Chiweruzo ndi Chipulumutso
1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;
ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.
Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,
ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga
anthu owukira aja,
amene amachita zoyipa,
natsatira zokhumba zawo.
3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa
mopanda manyazi.
Iwo amapereka nsembe mʼminda
ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
4Amakatandala ku manda
ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.
Amadya nyama ya nkhumba,
ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,
chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’
Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,
ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;
sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu
chifukwa cha machimo awo
7ndi a makolo awo,”
akutero Yehova.
“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri
ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,
Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata
zimene anachita kale.”
8Yehova akuti,
“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa
ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,
popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’
Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;
sindidzawononga onse.
9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,
ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.
Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,
ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,
ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe
kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
11“Koma inu amene mumasiya Yehova
ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,
amene munamukonzera Gadi chakudya
ndi kuthirira Meni chakumwa,
12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,
ndipo nonse mudzaphedwa;
chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,
ndinayankhula koma simunamvere.
Munachita zoyipa pamaso panga
ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,
“Atumiki anga adzadya,
koma inu mudzakhala ndi njala;
atumiki anga adzamwa,
koma inu mudzakhala ndi ludzu;
atumiki anga adzakondwa,
koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14Atumiki anga adzayimba
mosangalala,
koma inu mudzalira kwambiri
chifukwa chovutika mu mtima
ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15Anthu anga osankhidwa
adzatchula dzina lanu potemberera.
Ambuye Yehova adzakuphani,
koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo
adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;
ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo
adzalumbira mwa Mulungu woona.
Pakuti mavuto akale adzayiwalika
ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
Chilengedwe Chatsopano
17“Taonani, ndikulenga
mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.
Zinthu zakale sizidzakumbukika,
zidzayiwalika kotheratu.
18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya
chifukwa cha zimene ndikulenga,
pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa
ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu
ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.
Kumeneko sikudzamvekanso kulira
ndi mfuwu wodandaula.
20“Ana sadzafa ali akhanda
ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.
Wamngʼono mwa iwo
adzafa ali ndi zaka 100.
Amene adzalephere kufika zaka 100
adzatengedwa kukhala
wotembereredwa.
21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,
adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,
kapena kudzala ndi ena nʼkudya.
Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo
wautali ngati mitengo.
Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito
ya manja awo nthawi yayitali.
23Sadzagwira ntchito pachabe
kapena kubereka ana kuti aone tsoka;
chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,
iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.
Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.
Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,
koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.
Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala
chinthu chopweteka kapena chowononga,”
akutero Yehova.
Суд и спасение
1– Я открылся тем, кто не спрашивал Меня;
Я найден теми, кто не искал Меня.
Народу, не призывавшему Моё имя,
Я сказал: «Я здесь, Я здесь».
2Весь день Я простирал руки Мои
к этому упрямому народу,
что ходит путями недобрыми,
по собственным умыслам –
3к народу, что постоянно оскорбляет Меня прямо в лицо,
принося жертвы идолам в садах
и возжигая им благовония на кирпичных жертвенниках;
4что сидит в могильных пещерах
и ночи проводит в тайных местах,
вызывая мёртвых;
что ест свинину65:4 См. Лев. 11:7-8.
и держит в горшках похлёбку из нечистого мяса;
5что говорит: «Держись подальше, не приближайся ко мне;
я для тебя слишком свят».
Они – как дым для Моих ноздрей,
огонь, что горит весь день.
6Вот что написано предо Мной:
не смолчу, но воздам сполна,
сполна Я воздам им
7и за их грехи, и за грехи их отцов, –
говорит Вечный. –
Так как они возжигали благовония на горах
и оскорбляли Меня на холмах,
Я отмерю им наказание
за прежние их дела.
8Так говорит Вечный:
– Когда в виноградной грозди ещё остаётся сок,
говорят: «Не губи её;
в ней ещё есть польза!» –
так поступлю и Я ради Моих верных рабов:
всех Я не погублю.
9Я произведу новых потомков от Якуба,
и от Иуды – тех, кто будет владеть Моими горами:
унаследует их Мой избранный народ,
будут там жить Мои рабы.
10Шарон станет пастбищем для овец,
а долина Ахор – местом отдыха для волов;
они будут владениями Моего народа,
который Меня взыскал.
11Но вас, кто оставил Меня, Вечного,
забыл храм на Моей святой горе,
кто накрывает стол для Гада, божества удачи,
и наполняет приправленным вином чаши для Мени, божества судьбы, –
12вас обреку Я мечу;
все вы пойдёте на бойню,
потому что Я звал, а вы не отвечали,
Я говорил, а вы не слушали.
Вы творили зло у Меня на глазах
и предпочли то, что Мне неугодно.
13Поэтому так говорит Владыка Вечный:
– Рабы Мои будут есть,
а вы будете голодать;
рабы Мои будут пить,
а вы будете жаждать;
14рабы Мои будут радоваться,
а вы будете постыжены;
рабы Мои будут петь
от сердечной радости,
а вы будете кричать
от сердечных мук
и стенать от сокрушения духа.
15Имя своё вы оставите Моим избранным,
чтобы те использовали его как проклятие;
Владыка Вечный предаст вас смерти,
но рабам Своим даст Он другое имя.
16Всякий в стране, призывающий благословение на себя,
Богом истины будет благословляться;
всякий в стране, приносящий клятву,
Богом истины будет клясться.
Прежние горести позабудутся
и скроются с Моих глаз.
Новое небо и новая земля
17– Вот Я творю
новое небо и новую землю;
не пребудет в памяти прежнее
и на ум не придёт.
18Радуйтесь же и ликуйте вовеки о том,
что Я творю:
Я сделаю Иерусалим местом ликования,
а народ его наполню радостью!
19Сам Я возликую об Иерусалиме
и возрадуюсь о Моём народе.
Ни плача, ни вопля
не будет в нём больше слышно.
20Больше в нём не будут умирать младенцы,
и не будет старца, что не достиг бы полноты своих дней;
тот, кто умрёт столетним,
будет считаться юношей,
а кто не достигнет ста лет,
будет считаться проклятым65:20 Или: «а грешник, достигший ста лет, будет проклинаем»..
21Они будут строить дома и жить в них,
сажать виноградники и есть их плоды.
22Не будет такого больше, чтобы они строили дома,
а жил в них другой;
не будет такого, чтобы они сажали,
а плоды ел другой.
Люди Моего народа будут жить столь же долго, как и деревья;
избранные Мои будут наслаждаться плодами своего труда.
23Они не будут трудиться напрасно
и рожать детей на беду;
они будут народом, благословенным Вечным –
и они, и их потомки.
24Прежде чем воззовут они, Я отвечу;
пока ещё будут говорить, Я услышу.
25Волк и ягнёнок будут кормиться вместе,
и лев, как вол, будет есть сено,
а для змеи пыль будет пищей.
Не будут ни вредить, ни разрушать
на всей святой горе Моей, –
говорит Вечный.