Yesaya 2 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 2:1-22

Phiri la Yehova

1Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

2Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,

lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

3Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

4Iye adzaweruza pakati pa mayiko,

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

5Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,

tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

6Inu Yehova mwawakana anthu anu,

nyumba ya Yakobo.

Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;

amawombeza mawula ngati Afilisti,

ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.

7Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;

ndipo chuma chawo ndi chosatha.

Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;

ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.

8Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;

iwo amapembedza ntchito ya manja awo,

amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.

9Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa

ndi kutsitsidwa.

Inu Yehova musawakhululukire.

10Lowani mʼmatanthwe,

bisalani mʼmaenje,

kuthawa kuopsa kwa Yehova

ndi ulemerero wa ufumu wake!

11Kudzikuza kwa anthu kudzatha,

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku

limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,

ndipo adzagonjetsa

onse amphamvu,

13tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,

ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,

14tsiku la mapiri onse ataliatali

ndiponso la zitunda zonse zazitali,

15tsiku la nsanja zonse zazitali

ndiponso malinga onse olimba,

16tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi

ndiponso la mabwato onse okongola.

17Kudzikuza kwa munthu kudzatha

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,

18ndipo mafano onse adzatheratu.

19Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndi mʼmaenje a nthaka,

kuthawa mkwiyo wa Yehova,

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

20Tsiku limenelo anthu adzatayira

mfuko ndi mileme

mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,

amene anawapanga kuti aziwapembedza.

21Adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka

kuthawa mkwiyo wa Yehova

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22Lekani kudalira munthu,

amene moyo wake sukhalira kutha.

Iye angathandize bwanji wina aliyense?

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 2:1-22

Mlima Wa Bwana

(Mika 4:1-3)

12:1 Isa 1:1Hili ndilo aliloliona Isaya mwana wa Amozi kuhusu Yuda na Yerusalemu:

22:2 Dan 2:35; 11:45; Yoe 3:17; Mdo 2:17; Isa 11:9; 65:9; Zek 14:10; Yer 16:19Katika siku za mwisho

mlima wa Hekalu la Bwana utaimarishwa

kama mlima mkuu miongoni mwa milima yote,

utainuliwa juu ya vilima,

na mataifa yote yatamiminika huko.

32:3 Zek 8:21; Lk 24:47; Yn 4:22; Isa 33:22; 45:23; Yer 3:17; Kum 33:19Mataifa mengi yatakuja na kusema,

“Njooni, twendeni mlimani mwa Bwana,

kwenye nyumba ya Mungu wa Yakobo.

Atatufundisha njia zake,

ili tuweze kuenenda katika mapito yake.”

Sheria itatoka Sayuni,

neno la Bwana litatoka Yerusalemu.

42:4 Hos 2:18; Yer 30:11; Za 96:13; 51:4; 46:9; Yoe 3:10; Mwa 49:10; Zek 9:10Atahukumu kati ya mataifa

na ataamua migogoro ya mataifa mengi.

Watafua panga zao ziwe majembe,

na mikuki yao kuwa miundu ya kukata matawi.

Taifa halitainua upanga dhidi ya taifa jingine,

wala hawatajifunza vita tena.

52:5 Isa 60:19-20; 1Yn 1:5-7; Isa 58:1; 60:1Njooni, enyi nyumba ya Yakobo,

tutembeeni katika nuru ya Bwana.

Siku Ya Bwana

62:6 Kum 18:10, 14; 31:17; Yer 12:7; 2Nya 16:7; Isa 44:25; 2Fal 16:7; Kum 31:17Umewatelekeza watu wako,

nyumba ya Yakobo.

Wamejaa ushirikina utokao Mashariki,

wanapiga ramli kama Wafilisti

na wanashikana mikono na wapagani.

72:7 Mwa 41:43; Kum 17:16; Mik 5:10; Za 17:14; Isa 31:1; Kum 17:17Nchi yao imejaa fedha na dhahabu,

hakuna mwisho wa hazina zao.

Nchi yao imejaa farasi,

hakuna mwisho wa magari yao.

