Yesaya 60 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 60:1-22

Ulemerero wa Ziyoni

1“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,

ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.

2Taona, mdima waphimba dziko lapansi

ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,

koma Yehova adzakuwalira iwe,

ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

3Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako

ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.

4“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.

Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;

ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali

ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.

5Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,

mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;

chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe

chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.

6Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,

ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.

Ndipo onse a ku Seba adzabwera

atanyamula golide ndi lubani

uku akutamanda Yehova.

7Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,

nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;

zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,

ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.

8“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,

ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?

9Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;

patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,

zikubweretsa ana ako ochokera kutali,

pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,

kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,

Woyerayo wa Israeli,

pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.

10“Alendo adzamanganso malinga ako,

ndipo mafumu awo adzakutumikira.

Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,

koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.

11Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,

sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,

kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,

akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.

12Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;

adzawonongeka kotheratu.

13“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,

mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni

kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;

ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.

14Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;

onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.

Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;

Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.

15“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,

koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,

ndipo udzakhala malo a chimwemwe

cha anthu amibado yonse.

16Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu

ndi kuleredwa pa maere aufumu,

motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,

Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.

17Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,

ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.

Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa

ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.

Olamulira ako adzakhala a mtendere.

Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.

18Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,

bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,

ndidzakhala malinga ako okuteteza

ndipo udzanditamanda.

19Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,

kapena mwezi kuti uwunikire usiku,

pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,

ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20Dzuwa lako silidzalowanso,

ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;

Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,

ndipo masiku a mavuto ako adzatha.

21Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama

ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.

Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,

ntchito ya manja anga,

kuti aonetse ulemerero wanga.

22Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,

kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.

Ine ndine Yehova,

nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 60:1-22

Utukufu Wa Sayuni

160:1 Isa 52:2; Yn 8:12; Mal 4:2; Za 36:9; Efe 5:14; Za 118:27; Ufu 21:11; Kut 16:7“Ondoka, angaza, kwa kuwa nuru yako imekuja

na utukufu wa Bwana umezuka juu yako.

260:2 Yer 13:16; Kol 1:13; 1Sam 2:9; Za 82:5; Isa 8:20; Za 107:14Tazama, giza litaifunika dunia

na giza kuu litayafunika mataifa,

lakini Bwana atazuka juu yako

na utukufu wake utaonekana juu yako.

360:3 Mt 2:1-11; Isa 49:23; Ufu 21:24; Isa 44:5; 45:14; 42:6Mataifa watakuja kwenye nuru yako

na wafalme kwa mwanga wa mapambazuko yako.

460:4 Isa 11:12; 43:6; 49:20-22; Yer 30:10; Isa 43:6“Inua macho yako na utazame pande zote:

Wote wanakusanyika na kukujia,

wana wako wanakuja toka mbali,

nao binti zako wanabebwa mikononi.

560:5 Rum 11:25; Kut 34:29; Isa 35:2; 65:13; 66:14; Zek 10:7; Kum 33:19; Amu 3:15; Ufu 21; 6Ndipo utatazama na kutiwa nuru,

moyo wako utasisimka na kujaa furaha,

mali zilizo baharini zitaletwa kwako,

utajiri wa mataifa utakujilia.

660:6 Mwa 25:2-4; Yer 6:20; Za 72:10; Mt 2:11; Amu 6:5; Isa 42:10Makundi ya ngamia yatajaa katika nchi yako,

ngamia vijana wa Midiani na Efa.

Nao wote watokao Sheba watakuja,

wakichukua dhahabu na uvumba

na kutangaza sifa za Bwana.

760:7 Mwa 25:13; Hag 2:3-9; Isa 18:7; Sef 3:10; Eze 20:40; 43:27; Isa 19:21Makundi yote ya Kedari yatakusanyika kwako,

kondoo dume wa Nebayothi watakutumikia,

watakubalika kama sadaka juu ya madhabahu yangu,

nami nitalipamba Hekalu langu tukufu.

860:8 Isa 49:21; 19:1“Ni nani hawa warukao kama mawingu,

kama hua kuelekea kwenye viota vyao?

960:9 Mwa 10:4; Isa 2:16; 14:2; Yer 30:19; Isa 43:6; Gal 4:26; 1Fal 10:22Hakika visiwa vinanitazama,

merikebu za Tarshishi60:9 Au: za biashara (ona pia 1Fal 10:22; 22:48; 2Nya 9:21; 20:36; Isa 2:16). ndizo zinazotangulia,

zikiwaleta wana wenu kutoka mbali,

wakiwa na fedha na dhahabu zao,

kwa heshima ya Bwana, Mungu wenu,

yeye Aliye Mtakatifu wa Israeli,

kwa maana amekujalia utukufu.

