Yobu 28 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 28:1-28

1Pali mgodi wa siliva

ndiponso malo oyengerapo golide.

2Chitsulo amachikumba pansi,

ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.

3Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale,

amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo,

kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.

4Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu,

kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko;

iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.

5Nthaka, imene imatulutsa zakudya,

kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;

6miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake,

ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.

7Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi,

palibe kamtema amene anayiona.

8Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo,

ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.

9Munthu amaphwanya matanthwe olimba,

ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.

10Amabowola njira mʼmatanthwewo;

ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.

11Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso,

motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.

12“Koma nzeru zingapezeke kuti?

Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?

13Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo;

nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.

14Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’

Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’

15Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri,

mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.

16Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri,

kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.

17Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi,

sungayigule ndi zokometsera zagolide.

18Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe;

mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.

19Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi;

nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.

20“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti?

Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?

21Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse,

ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.

22Chiwonongeko ndi imfa zikuti,

‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’

23Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko,

ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,

24pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi

ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.

25Iye atapatsa mphepo mphamvu zake,

nayeza kuzama kwa nyanja,

26atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa

ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,

27pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake;

nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.

28Ndipo Iye anati kwa munthu,

‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo

ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’ ”

Persian Contemporary Bible

ايوب 28:1-28

1مردم می‌دانند چگونه نقره را از معدن استخراج نمايند، طلا را تصفيه كنند، 2آهن را از زمين بيرون آورند و مس را از سنگ جدا سازند. 3آنها می‌دانند چطور معادن تاريک را روشن كنند و در جستجوی سنگهای معدن تا عمقهای تاريک زمين فرو روند. 4آنها در نقاطی دور دست، جايی كه پای بشری بدان راه نيافته، در دل زمين نقب می‌زنند و از طنابها آويزان شده، به عمق معادن می‌روند.

5مردم می‌دانند چگونه از روی زمين غذا تهيه كنند، در حالی که در زير پوستهٔ همين زمين، آتش نهفته است. 6آنها می‌دانند چگونه از سنگهای آن ياقوت و طلا به دست بياورند. 7حتی پرندگان شكاری راه معادن را نمی‌دانند و چشم هيچ عقابی آن را نمی‌تواند ببيند؛ 8پای شير يا جانور درندهٔ ديگری به اين معادن نرسيده است؛ 9ولی مردم می‌دانند چطور سنگهای خارا را تكه‌تكه نموده، کوهها را از بيخ و بن بركنند، 10صخره‌ها را بشكافند و به سنگهای قيمتی دست يابند. 11آنها حتی سرچشمهٔ رودها را كاوش می‌كنند و چيزهای مخفی از آن بيرون می‌آورند.

12مردم همهٔ اينها را می‌دانند، ولی نمی‌دانند فهم و حكمت را در كجا بيابند. 13حكمت در بين انسانها پيدا نمی‌شود و هيچكس ارزش آن را نمی‌داند.

14اقيانوسها می‌گويند: «در اينجا حكمت نيست.» و درياها جواب می‌دهند: «در اينجا هم نيست.» 15حكمت را با طلا و نقره نمی‌توان خريد، 16و نه با طلای خالص و سنگهای قيمتی. 17حكمت از طلا و الماس بسيار گرانبهاتر است و آن را نمی‌توان با جواهرات خريداری كرد. 18مرجان و بلور در برابر حكمت هيچ ارزشی ندارند. قيمت آن از لعل بسيار گرانتر است. 19نه می‌توان آن را با زبرجد مرغوب خريد و نه با طلای ناب.

20پس حكمت را از كجا می‌توان به دست آورد؟ در كجا پيدا می‌شود؟ 21زيرا از چشمان تمامی افراد بشر پنهان است. حتی از چشمان تيزبين پرندگان هوا نيز مخفی است؛ 22دنيای مردگان نيز از آن اطلاع ندارد.

23فقط خدا می‌داند كه حكمت را كجا می‌توان پيدا كرد؛ 24زيرا او تمامی زمين را زير نظر دارد و آنچه را كه در زير آسمانست مشاهده می‌كند. 25او باد را به حركت درمی‌آورد و حدود اقيانوسها را تعيين می‌كند. 26به باران فرمان می‌دهد كه ببارد و مسير برق آسمان را تعيين می‌كند. 27پس او می‌داند حكمت كجاست. او آن را آزمايش كرده و تأييد نموده است، 28و به افراد بشر می‌گويد: «بدانيد كه ترس از خداوند، حكمت واقعی، و دوری نمودن از شرارت، فهم حقيقی می‌باشد.»