Yobu 30 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 30:1-31

1“Koma tsopano akundinyoza,

ana angʼonoangʼono kwa ine,

anthu amene makolo awo sindikanawalola

kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.

2Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine,

pakuti mphamvu zawo zinatha kale?

3Anali atatheratu kuwonda ndi njala,

ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi,

mʼchipululu usiku.

4Ankathyola therere ndi masamba owawa,

ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.

5Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo,

akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.

6Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma,

pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.

7Ankalira ngati nyama kuthengo

ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.

8Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina,

anathamangitsidwa mʼdziko.

9“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe;

ineyo ndasanduka chisudzo chawo.

10Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa;

akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.

11Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa,

iwowo analekeratu kundiopa.

12Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane;

andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda,

andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.

13Iwo anditsekera njira;

akufuna kundichititsa ngozi,

popanda wina aliyense wowaletsa.

14Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka,

iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.

15Zoopsa zandithetsa mphamvu;

ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo,

chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.

16“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo;

ndili mʼmasiku amasautso.

17Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti

zowawa zanga sizikuleka.

18Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa;

Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.

19Wandiponya mʼmatope,

ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.

20“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha;

ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.

21Inuyo mumandichitira zankhanza;

mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.

22Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo;

mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.

23Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa,

kumalo kumene amoyo onse adzapitako.

24“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima,

amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.

25Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto?

Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?

26Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera;

pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.

27Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka;

ndili mʼmasiku amasautso.

28Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa;

ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.

29Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe,

mnzawo wa akadzidzi.

30Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka;

thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.

31Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro,

ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

Hoffnung für Alle

Hiob 30:1-31

Ausgestoßen!

1»Und jetzt?

Jetzt lachen sie mich aus –

sie, die jünger sind als ich;

ihre Väter hätte ich nicht einmal für wert geachtet,

sie zu den Hunden meiner Herde zu stellen!

2Was sollen mir diese Schwächlinge nützen,

die keine Kraft mehr in den Knochen haben?

3Ausgezehrt von Hunger und Armut

nagen sie die Wurzeln in der Wüste ab,

draußen im Land der Einsamkeit.

4Sie pflücken Salzkraut von den Büschen,

und Ginsterwurzeln sind ihr Brot.

5Aus der menschlichen Gemeinschaft wurden sie verjagt,

man schreit ihnen nach wie Dieben.

6In verlassenen Tälern hausen sie,

zwischen Felsen und in Erdhöhlen.

7Im Gestrüpp, da kauern sie und schreien,

unter hohen Distelsträuchern drängen sie sich zusammen.

8Dieses Gesindel, diese Brut,

aus dem Lande weggejagt!

9Und jetzt?

Jetzt machen sie Spottverse,

sie zerreißen sich das Maul über mich.

10Sie verabscheuen mich

und gehen mir aus dem Weg;

und wenn sie mir doch einmal begegnen,

spucken sie mir ins Gesicht!

11Gott hat meine Lebenskraft zerbrochen30,11 Wörtlich: Gott hat die Sehne meines Bogens schlaff gemacht. und mich gedemütigt,

darum kennen sie in meiner Gegenwart keine Rücksicht mehr.

12Ja, diese Brut greift mich an!

Sie versuchen, mich zu Fall zu bringen,

sie schütten einen Belagerungswall rings um mich auf.

13Sie schneiden mir den Weg ab

und zerstören mein Leben,

niemand hält sie dabei auf.

14Sie durchbrechen meine Verteidigungsmauer

und zertrümmern, was ihnen in die Quere kommt.

15Furcht und Entsetzen haben mich gepackt

und meine Würde wie im Sturm verjagt;

meine Sicherheit ist vertrieben wie eine Wolke.

16Mein Leben verrinnt,

das Elend hat mich fest im Griff.

17Bohrende Schmerzen rauben mir den Schlaf,

sie nagen an mir Nacht für Nacht.

18Mit gewaltiger Kraft hat Gott mich am Gewand gepackt

und schnürt mich ein wie ein zu enger Kragen.

19Er wirft mich in den Schmutz,

ich bin zu Staub und Asche geworden.

20Ich schreie um Hilfe, o Gott,

aber du antwortest nicht;

ich stehe vor dir,

doch du starrst mich nur unerbittlich an.

21Du bist mein grausamer Feind geworden,

mit aller Kraft kämpfst du gegen mich!

22Du wirbelst mich empor in die Luft,

treibst mich vor dem Sturm dahin

und zerschmetterst mich dann mit lautem Krachen.

23Ja, ich weiß:

Du willst mich zu den Toten bringen,

hinunter in das Haus, wo alle Menschen sich versammeln.

24Doch wer unter Trümmern verschüttet wurde,

streckt die Hand nach Rettung aus;

schreit man nicht im Unglücksfall um Hilfe?

25Habe ich nicht damals über die geweint,

die ein schweres Los zu tragen hatten?

Ich hatte Mitleid mit den Armen!

26Und so erwartete ich Gutes,

doch das Unglück kam!

Ich erhoffte das Licht,

doch es kam die Dunkelheit.

27Mein Inneres ist aufgewühlt,

ich finde keine Ruhe,

die Tage des Elends haben mich eingeholt.

28Meine Haut ist schwarz geworden,

doch nicht von der Sonnenglut.

In der Versammlung stehe ich auf

und schreie laut um Hilfe.

29Mein Heulen klingt wie das der Schakale,

wie das Schreien der Strauße.

30Meine Haut ist schwarz geworden und schält sich,

das Fieber glüht in meinem Körper.

31Meine Laute spielt ein Trauerlied,

meine Flöte eine Melodie der Klage.«