Yoswa 14 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 14:1-15

Kugawa kwa Dziko la Kumadzulo kwa Yorodani

1Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli. 2Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose. 3Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo. 4Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo. 5Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.

Apereka Hebroni kwa Kalebe

6Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea. 7Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera. 8Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse. 9Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’

10“Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85. 11Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse. 12Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”

13Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake. 14Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse. 15(Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki).

Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.

New Russian Translation

Навин 14:1-15

Раздел земель к западу от Иордана

1Вот земли, что израильтяне получили в удел в земле Ханаана, которые им разделили священник Элеазар, Иисус, сын Навин, и главы семейств в родах Израиля. 2Их уделы были определены по жребию девяти с половиной родам, как повелел Господь через Моисея. 3Моисей дал двум с половиной родам уделы к востоку от Иордана, но не дал между остальными удела роду Левия, 4потому что от сыновей Иосифа произошли два рода – Манассия и Ефрем. Левиты не получили земельного надела, а только города, чтобы жить в них, с пастбищами для своих отар и стад. 5И израильтяне разделили землю, как повелел Моисею Господь.

Хеврон отдан Халеву

6Люди из рода Иуды пришли к Иисусу в Гилгал, и Халев, сын кенезеянина Иефоннии, сказал ему:

– Ты знаешь, что Господь сказал Моисею, Божьему человеку, в Кадеш-Барнеа обо мне и о тебе. 7Мне было сорок лет, когда Моисей, слуга Господа, послал меня из Кадеш-Барнеа разведать землю. Я вернулся к нему с правдивыми вестями, 8но мои братья, которые ходили со мной, заставили народ пасть духом, а я от всего сердца следовал Господу, моему Богу. 9И Моисей поклялся мне в тот день: «Земля, по которой ступали твои ноги, будет уделом тебе и твоим детям навеки, потому что ты от всего сердца следовал Господу, моему Богу»14:9 См. Втор. 1:36..

10И вот, как Господь и обещал, Он сохранял меня в живых сорок пять лет с того времени, как Он сказал это Моисею, когда Израиль скитался в пустыне. Мне теперь восемьдесят пять лет, 11и я все еще так же крепок, как в тот день, когда меня посылал Моисей; у меня столько же сил для битвы, сколько было тогда. 12Итак, дай мне эти нагорья, о которых говорил в тот день Господь. Ты сам тогда слышал, что там были анакиты, и города у них большие и укрепленные; может быть, Господь будет со мной, и я прогоню их, как Господь и сказал.

13И Иисус благословил Халева, сына Иефонниина, и дал ему в удел Хеврон. 14Так с тех пор Хеврон стал уделом Халева, сына кенезеянина Иефоннии, потому что он от всего сердца следовал Господу, Богу Израиля. 15(Прежде Хеврон назывался Кирьят-Арба14:15 То есть город Арбы.; этот Арба был самым великим человеком среди анакитов.)

И земля успокоилась от войны.