Yoswa 13 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 13:1-33

Mayiko Otsala Oyenera Kulandidwa

1Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.

2“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri 3kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto. 4Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori. 5Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.

6“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira. 7Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”

Kugawidwa kwa Dziko la Kummawa kwa Yorodani

8Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.

9Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni. 10Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni. 11Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka. 12Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali. 13Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.

14Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.

15Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.

16Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba. 17Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni, 18Yahaza, Kedemoti, Mefaati. 19Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa, 20Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti. 21Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni. 22Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga. 23Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.

24Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:

25Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba; 26ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri. 27Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto. 28Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.

29Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.

30Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko. 31Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.

32Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani. 33Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

La Bible du Semeur

Josué 13:1-33

Le partage du pays

Les territoires restant à conquérir

1Josué était devenu vieux13.1 Il avait entre 90 et 100 ans. Caleb en avait 85 (14.10).. L’Eternel lui dit : Te voilà âgé à présent, et il reste encore un grand pays à conquérir. 2Voici le territoire qui reste : tous les districts des Philistins et le territoire des Gueshouriens13.2 Peuplade habitant le sud de la Philistie du côté de l’Egypte. David les combattit pendant son séjour à Tsiqlag (1 S 27.8)., 3c’est-à-dire la région qui s’étend depuis le torrent du Shihor13.3 Le Wadi el-Arish qui coule à la limite est du Sinaï. qui coule en face de l’Egypte jusqu’au territoire d’Eqrôn au nord, toute cette contrée doit être considérée comme cananéenne. Elle comprend les cinq principautés philistines de Gaza, d’Ashdod, d’Ashkelôn, de Gath et d’Eqrôn, ainsi que le domaine des Avviens13.3 Sur les Avviens, voir Dt 2.23. au sud. 4Il reste également à conquérir tout le pays des Cananéens depuis Meara qui appartient aux Sidoniens jusqu’à Apheq à la frontière des Amoréens, 5celui des Guibliens13.5 Habitants de l’ancienne Byblos (au nord de l’actuelle Beyrouth), des Phéniciens. et tout le Liban oriental, depuis Baal-Gad au pied du mont Hermon jusqu’à Lebo-Hamath, 6ainsi que toute la région montagneuse située entre le Liban et Misrephoth-Maïm habitée par les Sidoniens13.6 Originaires de la ville phénicienne de Sidon.. Je déposséderai les populations de ce pays au fur et à mesure de l’avance des Israélites. En attendant, partage-leur déjà ce pays par le sort pour qu’ils le possèdent, comme je te l’ai ordonné.

Le territoire des tribus restées à l’est du Jourdain

7Maintenant, procède au partage pour attribuer le pays en possession aux neuf tribus et à la demi-tribu de Manassé.

8L’autre moitié de la tribu de Manassé, et les tribus de Ruben et de Gad, ont déjà reçu leur patrimoine. Moïse, serviteur de l’Eternel, le leur a attribué à l’est du Jourdain13.8 Voir Nb 32.28, 32 ; Dt 3.18-20. Cf. Jos 1.12-15.. 9Il s’étend jusqu’à Aroër, sur le bord du torrent de l’Arnon et jusqu’à la ville située au milieu de la vallée et comprend tout le plateau de Médeba jusqu’à Dibôn 10et toutes les villes de Sihôn, roi des Amoréens qui avait régné à Heshbôn, jusqu’à la frontière des Ammonites13.10 Nb 21.21-32 ; Dt 2.26-37 ; Nb 32.3.. 11Il comprend aussi le pays de Galaad et le territoire des Gueshouriens et des Maakathiens, le mont Hermon et tout le Basan jusqu’à Salka : 12dans le Basan, c’est l’ensemble du royaume de Og, le dernier des Rephaïm qui a régné à Ashtaroth et à Edréi. Moïse a vaincu ces rois et les a dépossédés de leurs territoires. 13Toutefois les Israélites n’ont pas dépossédé les Gueshouriens et les Maakathiens, si bien qu’ils ont habité jusqu’à aujourd’hui au milieu d’Israël. 14A la tribu de Lévi, et à elle seule, il ne donna pas de patrimoine. En effet, ce sont les sacrifices consumés par le feu qui appartiennent à l’Eternel, le Dieu d’Israël, qui constituent son bien comme Dieu le lui a déclaré13.14 Voir Dt 18.1-8..

