Yobu 12 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 12:1-25

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Ndithudi inuyo ndinu anthu

ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!

3Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu;

ineyo sindine munthu wamba kwa inu.

Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?

4“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga,

ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha.

Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!

5Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka.

Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.

6Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere,

ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino,

amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.

7“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa,

kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;

8kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa,

kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.

9Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa

kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?

10Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse,

ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.

11Kodi khutu sindiye limene limamva mawu

monga mmene lilime limalawira chakudya?

12Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba?

Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?

13“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu;

uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.

14Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso.

Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.

15Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma;

akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.

16Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana;

munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.

17Iye amalanda aphungu nzeru zawo

ndipo amapusitsa oweruza.

18Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo

ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.

19Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo

ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.

20Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika

ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.

21Iye amanyoza anthu otchuka

ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.

22Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima

ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.

23Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso;

amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.

24Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi;

amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.

25Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira;

Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

Slovo na cestu

Jób 12:1-25

1Odpověděv pak Job, řekl: 2V pravdě, že jste vy lidé, a že s vámi umře moudrost. 3I jáť mám srdce jako vy, aniž jsem zpozdilejší než vy, anobrž při komž toho není? 4Za posměch příteli svému jsem, kteréhož, když volá, vyslýchá Bůh; v posměchuť jest spravedlivý a upřímý. 5Pochodně zavržená jest (podlé smýšlení člověka pokoje užívajícího) ten, kterýž jest blízký pádu. 6Pokojné a bezpečné příbytky mají loupežníci ti, kteříž popouzejí Boha silného, jimž on uvodí dobré věci v ruku jejich. 7Ano zeptej se třebas hovad, a naučí tě, aneb ptactva nebeského, a oznámí tobě. 8Aneb rozmluv s zemí, a poučí tě, ano i ryby mořské vypravovati budou tobě. 9Kdo nezná ze všeho toho, že ruka Hospodinova to učinila? 10V jehož ruce jest duše všelikého živočicha, a duch každého těla lidského. 11Zdaliž ucho slov rozeznávati nebude, tak jako dásně pokrmu okoušejí? 12Při starcích jest moudrost, a při dlouhověkých rozumnost. 13Nadto pak u Boha moudrost a síla, jehoť jest rada a rozumnost. 14Jestliže on boří, nemůže zase stavíno býti; zavírá-li člověka, nemůže býti otevříno. 15Hle, tak zastavuje vody, až i vysychají, a tak je vypouští, že podvracejí zemi. 16U něho jest síla a bytnost, jeho jest ten, kterýž bloudí, i kterýž v blud uvodí. 17On uvodí rádce v nemoudrost, a z soudců blázny činí. 18Svazek králů rozvazuje, a pasem přepasuje bedra jejich. 19On uvodí knížata v nemoudrost, a mocné vyvrací. 20On odjímá řeč výmluvným, a soud starcům béře. 21On vylévá potupu na urozené, a sílu mocných zemdlívá. 22On zjevuje hluboké věci z temností, a vyvodí na světlo stín smrti. 23On rozmnožuje národy i hubí je, rozšiřuje národy i zavodí je. 24On odjímá srdce předním z lidu země, a v blud je uvodí na poušti bezcestné, 25Aby šámali ve tmě bez světla. Summou, činí, aby bloudili jako opilý.