Yohane 12 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 12:1-50

Mariya Adzoza Mapazi a Yesu

1Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa. 2Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho. 3Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.

4Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati, 5“Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi. 6Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.

7Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga. 8Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”

9Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa. 10Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro, 11pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.

Yesu Alowa mu Yerusalemu

12Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu. 13Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti,

“Hosana!

“Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye!

“Yodala Mfumu ya Israeli!”

14Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:

15“Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni;

taona mfumu yako ikubwera,

itakhala pa mwana wabulu.”

16Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.

17Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni. 18Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi. 19Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”

Agriki Afuna Kuona Yesu

20Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando. 21Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.” 22Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.

23Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe. 24Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’ 25Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. 26Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.

27“Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi. 28Atate, lemekezani dzina lanu!”

Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.” 29Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”

30Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine. 31Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa. 32Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.” 33Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.

34Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?”

35Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita. 36Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.

Ayuda Apitirira Kusakhulupirira

37Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe. 38Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti:

“Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani,

ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”

39Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:

40“Iye wachititsa khungu maso awo

ndi kuwumitsa mitima yawo,

kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo,

kapena kuzindikira ndi mitima yawo,

kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”

41Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.

42Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge; 43pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.

44Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine. 45Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine. 46Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.

47“Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa. 48Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa. 49Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere. 50Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иохан 12:1-50

Помазание Исо Масеха дорогим ароматическим маслом

(Мат. 26:6-13; Мк. 14:3-9; Лк. 7:37-39)

1За шесть дней до праздника Освобождения Исо пришёл в Вифанию, туда, где жил Элеазар, которого Он воскресил из мёртвых. 2Здесь в честь Исо был устроен обед. Марфа накрывала на стол, и Элеазар вместе с Исо и другими гостями тоже возлежал у стола. 3Марьям в это время взяла кувшин12:3 Букв.: «одна литра», что равняется примерно 330 г. чистого нардового12:3 Нард – ароматическая жидкость, получаемая из определённого растения, которое произрастает только в Индии, на Гималаях, и поэтому доставка делала нард дорогостоящим товаром. Нард смешивали с другими веществами и продавали в алебастровых кувшинах в виде масла, мази или нардовой воды. масла, которое стоило очень дорого, и вылила его на ноги Исо. Потом она стала вытирать Его ноги своими волосами. Весь дом наполнился ароматом масла. 4Иуда Искариот, один из учеников Исо, который впоследствии предал Его, возмутился:

5– Почему было не продать это масло за триста серебряных монет12:5 Букв.: «триста динариев». и не раздать деньги нищим?

6Он говорил это не потому, что заботился о нищих, а потому, что был вор. Ему был доверен ящик с общими деньгами, и он брал из него на свои нужды.

7– Оставь её, – сказал Исо, – она должна была сохранить этот бальзам на день Моего погребения. 8Нищие всегда будут с вами, а Я не всегда буду с вами.

9Тем временем множество иудеев узнало, что Исо там. Они пришли не только для того, чтобы увидеть Исо, но и посмотреть на Элеазара, которого Исо воскресил из мёртвых. 10Главные же священнослужители решили убить и Элеазара, 11потому что из-за него многие иудеи приходили к Исо и верили в Него.

Торжественный въезд в Иерусалим

(Мат. 21:4-9; Мк. 11:7-10; Лк. 19:35-38)

12На следующий день многочисленная толпа, пришедшая на праздник Освобождения, услышала о том, что Исо идёт в Иерусалим. 13Люди взяли пальмовые ветви12:13 Пальмовые ветви символизируют радость победы. и вышли Ему навстречу с возгласами:

– Хвала Царю!12:13 Хвала Царю (букв.: «Осанна» («Спаси нас»)) – выражение, ставшее возгласом хвалы.

Благословен Тот, Кто приходит во имя Вечного!12:13 Заб. 117:25, 26.

Благословен Царь Исроила!12:13 Народ здесь наделяет Исо титулами Масеха.

14Исо нашёл молодого осла и сел на него, как об этом и написано:

15«Не бойся, дочь Сиона!12:15 То есть жители Иерусалима.

Вот идёт Царь твой,

сидя на ослёнке»12:15 Зак. 9:9 (см. Ис. 62:11). Исо въехал в Иерусалим на осле, как миролюбивый и смиренный царь, а не на боевом коне с мечом, как это делали цари того времени..

