Yesaya 32 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 32:1-20

Ufumu Wachilungamo

1Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo,

ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.

2Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo

ndi malo obisalirapo namondwe,

adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu,

ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.

3Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,

ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.

4Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa,

ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.

5Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake

ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.

6Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru,

amaganiza kuchita zoyipa:

Iye amachita zoyipira Mulungu,

ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova;

anjala sawapatsa chakudya

ndipo aludzu sawapatsa madzi.

7Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso,

iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa.

Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake

ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.

8Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino,

Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.

Akazi a ku Yerusalemu

9Khalani maso, inu akazi

amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji

ndipo imvani mawu anga.

Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!

10Pakapita chaka ndi masiku pangʼono

inu akazi amatama mudzanjenjemera;

chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika

ndipo zipatso sizidzaoneka.

11Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu;

ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu.

Vulani zovala zanu,

ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.

12Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde,

ndi mphesa yawonongeka.

13Mʼdziko la anthu anga

mwamera minga ndi mkandankhuku.

Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero

ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.

14Nyumba yaufumu idzasiyidwa,

mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu;

malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya.

Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.

15Yehova adzatipatsa mzimu wake,

ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde,

ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.

16Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama

ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.

17Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo;

zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.

18Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere,

mʼnyumba zodalirika,

ndi malo osatekeseka a mpumulo.

19Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala

ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,

20inutu mudzakhala odalitsika ndithu.

Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse,

ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

Священное Писание

Исаия 32:1-20

Царство праведности

1Вот Царь будет царствовать в праведности,

и правители будут править справедливо.

2Каждый будет словно укрытие от ветра

и приют от бури,

как потоки воды в пустыне

и тень огромной скалы в жаждущей земле.

3Тогда глаза видящих больше не закроются,

и уши слышащих будут слушать.

4Разум нетерпеливых научится понимать,

и языки заикающихся будут говорить гладко и ясно.

5Не будут больше глупца называть благородным

и подлеца – почтенным.

6Ведь глупец говорит глупости,

разум его помышляет о зле –

поступать лицемерно

и распространять заблуждения о Вечном;

он голодного оставит голодным

и у жаждущего отнимет питьё.

7Приёмы подлеца скверные,

он вынашивает злобные мысли –

погубить бедняков ложью,

даже если жалоба бедных справедлива.

8А благородный мыслит благородно

и стоит за благородные дела.

Женщины Иерусалима

9Беззаботные женщины,

встаньте, послушайте меня;

беспечные дочери,

слушайте мою речь!

10Немногим больше, чем через год,

вы, беспечные, содрогнётесь,

потому что сбора винограда не будет,

не наступит время сбора плодов.

11Трепещите, беззаботные женщины,

дрожите, беспечные дочери!

В горе сорвите свои одежды

и рубищем оберните бёдра.

12Бейте себя в грудь, скорбя о полях плодородных

и плодоносных лозах,

13о земле моего народа,

которая порастёт терновником и колючками.

Плачьте о всех домах радости,

о ликующем ныне городе,

14ведь дворцы будут оставлены

и шумный город покинут;

крепость и сторожевая башня будут заброшены навеки,

станут пустошью, на радость диким ослам,

пастбищем для стад,

15пока не изольётся на нас Дух свыше

и не станет пустыня плодородным полем,

а плодородное поле не сочтут лесом.

16Правосудие будет обитать в пустыне

и праведность – в плодородном поле.

17Плодом праведности будет мир;

следствием праведности будут покой и безопасность навеки.

18Мой народ будет жить в мирных жилищах,

в надёжных домах,

в безопасных местах.

19Даже если лес будет полностью уничтожен32:19 Или: «будет побит градом».,

и город сровняется с землёй,

20благословенны будете вы, сеющие возле всякой реки

и пускающие своих коров и ослов бродить на воле.