Yobu 35 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 35:1-16

1Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

2“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?

Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’

3Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,

ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

4“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu

pamodzi ndi abwenzi anu omwe.

5Yangʼanani kumwamba ndipo muone

mitambo imene ili kutali ndi inuyo.

6Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?

Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?

7Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?

Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?

8Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,

ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

9“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;

akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.

10Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,

amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,

11amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi

ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’

12Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye

chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.

13Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;

Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.

14Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti

Iye saona zimene zikuchitika.

Iye adzaweruza molungama ngati

inu mutamudikira

15ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,

zoyipa zambiri zimene anthu amachita,

16abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,

mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

Korean Living Bible

욥기 35:1-16

1엘리후는 말을 계속하였다.

2-3“욥, 너는 하나님 앞에 죄가 없 다고 말하며 ‘내가 죄를 짓지 않는다고 해서 그것이 나에게 무슨 유익이 있습니까?’ 하고 묻는 것이 옳다고 생각하느냐?

4내가 너와 네 친구들에게 대답해 주겠다.

5너는 하늘을 우러러보고 네 위에 높이 걸려 있는 구름을 바라보아라.

6네가 범죄한다고 하나님이 해를 입겠느냐? 네 죄가 많다고 한들 그것이 하나님께 무슨 영향을 미치겠느냐?

7네가 의롭다고 해서 그것이 하나님께 무슨 유익을 줄 수 있겠느냐? 하나님이 너에게서 필요로 하는 것은 아무것도 없다.

8네 죄 때문에 해를 입을 자는 너와 같은 사람뿐이며 너의 의로움으로 유익을 얻을 자도 사람뿐이다.

9“사람들은 학대를 받으면 부르짖고 누가 와서 도와주기를 호소한다.

10-11그러나 ‘밤중에도 노래를 주시며 땅의 짐승보다 우리에게 더 많은 것을 가르치시고 공중의 새보다 우리를 더 지혜롭게 하시는 나의 창조주 하나님이 어디 계신가?’ 하고 말하는 자는 하나도 없구나.

12사람들이 부르짖을 때 하나님이 듣지 않으시는 것은 그들이 교만하고 악하기 때문이다.

13전능하신 하나님은 그들의 헛된 부르짖음에 귀를 기울이시지도 않고 듣지도 않으신다.

14그런데 하나님은 볼 수 없고 네 문제는 그분 앞에 있으니 기다릴 수밖에 없다고 말하는 너에게 하나님이 어떻게 응답하시겠느냐?

15너는 하나님이 벌을 주시지 않으며 죄에 대해서도 별로 관심을 갖지 않으신다고 생각하고 있다.

16그래서 네가 입을 열어 헛된 말을 많이 지껄이지만 너는 네가 하는 말도 깨닫지 못하고 있다.”