Yobu 38 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 38:1-41

Yehova Ayankhula

1Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:

2“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga

poyankhula mawu opanda nzeru?

3Onetsa chamuna;

ndikufunsa

ndipo undiyankhe.

4“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi?

Ndiwuze ngati ukudziwa.

5Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa!

Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?

6Kodi maziko ake anawakumba potani,

kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,

7pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi

ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?

8“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa,

pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,

9pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake

ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,

10pamene ndinayilembera malire ake

ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.

11Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire

apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’

12“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa,

kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,

13kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi

ndi kuthamangitsa anthu oyipa?

14Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo;

zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.

15Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa,

ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.

16“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja

kapena pa magwero ake ozama?

17Kodi anakuonetsapo zipata za imfa?

Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?

18Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa?

Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.

19“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti?

Nanga mdima umakhala kuti?

20Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi?

Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?

21Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale!

Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!

22“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana

kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,

23zimene ndazisungira nthawi ya mavuto

ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?

24Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani

kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?

25Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula,

nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,

26kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu,

chipululu chopandamo munthu,

27kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa

ndi kumeretsamo udzu?

28Kodi mvula ili ndi abambo ake?

Nanga madzi a mame anawabereka ndani?

29Kodi madzi owundana anawabereka ndani?

Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba

30pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala,

pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?

31“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi?

Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?

32Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake

kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?

33Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa?

Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?

34“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo

kuti igwetse mvula ya chigumula?

35Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime?

Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’

36Kodi ndani anayika nzeru mu mtima,

ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?

37Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo?

Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo

38pamene fumbi limasanduka matope,

ndipo matopewo amawumbika?

39“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi

ndi kukhutitsa misona ya mikango

40pamene ili khale mʼmapanga mwawo

kapena pamene ikubisala pa tchire?

41Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani

pamene ana ake akulirira kwa Mulungu

ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?