Yobu 23 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 23:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;

Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.

3Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;

ndikanangopita kumene amakhalako!

4Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake

ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.

5Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,

ndi kulingalira bwino zimene akananena!

6Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?

Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.

7Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,

ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.

8“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,

ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.

9Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko

akapita kummwera, sindimuona.

10Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;

Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.

11Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;

ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.

12Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;

ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.

13“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?

Iye amachita chilichonse chimene wafuna.

14Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,

ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.

15Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;

ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.

16Mulungu walefula mtima wanga;

Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.

17Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,

ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Аюб 23:1-17

Ответ Аюба

1Тогда Аюб ответил:

2– Всё ещё горька моя жалоба;

невзирая на мой стон, Его рука тяжела.

3О, если бы я знал, где мне найти Его!

О, если бы я мог войти в жилище Его!

4Я бы дело моё перед Ним изложил

и наполнил уста свои оправданиями.

5Я узнал бы, что Он ответит мне,

я бы понял, что Он мне скажет.

6Разве стал бы Он судиться со мной во всей Своей мощи?

Нет! Он выслушал бы меня Сам.

7Тогда праведник мог бы судиться с Ним,

и я был бы навеки оправдан моим Судьёй.

8Иду ли на восток – Его там нет;

иду ли на запад – не нахожу Его.

9Творит ли Он что на севере – не вижу Его;

повернёт ли к югу – не замечаю.

10Но Ему известен мой путь;

пусть Он испытает меня, я выйду как очищенное золото.

11Я верно держался и хранил Его пути,

не уклоняясь в сторону.

12Не отступал я от повелений Его,

слова Его я хранил в сердце своём.

13Но если Он решил, то кто Ему противостанет?

Он творит, что Ему угодно.

14Исполняет Он Свой приговор против меня,

и много подобного в запасе у Него!

15Потому я и в ужасе перед Ним;

размышляя об этом, страшусь Его.

16Сделал Всевышний моё сердце слабым;

Всемогущий ужасом поразил меня.

17Но тьма и мгла, застилающая мне лицо,

не ввергли меня в безмолвие.