Yesaya 4 – CCL & TCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 4:1-6

1Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri

adzagwira mwamuna mmodzi,

nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu,

ndi kuvala zovala zathu;

inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu.

Tichotseni manyazi aumbeta!”

Nthambi ya Yehova

2Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli. 3Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu. 4Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto. 5Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova. 6Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.

Tagalog Contemporary Bible

Isaias 4:1-6

1Sa mga araw na iyon, pitong babae ang mag-aagawan sa isang lalaki at sasabihin nila, “Kami na ang bahala sa pagkain at damit namin, pakasalan mo lang kami para hindi kami kahiya-hiya dahil wala kaming asawa.”

Muling Pagpapalain ang Jerusalem

2Darating ang araw na pasasaganain at pagagandahin ng Panginoon ang mga pananim4:2 mga pananim: sa literal, mga sanga. sa Israel, at ang mga ani ng lupain ay magiging karangalan at kaligayahan ng natitirang mga tao sa Jerusalem. 3Tatawaging banal ang mga natirang buhay sa Zion, ang lungsod ng Jerusalem. 4Sa pamamagitan ng kanyang kapangyarihan, hahatulan niya at lilinisin ang kasamaan ng mga babae sa Jerusalem at ang mga patayan doon. 5Pagkatapos, lilikha ang Panginoon ng ulap na lililim sa ibabaw ng Jerusalem4:5 Jerusalem: sa Hebreo, Bundok ng Zion. at sa mga nagtitipon doon. Lilikha rin siya ng nagniningas na apoy na magbibigay ng liwanag kung gabi. Tatakip ito sa Jerusalem na parang isang malapad na tolda, 6at parang kubol na magsisilbing lilim sa init ng araw at kublihan sa panahon ng bagyo at ulan.