Yoswa 17 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 17:1-18

1Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani. 2Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.

3Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. 4Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova. 5Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi 6chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.

7Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa. 8(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu). 9Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja. 10Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.

11Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).

12Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi. 13Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.

14Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”

15Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”

16Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”

17Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha, 18dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約書亞記 17:1-18

1以下是約瑟的長子瑪拿西支派分到的土地:瑪拿西的長子、基列的父親瑪吉是個戰士,因此分到了基列巴珊兩地。 2瑪拿西其他的子孫也按宗族分到了土地,他們屬於亞比以謝希勒亞斯列示劍希弗示米大宗族。這些男子按宗族都是約瑟的兒子瑪拿西的後代。 3瑪拿西的玄孫、瑪吉的曾孫、基列的孫子、希弗的兒子西羅非哈沒有兒子,只有五個女兒,名叫瑪拉挪阿曷拉密迦得撒4她們來見祭司以利亞撒的兒子約書亞和各首領,說:「耶和華曾經吩咐摩西在我們親族中分給我們產業。」約書亞便照耶和華的吩咐,讓她們在叔伯中也分到產業。 5除了約旦河東的基列巴珊兩地以外,瑪拿西人還分到十塊土地, 6因為在瑪拿西的後代中,女性也分到了產業。瑪拿西其他的子孫分到基列地區。

7瑪拿西支派分到的產業從亞設開始,到示劍東面的密米他,再向南到隱·他普亞人居住的地方。 8他普亞地屬於瑪拿西,但在瑪拿西邊界上的他普亞城屬於以法蓮的子孫。 9邊界繼續向南到加拿河,在河南側瑪拿西境內的城邑都歸以法蓮瑪拿西的邊界沿著加拿河北側直到地中海。 10這樣,南面歸以法蓮,北面歸瑪拿西,西部邊界是地中海,北接亞設,東鄰以薩迦11以薩迦亞設境內,瑪拿西擁有伯·善以伯蓮多珥隱·多珥他納米吉多及其附近的鄉村。 12可是,瑪拿西人沒能把這些城邑的迦南人趕走,因為他們執意不肯離開。 13以色列人國勢強盛的時候,就讓迦南人服勞役,但始終沒有把他們完全趕走。

14約瑟的子孫對約書亞說:「耶和華賜福給我們,使我們人口眾多,為什麼你只讓我們抽一支籤,分一份產業呢?」 15約書亞對他們說:「如果你們人口眾多,認為以法蓮山區窄小,你們可以到比利洗人和利乏音人居住的地方開闢林區。」 16他們答道:「那些地方不夠我們住,何況住在伯·善一帶和耶斯列平原的迦南人都有鐵戰車。」 17約書亞約瑟的子孫以法蓮人和瑪拿西人說:「你們人口眾多,勢力強大,不應只得一籤之地, 18山區也要分給你們,雖然全是森林,但可以開闢土地,使整個地區歸你們。雖然迦南人強盛,有鐵戰車,但你們能夠趕走他們。」