Yobu 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 4:1-21

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?

Koma ndani angakhale chete wosayankhula?

3Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,

momwe walimbitsira anthu ofowoka.

4Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;

unachirikiza anthu wotha mphamvu.

5Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,

zakukhudza ndipo uli ndi mantha.

6Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?

Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

7“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?

Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?

8Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,

ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.

9Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;

amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.

10Mikango imabangula ndi kulira,

komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.

11Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,

ndipo ana amkango amamwazikana.

12“Mawu anabwera kwa ine mwamseri,

makutu anga anamva kunongʼona kwake.

13Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,

nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,

14ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera

ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.

15Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,

ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.

16Chinthucho chinayimirira

koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.

Chinthu chinayima patsogolo panga,

kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,

17‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?

Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?

18Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,

ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,

19nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,

amene maziko awo ndi fumbi,

amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!

20Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;

mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.

21Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,

kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約伯記 4:1-21

以利法的責難

1提幔以利法回答說:

2「若有人向你進言,

你會厭煩嗎?

可是,誰能忍住不說呢?

3你曾教導許多人,

使無力的手強壯。

4你的話使人免於跌倒,

你使顫抖的膝硬朗。

5但現在苦難一來,

你便灰心喪膽;

災禍來臨,

你便驚慌失措。

6你敬畏上帝還沒有信心嗎?

你行為純全還沒有盼望嗎?

7你想一想,

哪有無辜的人滅亡?

哪有正直的人遭殃?

8據我所見,

播惡收惡,

種禍得禍。

9他們被上帝的氣息所毀,

被上帝的怒氣所滅。

10獅子咆哮,猛獅吼叫,

壯獅的牙齒被敲掉。

11雄獅因無食而死,

母獅的幼崽離散。

12「有信息暗暗地傳給我,

一聲低語傳入我耳中。

13夜間人們沉睡的時候,

在攪擾思緒的異象中,

14恐懼襲來,

令我戰慄不已,

全身發抖。

15有靈從我臉上拂過,

使我毛骨悚然。

16那靈停住,

我無法辨認其模樣。

眼前出現一個形狀,

寂靜中聽見有聲音說,

17『在上帝面前,世人豈算得上公義?

在創造主面前,凡人豈算得上純潔?

18連上帝的僕人都無法令祂信任,

連祂的天使都被祂找出過錯,

19更何況源自塵土、

住在土造的軀殼裡、

脆弱如蛾的世人呢?

20早晚之間,他們便被毀滅,

永遠消逝,無人察覺。

21他們帳篷的繩索被拔起,

他們毫無智慧地死去。』