16Вначале ученики Исо ничего не могли понять. Только после того, как Он был прославлен, они поняли, что сбылось написанное о Нём. 17Люди, бывшие с Исо, когда Он вызвал Элеазара из могилы, воскресив его из мёртвых, продолжали рассказывать об этом случае. 18Потому и вышла встречать Исо целая толпа, что все хотели увидеть Человека, сотворившего такое знамение. 19Блюстители Закона с досадой говорили друг другу:

– Ничего не помогает. Весь мир идёт за Ним!

Исо Масех говорит о Своей смерти

20Среди пришедших на праздник для поклонения было несколько греков. 21Они подошли к Филиппу, ученику Исо, который был родом из Вифсаиды в Галилее, и попросили:

– Господин, мы бы хотели увидеть Исо.

22Филипп пошёл к Андеру, и они вдвоём подошли и сказали об этом Исо. 23Исо ответил:

– Настал час прославиться Ниспосланному как Человек. 24Говорю вам истину: если пшеничное зерно не упадёт в землю и не умрёт, то оно останется одним зерном. Если же оно умрёт, то из него произойдёт много зёрен. 25Тот, кто любит свою жизнь, тот потеряет её, но кто возненавидит свою жизнь в этом мире, тот сохранит её для вечной жизни. 26Тот, кто служит Мне, должен и следовать за Мной. И где Я, там будет и Мой слуга. И Отец Мой прославит того, кто служит Мне.

27Сейчас Моя душа взволнована. Что Я могу сказать? Сказать ли: «Отец, избавь Меня от этого часа»? Но ведь для этого часа Я и пришёл! 28Отец, прославь имя Твоё!

И с небес раздался голос:

– Прославил и ещё прославлю!

29Народ, который там стоял и слышал, говорил, что это гром, но некоторые утверждали, что это ангел говорил с Ним. 30Исо сказал:

– Этот голос был не для Меня, а для вас. 31Теперь настало время суда для мира, и сатана, князь этого греховного мира, будет изгнан вон. 32Но когда Я буду поднят от земли, Я всех привлеку к Себе.

33Это Он сказал, давая им понять, какой смертью Он умрёт.

34Толпа ответила Ему:

– Мы слышали из Писания, что Масех вечно жив12:34 См. Заб. 88:37-38; Ис. 9:6-7; Езек. 37:25; Дон. 7:13-14.. Как же Ты можешь говорить, что «Ниспосланный как Человек будет поднят»? И что тогда из Себя представляет Ниспосланный как Человек?

35Тогда Исо сказал им:

– Ещё совсем недолго Свет будет с вами. Ходите, пока есть Свет и пока вас не покрыла тьма. А тот, кто ходит во тьме, не знает, куда он идёт. 36Верьте в Свет, пока Свет есть, чтобы вам стать сынами Света.

Закончив говорить, Исо ушёл и скрылся от них.

Неверие народа и страх перед гонениями

37Даже после того как Исо сотворил перед ними столько знамений, они не верили в Него. 38Так исполнились слова пророка Исаии:

«Вечный, кто поверил слышанному от нас,

и кому открылась сила Вечного?»12:38 Ис. 53:1.

39Они потому не могли верить, что, как ещё сказал Исаия:

40«Он ослепил их глаза

и ожесточил их сердца,

чтобы они не увидели глазами,

не поняли сердцами

и не обратились, чтобы Я их исцелил»12:40 Ис. 6:10..

41Исаия сказал это потому, что он видел славу Масеха и говорил о Нём12:41 См. Ис. 6:1-3. То, что Исаия говорит о Вечном, Иохан относит к Исо Масеху.. 42Впрочем даже среди начальников многие поверили в Исо, хотя из боязни, что блюстители Закона отлучат их от общества, они не говорили о своей вере. 43Похвала людей была для них дороже одобрения Всевышнего.

Важность принятия слов Исо Масеха

44Исо воскликнул:

– Когда человек верит в Меня, он верит не только в Меня, но и в Пославшего Меня. 45Когда он смотрит на Меня, он видит Того, Кто послал Меня. 46Я – свет, и Я пришёл в мир, чтобы никто из тех, кто верит в Меня, не остался во тьме.

47Я не сужу того, кто слушает Мои слова, но не делает того, что Я говорю. Ведь Я пришёл не судить мир, а спасти его. 48Для того, кто отвергает Меня и не принимает Моих слов, есть судья; Моё слово будет судить его в Последний день. 49Я ведь не от Себя говорил, но Отец, Который послал Меня, повелел Мне, что говорить и как говорить. 50Я знаю, что Его повеление ведёт к вечной жизни. Поэтому то, что говорю, Я говорю так, как сказал Мне Отец.