Yesaya 56 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 56:1-12

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

1Yehova akuti,

“Chitani chilungamo

ndi zinthu zabwino,

chifukwa chipulumutso changa chili pafupi

ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.

2Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,

munthu amene amalimbika kuzichita,

amene amasunga Sabata osaliyipitsa,

ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

3Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,

“Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”

Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,

“Ine ndine mtengo wowuma basi.”

4Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,

nachita zokomera Ine

ndi kusunga pangano langa,

5ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino

mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,

kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.

Ndidzawapatsa dzina labwino,

losatha ndi losayiwalika.”

6Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,

motero kuti amamutumikira Iye,

amakonda dzina la Yehova,

amamugwirira ntchito,

komanso kusunga Sabata osaliyipitsa

ndi kusunga bwino pangano langa,

7amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,

ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.

Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo

ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.

Paja nyumba yanga idzatchedwa

nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”

8Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa

Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,

“Ndidzasonkhanitsano anthu ena

kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

9Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,

inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!

10Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,

onse ndi opanda nzeru;

onse ndi agalu opanda mawu,

samatha kuwuwa:

amagona pansi nʼkumalota

amakonda kugona tulo.

11Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;

sakhuta konse.

Abusa nawonso samvetsa zinthu;

onse amachita monga akufunira,

aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.

12Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!

Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!

Mawa lidzakhala ngati leroli,

kapena kuposa lero lino.”

New International Version – UK

Isaiah 56:1-12

Salvation for others

1This is what the Lord says:

‘Maintain justice

and do what is right,

for my salvation is close at hand

and my righteousness will soon be revealed.

2Blessed is the one who does this –

the person who holds it fast,

who keeps the Sabbath without desecrating it,

and keeps their hands from doing any evil.’

3Let no foreigner who is bound to the Lord say,

‘The Lord will surely exclude me from his people.’

And let no eunuch complain,

‘I am only a dry tree.’

4For this is what the Lord says:

‘To the eunuchs who keep my Sabbaths,

who choose what pleases me

and hold fast to my covenant –

5to them I will give within my temple and its walls

a memorial and a name

better than sons and daughters;

I will give them an everlasting name

that will endure for ever.

6And foreigners who bind themselves to the Lord

to minister to him,

to love the name of the Lord,

and to be his servants,

all who keep the Sabbath without desecrating it

and who hold fast to my covenant –

7these I will bring to my holy mountain

and give them joy in my house of prayer.

Their burnt offerings and sacrifices

will be accepted on my altar;

for my house will be called

a house of prayer for all nations.’

8The Sovereign Lord declares –

he who gathers the exiles of Israel:

‘I will gather still others to them

besides those already gathered.’

God’s accusation against the wicked

9Come, all you beasts of the field,

come and devour, all you beasts of the forest!

10Israel’s watchmen are blind,

they all lack knowledge;

they are all mute dogs,

they cannot bark;

they lie around and dream,

they love to sleep.

11They are dogs with mighty appetites;

they never have enough.

They are shepherds who lack understanding;

they all turn to their own way,

they seek their own gain.

12‘Come,’ each one cries, ‘let me get wine!

Let us drink our fill of beer!

And tomorrow will be like today,

or even far better.’