Yobu 35 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 35:1-16

1Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

2“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?

Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’

3Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,

ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

4“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu

pamodzi ndi abwenzi anu omwe.

5Yangʼanani kumwamba ndipo muone

mitambo imene ili kutali ndi inuyo.

6Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?

Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?

7Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?

Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?

8Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,

ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

9“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;

akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.

10Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,

amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,

11amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi

ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’

12Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye

chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.

13Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;

Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.

14Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti

Iye saona zimene zikuchitika.

Iye adzaweruza molungama ngati

inu mutamudikira

15ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,

zoyipa zambiri zimene anthu amachita,

16abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,

mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

Hoffnung für Alle

Hiob 35:1-16

Dir selbst schadet deine Bosheit!

1Elihu fuhr fort:

2»Du behauptest:

›Gott wird mich für unschuldig erklären!‹

Meinst du im Ernst, das sei richtig?

3Denn du fragst:

›Was nützt es mir, wenn ich nicht sündige,

was habe ich davon?‹

4Darauf kann ich dir die Antwort geben,

dir und deinen Freunden hier:

5Schau zum Himmel empor,

sieh dir die Wolken an –

sie sind unerreichbar für dich!

6Genauso wenig kann deine Sünde Gott erreichen;

selbst wenn du dich offen gegen ihn stellst:

ihn triffst du damit nicht!

7Und umgekehrt:

Bringt ihm dein tadelloses Leben irgendeinen Nutzen?

Empfängt er damit eine Gabe aus deiner Hand?

8Nein, deine Bosheit trifft nur deine Mitmenschen,

und wenn du Gutes tust, hilft es nur ihnen!

9Laut stöhnen die Menschen unter der Last der Gewaltherrschaft,

sie schreien nach Befreiung vom Joch der Tyrannei.

10Doch keiner fragt nach Gott,

nach seinem Schöpfer,

der in der dunkelsten Stunde uns noch Hoffnung gibt35,10 Wörtlich: der Loblieder gibt in der Nacht..

11Keiner wendet sich an Gott, der uns belehrt

und der uns weiser macht als alle Tiere draußen,

klüger als die Vögel in der Luft.

12Wenn Menschen um Hilfe schreien,

weil die Bosheit siegt,

wird Gott sie doch nicht hören.

13Ja, sie rufen vergeblich;

Gott erhört sie nicht, er beachtet sie nicht einmal.

14Und wie viel weniger wird er dich hören,

wenn du sagst, dass du ihn gar nicht siehst!

Warte geduldig, Hiob, dein Fall ist Gott bekannt!

15Du meinst, dass er niemals zornig wird,

dass er Verbrechen nicht bestraft,

weil er von ihnen gar nichts weiß.

16Und deshalb nimmst du den Mund hier so voll!

Aber du machst bloß leere Worte,

du redest viel und zeigst doch nur,

wie unwissend du bist!«