Yesaya 42 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 42:1-25

Mtumiki wa Yehova

1“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,

amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.

Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,

ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.

2Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,

kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.

3Bango lophwanyika sadzalithyola,

ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.

Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;

4sadzafowoka kapena kukhumudwa

mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,

ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”

5Yehova Mulungu

amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,

amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,

amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,

ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,

6“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;

ndikugwira dzanja ndipo

ndidzakuteteza.

Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu

ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.

7Udzatsekula maso a anthu osaona,

udzamasula anthu a mʼndende

ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.

8“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!

Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense

kapena matamando anga kwa mafano.

9Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,

ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;

zinthuzo zisanaonekere

Ine ndakudziwitsani.”

Nyimbo Yotamanda Yehova

10Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,

inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.

Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.

11Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;

midzi ya Akedara ikondwere.

Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;

afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.

12Atamande Yehova

ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.

13Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,

adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;

akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo

ndipo adzagonjetsa adani ake.

14Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,

ndakhala ndili phee osachita kanthu.

Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,

ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.

15Ndidzawononga mapiri ndi zitunda

ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;

ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba

ndipo ndidzawumitsa maiwe.

16Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,

ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;

ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala

ndipo ndidzasalaza malo osalala.

Zimenezi ndizo ndidzachite;

sindidzawataya.

17Koma onse amene amadalira mafano

amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’

ndidzawachititsa manyazi kotheratu.

Aisraeli Alephera Kuphunzira

18“Imvani, agonthi inu;

yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?

Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?

Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,

kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?

20Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;

makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”

21Chinamukomera Yehova

chifukwa cha chilungamo chake,

kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.

22Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,

onsewa anawakola mʼmaenje

kapena akuwabisa mʼndende.

Tsono asanduka chofunkha

popanda wina wowapulumutsa

kapena kunena kuti,

“Abwezeni kwawo.”

23Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi

kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?

24Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,

ndi Israeli kwa anthu akuba?

Kodi si Yehova,

amene ife tamuchimwirayu?

Pakuti sanathe kutsatira njira zake;

ndipo sanamvere malangizo ake.

25Motero anawakwiyira kwambiri,

nawavutitsa ndi nkhondo.

Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;

motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.

Hoffnung für Alle

Jesaja 42:1-25

Der Diener Gottes und sein Auftrag

1Der Herr spricht: »Seht, hier ist mein Diener, zu dem ich stehe. Ihn habe ich auserwählt, und ich freue mich über ihn. Ich habe ihm meinen Geist gegeben, und er wird den Völkern mein Recht verkünden. 2Aber er schreit es nicht hinaus; er ruft nicht laut und lässt seine Stimme nicht durch die Straßen der Stadt hallen. 3Das geknickte Schilfrohr wird er nicht abbrechen und den glimmenden Docht nicht auslöschen. Unbeirrbar setzt er sich für das Recht ein. 4Er wird nicht müde, nie verliert er den Mut, bis er auf der ganzen Erde für Gerechtigkeit gesorgt hat. Selbst die Bewohner der Inseln und der fernen Küsten warten auf seine Weisung.«

5Gott, der Herr, hat den Himmel geschaffen und ihn wie ein Zeltdach ausgespannt. Die Erde in ihrer ganzen Weite hat er gebildet, die Pflanzen ließ er hervorsprießen, und den Menschen hat er Leben und Atem gegeben. Und nun sagt er zu seinem Diener:

6»Ich, der Herr, habe dich berufen, meine gerechten Pläne auszuführen. Ich fasse dich an der Hand und helfe dir, ich beschütze dich. Durch dich schließe ich einen Bund mit den Menschen, ja, für alle Völker mache ich dich zu einem Licht, das ihnen den Weg zu mir zeigt.42,6 Wörtlich: Ich mache dich zu einem Bund für das Volk und zum Licht für die Völker. 7Den Blinden sollst du das Augenlicht geben und die Gefangenen aus ihren Zellen holen. Alle, die in Finsternis sitzen, sollst du aus ihrer Gefangenschaft befreien. 8Ich heiße ›Herr‹, und ich bin es auch. Die Ehre, die mir zusteht, lasse ich mir nicht rauben. Ich dulde nicht, dass Götterfiguren für meine Taten gerühmt werden. 9Ihr könnt sehen, dass meine Vorhersagen eingetroffen sind. Und nun kündige ich etwas Neues an. Ich sage euch, was geschehen wird, ehe man das Geringste davon erkennt.«

Singt dem Herrn ein neues Lied!

