Yesaya 15 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 15:1-9

Za Kulangidwa kwa Mowabu

1Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

Mzinda wa Kiri wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,

akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;

anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.

Mutu uliwonse wametedwa mpala,

ndipo ndevu zonse zametedwa.

3Mʼmisewu akuvala ziguduli;

pa madenga ndi mʼmabwalo

aliyense akulira mofuwula,

misozi ili pupupu.

4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,

mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.

Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,

ndipo ataya mtima.

5Inenso ndikulirira Mowabu;

chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari

ndi Egilati-Selisiya

akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,

Akulira mosweka mtima

pa njira yopita ku Horonaimu;

akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.

6Madzi a ku Nimurimu aphwa

ndipo udzu wauma;

zomera zawonongeka

ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.

7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,

achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.

8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;

kulira kwawo kosweka mtima kukumveka

mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.

9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,

komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,

mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu

ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

New Serbian Translation

Књига пророка Исаије 15:1-9

Тужбалица над Моавцима

1Пророштво против Моава:

„Обноћ је опустошен Ар;

срушен је Моав!

Обноћ је опустошен Кир;

срушен је Моав!

2У храм и Девон она се успиње

на узвишицу да плаче;

над Нававом и над Медевом

нариче народ моавски;

а све су главе оголеле

и све браде обријане;

3по улицама су врећама заогрнути,

на њиховим крововима и по трговима

сви они наричу

и плачући силазе.

4Есевон и Елеалија јаучу,

глас њихов се чује до Јасе.

Зато дрхћу ратници моавски,

у грчу је душа њихова.

5Зато јеца срце моје због Моаваца,

бегунци њихови беже

до Соара, Еглат-Селисије,

плачући се пењу на Луит;

путем оронајимским

разлеже се јаук над рушевинама.

6Јер су се исушиле воде нимримске,

трава је усахла,

биље пропало,

зеленила више нема.

7Зато ко је нешто уштедео и складишта њихова,

тај ће то носити на Поток врба.

8Јер јаук се разлеже до границе с Моавом,

нарицање му је до Еглајима,

нарицање му је до Вир-Елима.

9Та, пуне су крви воде димонске,

а ја ћу још додати Димону

једног лава на моавске бегунце

и на преостале у земљи.“