16Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.

Dziko la Isakara

17Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara. 18Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi:

Yezireeli, Kesuloti, Sunemu, 19Hafaraimu, Sioni, Anaharati, 20Rabiti, Kisoni, Ebezi, 21Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi. 22Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.

23Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.

Dziko la Aseri

24Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri. 25Gawo lawo linaphatikiza

Helikati, Hali, Beteni, Akisafu, 26Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati. 27Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli, 28Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu. 29Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu, 30Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.

31Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.

Dziko la Nafutali

32Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.

33Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani. 34Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa. 35Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti, 36Adama, Rama, Hazori, 37Kedesi, Ederi, Eni Hazori, 38Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.

39Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.

Dziko la Dani

40Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani. 41Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi:

Zora, Esitaoli, Iri Semesi, 42Saalabini, Ayaloni, Itira, 43Eloni, Timna, Ekroni, 44Eliteke, Gibetoni, Baalati, 45Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni, 46Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.

47Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.

48Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.

Dziko la Yoswa

49Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake. 50Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.

51Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

New International Reader’s Version

Joshua 19:1-51

Land Is Given to Simeon

1The second lot drawn out was for the tribe of Simeon, according to its family groups. The share of land they were given was in the territory of Judah.

2Here is what Simeon’s share included.

Beersheba, Moladah, 3Hazar Shual, Balah, Ezem, 4Eltolad, Bethul, Hormah, 5Ziklag, Beth Markaboth, Hazar Susah, 6Beth Lebaoth and Sharuhen. The total number of towns was 13. Some of them had villages near them.

7Here’s another list of towns given to Simeon.

Ain, Rimmon, Ether and Ashan. The total number of towns was four. Some of them had villages near them. 8The towns and all the villages around them reached all the way to Ramah in the Negev Desert.

That was the share of land the tribe of Simeon received, according to its family groups. 9Simeon’s share of land was taken from Judah’s share. That’s because Judah had more land than they needed. So the people of Simeon received their share of land inside the territory of Judah.

Land Is Given to Zebulun

10The third lot drawn out was for the tribe of Zebulun, according to its family groups. Here are the borders of Zebulun’s territory.

The border of their share of land went as far as Sarid. 11It ran west to Maralah and touched Dabbesheth. It reached to the valley near Jokneam. 12It turned east from Sarid toward the sunrise. It went to the territory of Kisloth Tabor. It went on to Daberath and up to Japhia. 13Then it continued east to Gath Hepher and Eth Kazin. It came to an end at Rimmon and turned toward Neah. 14There the border went around on the north to Hannathon. It came to an end at the Valley of Iphtah El.

15Zebulun’s territory included Kattath, Nahalal, Shimron, Idalah and Bethlehem.

The total number of towns was 12. Some of them had villages near them.

16Those towns and their villages were Zebulun’s share, according to its family groups.

Land Is Given to Issachar

17The fourth lot drawn out was for the tribe of Issachar, according to its family groups. 18Here is what Issachar’s share included.

Jezreel, Kesulloth, Shunem, 19Hapharaim, Shion, Anaharath, 20Rabbith, Kishion, Ebez, 21Remeth, En Gannim, En Haddah and Beth Pazzez.

22The border touched Tabor, Shahazumah and Beth Shemesh. It came to an end at the Jordan River.

The total number of towns was 16. Some of them had villages near them.

23Those towns and their villages were the share the tribe of Issachar received, according to its family groups.

Land Is Given to Asher

24The fifth lot drawn out was for the tribe of Asher, according to its family groups. 25Here is what Asher’s share included.

Helkath, Hali, Beten, Akshaph, 26Allammelek, Amad and Mishal. On the west the border touched Carmel and Shihor Libnath. 27Then it turned east toward Beth Dagon. It touched Zebulun and the Valley of Iphtah El. It went north to Beth Emek and Neiel. It went past Kabul on the left. 28It went to Abdon, Rehob, Hammon and Kanah. It reached all the way to Greater Sidon. 29The border then turned back toward Ramah. It went to Tyre, a city that had high walls around it. It turned toward Hosah. It came to an end at the Mediterranean Sea in the area of Akzib, 30Ummah, Aphek and Rehob.

The total number of towns was 22. Some of them had villages near them.

31Those towns and their villages were the share the tribe of Asher received, according to its family groups.

Land Is Given to Naphtali

32The sixth lot drawn out was for Naphtali, according to its family groups.

33Their border started at Heleph and the large tree in Zaanannim. It went past Adami Nekeb and Jabneel. It went to Lakkum and came to an end at the Jordan River. 34The border ran west through Aznoth Tabor. It came to an end at Hukkok. It touched Zebulun on the south. It touched Asher on the west. It touched the Jordan on the east.

35The towns that had high walls around them were Ziddim, Zer, Hammath, Rakkath, Kinnereth, 36Adamah, Ramah, Hazor, 37Kedesh, Edrei, En Hazor, 38Iron, Migdal El, Horem, Beth Anath and Beth Shemesh.

The total number of towns was 19. Some of them had villages near them.

39Those towns and their villages were the share the tribe of Naphtali received, according to its family groups.

Land Is Given to Dan

40The seventh lot drawn out was for the tribe of Dan, according to its family groups. 41Here is what Dan’s share of land included.

Zorah, Eshtaol, Ir Shemesh, 42Shaalabbin, Aijalon, Ithlah, 43Elon, Timnah, Ekron, 44Eltekeh, Gibbethon, Baalath, 45Jehud, Bene Berak, Gath Rimmon, 46Me Jarkon and Rakkon. Dan’s share included the area that faces Joppa.

47The people of Dan lost their territory. So they went up and attacked Leshem. They captured it. They killed its people with their swords. Then they moved into Leshem and made their homes there. They named it Dan. That’s because they traced their family line back to him.

48All those towns and their villages were the share the tribe of Dan received, according to its family groups.

Land Is Given to Joshua

49The Israelites finished dividing up the shares of land the tribes received. Then they gave a share to Joshua, the son of Nun. 50They did what the Lord had commanded them to do. They gave Joshua the town he asked for. It was Timnath Serah in the hill country of Ephraim. He built up the town and made his home there.

51All those territories were given out by casting lots at Shiloh. The lots were drawn out by Eleazar the priest and by Joshua, the son of Nun. The leaders of the tribes of Israel helped them. The lots were drawn out in front of the Lord at the entrance to the tent of meeting. So the work of dividing up the land was finished.