Yesaya 46 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 46:1-13

Za Kupasuka kwa Babuloni ndi Mafano Ake

1Beli wagwada pansi, Nebo wawerama;

nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo.

Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe.

Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.

2Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo;

sizikutha kupulumutsa katunduyo,

izo zomwe zikupita ku ukapolo.

3Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo,

inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli,

Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu,

ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.

4Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi

ndidzakusamalirani ndithu.

Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani,

ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.

5“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani?

Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?

6Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo

ndipo amayeza siliva pa masikelo;

amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu,

kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.

7Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo;

amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo.

Singathe kusuntha pamalo pakepo.

Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha;

kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.

8“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi,

Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.

9Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana;

chifukwa Ine ndine Mulungu

ndipo palibe wina ofanana nane.

10Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe.

Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike.

Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi.

Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.

11Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa.

Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa.

Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi;

zimene ndafuna ndidzazichitadi.

12Ndimvereni, inu anthu owuma mtima,

inu amene muli kutali ndi chipulumutso.

13Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa;

sichili kutali.

Tsikulo layandikira

ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani

ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

Священное Писание

Исаия 46:1-13

Боги Вавилона низвержены

1Пал на колени Бел, склоняется Нево46:1 Бел – верховное божество вавилонского пантеона, также называемое Мардуком. Нево – сын Мардука, бог мудрости, покровитель писцов и искусства письма.;

идолы их погружены на вьючных животных.

То, что носили вы, нагружено

поклажей на усталых животных.

2Вместе они все склоняются и падают на колени;

не в силах спасти поклажу,

они сами идут в плен.

3– Слушайте Меня, потомки Якуба,

все уцелевшие из народа Исраила,

вы, кого Я принял от рождения

и носил с тех пор, как вы родились.

4И до седой старости вашей Я буду Тот же,

и Я буду заботиться о вас.

Я вас создал и буду носить вас,

печься о вас и спасать.

5С кем вы Меня сравните,

равным кому сочтёте?

Кому вы Меня уподобите,

чтобы сравниться нам?

6Люди расточают золото из кошельков

и отвешивают на весах серебро,

нанимают плавильщика,

который делает из этого бога,

и простираются перед этим идолом,

поклоняются ему.

7Они поднимают его на плечи и носят;

ставят его на место, и он стоит.

С места своего он не двинется.

Пусть взывают к нему – не ответит;

он не может спасти от беды.

8Вспомните это и поразмыслите,

в памяти переберите, отступники.

9Вспомните прежние дела, бывшие издревле;

Я – Бог, и другого нет,

Я – Бог, и нет Мне равного.

10Я возвестил о конце изначала,

из древности – о грядущем.

Я говорю: «Мой замысел устоит;

всё, что угодно Мне, – сделаю».

11С востока зову Я хищную птицу,

из далёкой страны – человека, исполнить Мой замысел46:11 Здесь подразумевается Кир, царь Персии. См. также сноски на 41:2 и 44:28..

То, что Я сказал, Я исполню;

то, что задумал, – сделаю.

12Слушайте Меня, упрямые,

далёкие от избавления!

13Я приближаю Своё избавление,

недалеко оно;

спасение Моё не замедлит.

Я дарую спасение Сиону

и славу Мою – Исраилу.