10Singt dem Herrn ein neues Lied und rühmt ihn überall auf der Welt. Besingt ihn, ihr Seefahrer und alles, was im Meer lebt! Preist ihn, ihr Inseln und seine Bewohner! 11Auch die Wüste und alle, die dort leben, sollen in das Lied mit einstimmen. Singt und jubelt, ihr Beduinen von Kedar! Ihr aus dem Bergland,42,11 Oder: Ihr aus Sela (= Felsenstadt). – Vgl. die Anmerkung zu Kapitel 16,1. steigt auf die Gipfel und jubelt ihm zu! 12Ihr alle – gebt dem Herrn die Ehre und verkündet selbst auf den fernsten Inseln seine ruhmvollen Taten!

13Der Herr zieht in den Krieg wie ein Held. In aller Entschlossenheit rüstet er sich zum Kampf. Dann erhebt er sein lautes Kriegsgeschrei und zwingt seine Feinde in die Knie.

14»Sehr lange habe ich geschwiegen«, sagt der Herr. »Ich blieb ruhig und hielt mich zurück. Aber jetzt kann ich nicht mehr an mich halten. Nun schreie ich auf wie eine Frau in den Wehen, ich keuche und schnappe nach Luft. 15Berge und Hügel lasse ich austrocknen, alle Pflanzen darauf verdorren. Die Flüsse und Sümpfe sollen versanden und zu festem Boden werden. 16Mein blindes Volk werde ich auf Straßen führen, die sie nicht kennen, und neue Wege mit ihnen gehen. Ich mache die Dunkelheit um sie her zum Licht und räume die Hindernisse beiseite. Das alles werde ich tun, mein Plan steht fest.

17Aber alle, die ihre Hilfe von einer selbst gemachten Statue erwarten und zu ihr sagen: ›Du bist mein Gott‹, müssen beschämt die Flucht ergreifen.«

Israel verschließt die Augen vor dem Herrn

18»Ach, wie seid ihr taub und blind!«, sagt der Herr. »Warum wollt ihr nicht hören, warum nicht sehen? 19Wenn je ein Volk blind war, dann mein Volk Israel. Gibt es überhaupt einen, der so taub ist wie mein Volk, das ich als meinen Boten senden will? Gibt es ein Volk, das so blind ist wie Israel, mein Vertrauter42,19 Das hebräische Wort ist nicht sicher zu deuten., den ich in meinen Dienst gestellt habe? 20Was habt ihr nicht alles an Gutem gesehen, aber es lässt euch kalt! Was habt ihr nicht alles gehört, aber es war vergeblich!« 21Der Herr will, dass das Recht geschieht, darum hat er sein Gesetz klar und unübertrefflich gemacht. 22Was aber ist aus euch geworden? Ihr seid ein beraubtes und ausgeplündertes Volk. Gefesselt hockt ihr in Erdlöchern; man hat euch in Kerker gesteckt. Man hat euch ausgeplündert und verschleppt. Niemand hilft euch, niemand fordert eure Freilassung.

23Ach, wenn euch das doch zum Nachdenken bringen würde! Wenn ihr doch für euer weiteres Leben eine Lehre daraus ziehen wolltet! 24Wer hat denn zugelassen, dass Israel ausgeplündert wurde? Wer hat die Nachkommen von Jakob an die Räuber ausgeliefert? Ist es nicht der Herr, dem wir ungehorsam waren? Er hat es getan, weil Israel nicht auf ihn hören wollte, weil es seinen Geboten keine Beachtung schenkte. 25Darum bekamen sie seinen glühenden Zorn zu spüren: Er ließ Krieg ausbrechen; sie waren eingeschlossen von loderndem Feuer. Das ganze Land brannte – aber sie wollten nicht einsehen, dass der Herr sie straft. Sie ließen sich nicht belehren.