Yobu 32 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 32:1-22

Mawu a Elihu

1Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. 2Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. 3Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. 4Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. 5Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

6Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,

inuyo ndinu akuluakulu,

nʼchifukwa chake ndimaopa,

ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.

7Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;

anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’

8Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,

mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.

9Si okalamba amene ali ndi nzeru,

si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;

inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’

11Ndadikira nthawi yonseyi,

ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,

pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,

12ineyo ndinakumvetseranidi.

Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;

palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.

13Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;

Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’

14Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,

ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;

mawu awathera.

16Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,

pakuti angoyima phee wopanda yankho?

17Inenso ndiyankhulapo tsopano;

nanenso ndinena zimene ndikudziwa.

18Pakuti ndili nawo mawu ambiri,

ndipo mtima wanga ukundikakamiza;

19mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,

ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.

20Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;

ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.

21Sindidzakondera munthu wina aliyense,

kapena kuyankhula zoshashalika,

22pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,

Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

New Serbian Translation

Књига о Јову 32:1-22

Елијуј

1И тако су тројица људи престали да узвраћају Јову који је у својим очима био праведан. 2На то је на Јова у љутњи плануо Елијуј из Вуза, син Варахилов из Рамовог рода. Разљутио се, јер се овај чинио праведнијим од Бога. 3Разљутио се и на три пријатеља што нису имали одговор, а опет су осудили Јова. 4Наиме, Елијуј је чекао да узврати Јову, јер су остали били старији по годинама од њега. 5Разљутио се Елијуј када је видео да ова тројица људи немају шта да кажу и одговоре.

6Тада је овако одговорио Елијуј из Вуза, син Варахилов:

„Млађи сам од вас по годинама.

Ви сте старији,

па сам се зато склањао у страху

да вам кажем своје мишљење.

7Наиме, рекао сам себи:

’Старост нека говори

и године многе нек разгласе мудрост!’

8Јер је дух у људима

и дах Свемоћнога им даје разум.

9Године многе мудрост не дају

и стари праведност не схватају.

10Зато кажем: ’Послушајте ме,

па да вам и ја изнесем своје мишљење.’

11Ето, чекао сам беседе ваше,

саслушао мишљења ваша

док сте бирали речи.

12Да, пажљиво сам вас пратио.

Али – гле – нико није оповргнуо Јова

и ниједан од вас није узвратио на речи његове!

13И не говорите: ’Мудрост смо пронашли!

А њега нека Бог оповргне, а не човек.’

14Али, није он против мене говорио

па ни ја нећу да узвратим њему вашим доказима.

15А они су се смели и више не узвраћају,

сасвим су остали без речи.

16Зашто да чекам када не говоре,

само стоје и више не узвраћају?!

17А сада ћу ја своје да кажем,

мишљење ћу своје да изнесем.

18Јер препун сам речи,

из утробе моје дух ме на то тера.

19Ево, попут вина без одушка утроба је моја,

распукла би се ко мешина нова.

20Морам да говорим, да себи одушка дам;

отворићу усне своје да бих узвратио.

21Нећу да гледам ко је ко,

никоме да ласкам нећу.

22Па ја и не умем да ласкам,

јер би ме одмах узео Саздатељ мој!