Yobu 4 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 4:1-21

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?

Koma ndani angakhale chete wosayankhula?

3Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,

momwe walimbitsira anthu ofowoka.

4Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;

unachirikiza anthu wotha mphamvu.

5Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,

zakukhudza ndipo uli ndi mantha.

6Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?

Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

7“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?

Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?

8Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,

ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.

9Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;

amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.

10Mikango imabangula ndi kulira,

komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.

11Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,

ndipo ana amkango amamwazikana.

12“Mawu anabwera kwa ine mwamseri,

makutu anga anamva kunongʼona kwake.

13Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,

nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,

14ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera

ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.

15Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,

ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.

16Chinthucho chinayimirira

koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.

Chinthu chinayima patsogolo panga,

kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,

17‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?

Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?

18Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,

ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,

19nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,

amene maziko awo ndi fumbi,

amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!

20Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;

mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.

21Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,

kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

Hoffnung für Alle

Hiob 4:1-21

Elifas: Kann ein Mensch gerechter sein als Gott?

1Elifas aus Teman versuchte als Erster, Hiob eine Antwort zu geben.

2»Du bist zwar aufgebracht«, sagte er,

»doch will ich versuchen, dir etwas zu sagen;

ich kann nicht länger schweigen!

3Du selbst hast zahllose Menschen gelehrt,

auf Gott zu vertrauen.

Kraftlose Hände hast du wieder gestärkt.

4War jemand mutlos und ohne Halt,

du hast ihn wieder aufgerichtet

und ihm neuen Lebensmut gegeben.

5Jetzt aber, wo du selbst an der Reihe bist,

verlierst du die Fassung.

Kaum bricht das Unglück über dich herein,

bist du entsetzt!

6Dabei hast du allen Grund zur Hoffnung!

Dein Leben war stets tadellos,

und Gott hast du von Herzen geehrt.

Sei zuversichtlich!

7Kannst du mir nur ein Beispiel nennen,

wo ein gerechter Mensch schuldlos zugrunde ging?

8Im Gegenteil – immer wieder habe ich gesehen:

Wer Unrecht sät, wird Unglück ernten!

9Denn Gott fegt Übeltäter mit seinem Atem hinweg,

mit zornigem Schnauben richtet er sie zugrunde.

10Wenn sie auch wie die Löwen brüllen,

bringt Gott sie doch zum Schweigen

und bricht ihnen die Zähne aus.

11Sie verenden wie Löwen,

die keine Beute mehr finden,

und ihre Kinder werden in alle Winde zerstreut.

12Hiob, heimlich habe ich eine Botschaft bekommen,

leise wurde sie mir zugeflüstert!

13Es geschah in jener Zeit der Nacht,

wenn man sich unruhig im Traum hin- und herwälzt,

wenn tiefer Schlaf die Menschen überfällt:

14Da packten mich Grauen und Entsetzen;

ich zitterte am ganzen Leib.

15Ein Windhauch wehte dicht an mir vorüber –

die Haare standen mir zu Berge!

16Dann sah ich jemanden neben mir,

aber ich konnte ihn nicht erkennen,

nur ein Schatten war zu sehen; er flüsterte:

17›Kann denn ein Mensch gerecht sein vor Gott,

vollkommen vor seinem Schöpfer?‹

18Selbst seinen Dienern im Himmel vertraut Gott nicht,

und an seinen Engeln findet er Fehler.

19Wie viel weniger vertraut er dann den Menschen!

Sie hausen in Lehmhütten,

die im Staub auf der Erde stehen,

und werden wie eine Motte zertreten.

20Mitten aus dem Leben werden sie gerissen,

unwiederbringlich, und keiner beachtet es!

21Ja, Gott bricht ihre Zelte ab;

sie sterben plötzlich

und sind kein bisschen weise geworden!«