Yobu 30 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 30:1-31

1“Koma tsopano akundinyoza,

ana angʼonoangʼono kwa ine,

anthu amene makolo awo sindikanawalola

kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.

2Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine,

pakuti mphamvu zawo zinatha kale?

3Anali atatheratu kuwonda ndi njala,

ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi,

mʼchipululu usiku.

4Ankathyola therere ndi masamba owawa,

ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.

5Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo,

akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.

6Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma,

pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.

7Ankalira ngati nyama kuthengo

ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.

8Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina,

anathamangitsidwa mʼdziko.

9“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe;

ineyo ndasanduka chisudzo chawo.

10Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa;

akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.

11Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa,

iwowo analekeratu kundiopa.

12Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane;

andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda,

andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.

13Iwo anditsekera njira;

akufuna kundichititsa ngozi,

popanda wina aliyense wowaletsa.

14Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka,

iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.

15Zoopsa zandithetsa mphamvu;

ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo,

chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.

16“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo;

ndili mʼmasiku amasautso.

17Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti

zowawa zanga sizikuleka.

18Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa;

Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.

19Wandiponya mʼmatope,

ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.

20“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha;

ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.

21Inuyo mumandichitira zankhanza;

mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.

22Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo;

mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.

23Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa,

kumalo kumene amoyo onse adzapitako.

24“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima,

amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.

25Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto?

Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?

26Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera;

pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.

27Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka;

ndili mʼmasiku amasautso.

28Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa;

ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.

29Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe,

mnzawo wa akadzidzi.

30Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka;

thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.

31Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro,

ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

Slovo na cestu

Jób 30:1-31

1Nyní pak posmívají se mi mladší mne, jejichž bych otců nechtěl byl postaviti se psy stáda svého. 2Ač síla rukou jejich k čemu by mi byla? Zmařena jest při nich starost jejich. 3Nebo chudobou a hladem znuzeni, utíkali na planá, tmavá, soukromná a pustá místa. 4Kteříž trhali zeliny po chrastinách, ano i koření, a jalovec za pokrm byl jim. 5Z prostřed lidí vyháníni byli; povolávali za nimi, jako za zlodějem, 6Tak že musili bydliti v výmolích potoků, v děrách země a skálí. 7V chrastinách řvali, pod trní se shromažďovali, 8Lidé nejnešlechetnější, nýbrž lidé bez poctivosti, menší váhy i než ta země. 9Nyní, pravím, jsem jejich písničkou, jsa jim učiněn za přísloví. 10V ošklivosti mne mají, vzdalují se mne, a na tvář mou nestydí se plvati. 11Nebo Bůh mou vážnost odjal, a ssoužil mne; pročež uzdu před přítomností mou svrhli. 12Po pravici mládež povstává, nohy mi podrážejí, tak že šlapáním protřeli ke mně stezky nešlechetnosti své. 13Mou pak stezku zkazili, k bídě mé přidali, ač jim to nic nepomůže. 14Jako širokou mezerou vskakují, a k vyplénění mému valí se. 15Obrátily se na mne hrůzy, stihají jako vítr ochotnost mou, nebo jako oblak pomíjí zdraví mé. 16A již ve mně rozlila se duše má, pochytili mne dnové trápení mého, 17Kteréž v noci vrtá kosti mé ve mně; pročež ani nervové moji neodpočívají. 18Oděv můj mění se pro násilnou moc bolesti, kteráž mne tak jako obojek sukně mé svírá. 19Uvrhl mne do bláta, tak že jsem již podobný prachu a popelu. 20Volám k tobě, ó Bože, a neslyšíš mne; postavuji se, ale nehledíš na mne. 21Obrátils mi se v ukrutného nepřítele, silou ruky své mi odporuješ. 22Vznášíš mne u vítr, sázíš mne na něj, a k rozplynutí mi přivodíš zdravý soud. 23Nebo vím, že mne k smrti odkážeš, a do domu, do něhož se shromažďuje všeliký živý. 24Jistě žeť nevztáhne Bůh do hrobu ruky, by pak, když je stírá, i volali. 25Zdaliž jsem neplakal nad tím, kdož okoušel zlých dnů? Duše má kormoutila se nad nuzným. 26Když jsem dobrého čekal, přišlo mi zlé; nadál jsem se světla, ale přišla mrákota. 27Vnitřností mé zevřely, tak že se ještě neupokojily; předstihli mne dnové trápení. 28Chodím osmahlý, ne od slunce, povstávaje, i mezi mnohými křičím. 29Bratrem učiněn jsem draků, a tovaryšem mladých pstrosů. 30Kůže má zčernala na mně, a kosti mé vyprahly od horkosti. 31A protož v kvílení obrátila se harfa má, a píšťalka má v hlas plačících.