1060:10 Ezr 1:2; Ufu 21:24; Za 102:13; Isa 54:8; Kut 1:11; Isa 14:1-2; 56:6“Wageni watazijenga upya kuta zako,

na wafalme wao watakutumikia.

Ingawa katika hasira nilikupiga,

lakini katika upendeleo wangu

nitakuonyesha huruma.

1160:11 Mik 2:13; Ufu 21:25-26; Isa 2:12; 61:6; Za 24:7Malango yako yatakuwa wazi siku zote,

kamwe hayatafungwa, mchana wala usiku,

ili watu wapate kukuletea utajiri wa mataifa:

wafalme wao wakiongoza maandamano ya ushindi.

1260:12 Isa 11:14; Zek 14:17; Za 2:12; Dan 2:34; Mwa 27:29Kwa maana taifa au ufalme ule ambao hautakutumikia utaangamia;

utaharibiwa kabisa.

1360:13 Isa 35:2; Ezr 3:7; 1Nya 28:2; Isa 41:19“Utukufu wa Lebanoni utakujilia,

msunobari, mvinje pamoja na mteashuri,

ili kupapamba mahali pangu patakatifu,

nami nitapatukuza mahali pa miguu yangu.

1460:14 Mwa 27:29; Ufu 3:9; Ebr 12:22; Isa 14:9; 1:12Wana wa wale waliokuonea watakuja wakisujudu mbele yako,

wote wanaokudharau watasujudu kwenye miguu yako,

nao watakuita Mji wa Bwana,

Sayuni ya Aliye Mtakatifu wa Israeli.

1560:15 Isa 6:12; 54:6; Za 126:5; Isa 65:18; 1:7-9; Kut 14:30; Isa 33:8“Ingawa umeachwa na kuchukiwa,

bila yeyote anayesafiri ndani yako,

nitakufanya kuwa fahari ya milele,

na furaha ya vizazi vyote.

1660:16 Eze 34:30; Kut 6:2; Isa 66:11-12; Ay 19:25; Isa 59:20; Kut 14:30Utanyonya maziwa ya mataifa,

na kunyonyeshwa matiti ya wafalme.

Ndipo utakapojua kwamba Mimi, Bwana, ni Mwokozi wako,

Mkombozi wako, niliye Mwenye Nguvu wa Yakobo.

1760:17 1Fal 10:21; Za 85:8; Isa 66:12; 9:7; Hag 2:9Badala ya shaba nitakuletea dhahabu,

na fedha badala ya chuma.

Badala ya mti nitakuletea shaba,

na chuma badala ya mawe.

Nitafanya amani kuwa mtawala wako,

na haki kuwa mfalme wako.

1860:18 Law 26:6; 2Sam 7:10; Yer 33:9; Sef 3:20; Isa 9:4; 49:19; 33:6; 61:11; 62:7Jeuri hazitasikika tena katika nchi yako,

wala maangamizi au uharibifu ndani ya mipaka yako,

lakini utaita kuta zako Wokovu,

na malango yako Sifa.

1960:19 Zek 2:5; Za 36:9; Ufu 21:23; 22:5; Za 118:27Jua halitakuwa tena nuru yako mchana,

wala mwangaza wa mwezi hautakuangazia,

kwa maana Bwana atakuwa nuru yako ya milele,

naye Mungu wako atakuwa utukufu wako.

2060:20 Amo 8:9; Isa 30:19, 26; Ufu 7:17; Isa 35:10Jua lako halitazama tena,

nao mwezi wako hautafifia tena;

Bwana atakuwa nuru yako milele,

nazo siku zako za huzuni zitakoma.

2160:21 Efe 2:10; Law 10:3; Za 37:11, 22; Zek 8:12; Amo 9:15; Isa 4:3; Yer 32:41; Mt 15:13Ndipo watu wako wote watakuwa waadilifu,

nao wataimiliki nchi milele.

Wao ni chipukizi nililolipanda,

kazi ya mikono yangu,

ili kuonyesha utukufu wangu.

2260:22 Mwa 12:2; Kum 1:10; Isa 5:19Aliye mdogo kwenu atakuwa elfu,

mdogo kuliko wote atakuwa taifa lenye nguvu.

Mimi ndimi Bwana;

katika wakati wake nitayatimiza haya upesi.”