Le territoire de la tribu de Ruben

15Le territoire que Moïse avait attribué aux familles de la tribu de Ruben 16s’étend depuis la ville d’Aroër au bord du torrent de l’Arnon et la ville située au milieu de cette vallée. Il comprenait tout le plateau autour de Médeba, 17Heshbôn et toutes les bourgades du plateau qui en dépendaient, c’est-à-dire Dibôn, Bamoth-Baal, Beth-Baal-Meôn, 18Yahats, Qedémoth, Méphaath, 19Qiryataïm, Sibma, Tséreth-Hashahar sur la montagne qui domine la vallée, 20Beth-Peor, les pentes du Pisga et Beth-Hayeshimoth. 21En outre, il comprenait toutes les villes du plateau et tout le royaume de Sihôn, roi des Amoréens, qui avait régné à Heshbôn, que Moïse avait vaincu en même temps que les chefs de Madian, vassaux de Sihôn qui habitaient le pays : Evi, Réqem, Tsour, Hour et Réba. 22Parmi les victimes des Israélites il y avait aussi le devin Balaam, fils de Béor, qu’ils tuèrent par l’épée à ce moment-là13.22 Voir Nb 22 à 24. Balaam fut tué avec les Madianites qui tentèrent de séduire Israël par l’idolâtrie et la débauche (Nb 25 ; 31.8).. 23La frontière des descendants de Ruben était constituée par le Jourdain et le territoire limitrophe. Tel était le patrimoine réparti entre les familles de Ruben, avec les villes qu’il comprenait et les villages qui en dépendaient.

Le territoire de la tribu de Gad

24Moïse avait aussi donné sa part aux familles de la tribu de Gad. 25Leur territoire comprenait Yaezer, toutes les villes de Galaad et la moitié du pays des Ammonites jusqu’à Aroër près de Rabba. 26Il s’étendait depuis Heshbôn jusqu’à Ramath-Mitspé et Betonim, et depuis Mahanaïm jusqu’à la frontière de Debir. 27Enfin, dans la vallée du Jourdain, il comprenait Beth-Haram, Beth-Nimra, Soukkoth et Tsaphôn, qui formaient le reste du royaume de Sihôn, roi de Heshbôn, et toute la rive est du Jourdain qui constituait la frontière jusqu’au lac de Génézareth. 28Tel était le patrimoine réparti entre les familles de Gad avec les villes qu’il comprenait et les villages qui en dépendaient.

Le territoire de la demi-tribu de Manassé (domaine oriental)

29Enfin Moïse avait donné sa part à la demi-tribu de Manassé, répartie selon ses familles. 30Leur territoire comprenait, à partir de Mahanaïm, le Basan, tout le royaume de Og, le roi du Basan, ainsi que les soixante bourgs de Yaïr en Basan. 31La moitié du pays de Galaad, Ashtaroth et Edréi, les anciennes capitales du royaume de Og en Basan, échurent aux descendants de Makir, fils de Manassé, à la moitié d’entre eux, réparties entre leurs familles. 32Telle fut la répartition faite par Moïse, lorsqu’il se trouvait dans les plaines de Moab, du côté oriental du Jourdain, en face de Jéricho. 33Il n’attribua pas de patrimoine à la tribu de Lévi. L’Eternel, le Dieu d’Israël, est lui-même leur patrimoine, comme il le leur a dit13.33 Voir Nb 18.20 ; Dt 18.2..