82:8 Isa 10:9-11; 17:8; 44:17; Ufu 9:20; 2Nya 32:19; Mik 5:13; Isa 44:17; Za 135:15Nchi yao imejaa sanamu,

wanasujudia kazi za mikono yao,

vitu vile vidole vyao vimevitengeneza.

92:9 Za 62:9; Isa 13:11; 5:15; 2:11, 17; Hes 4:5; Neh 4:5Kwa hiyo mwanadamu atashushwa

na binadamu atanyenyekezwa:

usiwasamehe.

102:10 Ufu 6:15-16; Nah 3:11; Za 145:12; Isa 2:19; 2The 1:9Ingieni kwenye miamba,

jificheni ardhini

kutokana na utisho wa Bwana

na utukufu wa enzi yake!

112:11 Isa 24:21-23; 37:23; 10:12; 5:15; Eze 31:10; Oba 1:8; Neh 9:29; Ay 40:11; Za 46:10; Hab 2:5Macho ya mtu mwenye majivuno yatanyenyekezwa

na kiburi cha wanadamu kitashushwa,

Bwana peke yake ndiye atakayetukuzwa siku hiyo.

122:12 Za 76:12; 59:12; Eze 7:7; Ay 40:11; Isa 13:6-9; 34:8; Yer 30:7; Mao 1:12; 2Sam 22:28; Yoe 1:15; Amo 5:18Bwana Mwenye Nguvu Zote anayo siku aliyoiweka akiba

kwa wote wenye kujivuna na wenye kiburi,

kwa wote wanaojikweza

(nao watanyenyekezwa),

132:13 Amu 9:15; Isa 10:33, 34; 29:17; Eze 27:5; Za 22:12; Zek 11:2kwa mierezi yote ya Lebanoni iliyo mirefu sana,

na mialoni yote ya Bashani,

142:14 Isa 30:25; 40:4kwa milima yote mirefu

na vilima vyote vilivyoinuka,

152:15 Isa 25:2, 12; 30:25; 32:14; 33:18; Sef 1:16kwa kila mnara ulio mrefu sana

na kila ukuta wenye ngome,

162:16 Mwa 10:4; 1Fal 10:22; 9:26kwa kila meli ya biashara,2:16 Au: ya Tarshishi (ona pia 1Fal 10:22; 22:48; 2Nya 9:21; 20:36; Isa 60:9.)

na kila chombo cha baharini cha fahari.

172:17 2Sam 22:28; Ay 40:112:17 Nah 3:13; Ebr 10:31; Kum 2:25; Isa 11:10, 15Majivuno ya mwanadamu yatashushwa,

na kiburi cha wanadamu kitanyenyekezwa,

Bwana peke yake ndiye atatukuzwa siku hiyo,

182:18 Kum 9:21; Mik 5:13; Eze 36:25; Isa 21:9; Yer 10:11; 1Sam 5:2nazo sanamu zitatoweka kabisa.

192:19 Hos 10:8; Nah 1:3-6; Ay 9:6; 30:9; Ebr 12:26; Hab 3:6; Amu 6:2; Isa 7:19; 14:16; Ay 30:6; Lk 23:30; Ufu 6:15Watu watakimbilia kwenye mapango ndani ya miamba,

na kwenye mahandaki ardhini

kutokana na utisho wa Bwana

na utukufu wa enzi yake,

ainukapo kuitikisa dunia.

202:20 Law 11:19; Eze 36:25; 7:19-20; 14:6; Ufu 9:20; Isa 2:11; Ay 22:24Siku ile, watu watawatupia

panya na popo

sanamu zao za fedha na za dhahabu,

walizozitengeneza ili waziabudu.

212:21 Kut 33:22; Za 145:12; Isa 33:10; 2:19Watakimbilia kwenye mapango miambani

na kwenye nyufa za miamba

kutokana na utisho wa Bwana

na utukufu wa enzi yake,

ainukapo kuitikisa dunia.

222:22 Mit 23:4; Yer 17:5; Yak 4:14; Ay 12:19; Za 119:8-9; Isa 51:12; 40:15; Za 18:42; 118:6, 8; 146:3Acheni kumtumainia mwanadamu,

ambaye hana kitu ila pumzi katika pua zake.

Yeye ana thamani gani?