Yesaya 56 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 56:1-12

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

1Yehova akuti,

“Chitani chilungamo

ndi zinthu zabwino,

chifukwa chipulumutso changa chili pafupi

ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.

2Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,

munthu amene amalimbika kuzichita,

amene amasunga Sabata osaliyipitsa,

ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

3Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,

“Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”

Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,

“Ine ndine mtengo wowuma basi.”

4Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,

nachita zokomera Ine

ndi kusunga pangano langa,

5ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino

mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,

kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.

Ndidzawapatsa dzina labwino,

losatha ndi losayiwalika.”

6Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,

motero kuti amamutumikira Iye,

amakonda dzina la Yehova,

amamugwirira ntchito,

komanso kusunga Sabata osaliyipitsa

ndi kusunga bwino pangano langa,

7amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,

ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.

Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo

ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.

Paja nyumba yanga idzatchedwa

nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”

8Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa

Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,

“Ndidzasonkhanitsano anthu ena

kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

9Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,

inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!

10Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,

onse ndi opanda nzeru;

onse ndi agalu opanda mawu,

samatha kuwuwa:

amagona pansi nʼkumalota

amakonda kugona tulo.

11Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;

sakhuta konse.

Abusa nawonso samvetsa zinthu;

onse amachita monga akufunira,

aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.

12Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!

Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!

Mawa lidzakhala ngati leroli,

kapena kuposa lero lino.”

Nova Versão Internacional

Isaías 56:1-12

Salvação para os Gentios

1Assim diz o Senhor:

“Mantenham a justiça

e pratiquem o que é direito,

pois a minha salvação está perto,

e logo será revelada a minha retidão.

2Feliz aquele que age assim,

o homem que nisso permanece firme,

observando o sábado para não profaná-lo,

e vigiando sua mão para não cometer nenhum mal”.

3Que nenhum estrangeiro

que se disponha a unir-se ao Senhor venha a dizer:

“É certo que o Senhor me excluirá do seu povo”.

E que nenhum eunuco se queixe: “Não passo de uma árvore seca”.

4Pois assim diz o Senhor:

“Aos eunucos que guardarem os meus sábados,

que escolherem o que me agrada

e se apegarem à minha aliança,

5a eles darei, dentro de meu templo e dos seus muros,

um memorial e um nome

melhor do que filhos e filhas,

um nome eterno, que não será eliminado.

6E os estrangeiros que se unirem ao Senhor para servi-lo,

para amarem o nome do Senhor e prestar-lhe culto,

todos os que guardarem o sábado deixando de profaná-lo,

e que se apegarem à minha aliança,

7esses eu trarei ao meu santo monte

e lhes darei alegria em minha casa de oração.

Seus holocaustos56.7 Isto é, sacrifícios totalmente queimados. e demais sacrifícios

serão aceitos em meu altar;

pois a minha casa será chamada

casa de oração para todos os povos”.

8Palavra do Soberano, do Senhor,

daquele que reúne os exilados de Israel:

“Reunirei ainda outros

àqueles que já foram reunidos”.

A Acusação de Deus contra os Ímpios

9Venham todos vocês, animais do campo;

todos vocês, animais da floresta, venham comer!

10As sentinelas de Israel estão cegas

e não têm conhecimento;

todas elas são como cães mudos,

incapazes de latir.

Deitam-se e sonham;

só querem dormir.

11São cães devoradores, insaciáveis.

São pastores sem entendimento;

todos seguem seu próprio caminho,

cada um procura vantagem própria.

12“Venham”, cada um grita, “tragam-me vinho!

Bebamos nossa dose de bebida fermentada,

que amanhã será como hoje,

e até muito melhor!”