Za Kulangidwa kwa Mowabu
1Uthenga wonena za Mowabu:
Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Mzinda wa Kiri wawonongedwa,
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,
akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;
anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.
Mutu uliwonse wametedwa mpala,
ndipo ndevu zonse zametedwa.
3Mʼmisewu akuvala ziguduli;
pa madenga ndi mʼmabwalo
aliyense akulira mofuwula,
misozi ili pupupu.
4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,
mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.
Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,
ndipo ataya mtima.
5Inenso ndikulirira Mowabu;
chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari
ndi Egilati-Selisiya
akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,
Akulira mosweka mtima
pa njira yopita ku Horonaimu;
akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6Madzi a ku Nimurimu aphwa
ndipo udzu wauma;
zomera zawonongeka
ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,
achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;
kulira kwawo kosweka mtima kukumveka
mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,
komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,
mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu
ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Тужбалица над Моавцима
1Пророштво против Моава:
„Обноћ је опустошен Ар;
срушен је Моав!
Обноћ је опустошен Кир;
срушен је Моав!
2У храм и Девон она се успиње
на узвишицу да плаче;
над Нававом и над Медевом
нариче народ моавски;
а све су главе оголеле
и све браде обријане;
3по улицама су врећама заогрнути,
на њиховим крововима и по трговима
сви они наричу
и плачући силазе.
4Есевон и Елеалија јаучу,
глас њихов се чује до Јасе.
Зато дрхћу ратници моавски,
у грчу је душа њихова.
5Зато јеца срце моје због Моаваца,
бегунци њихови беже
до Соара, Еглат-Селисије,
плачући се пењу на Луит;
путем оронајимским
разлеже се јаук над рушевинама.
6Јер су се исушиле воде нимримске,
трава је усахла,
биље пропало,
зеленила више нема.
7Зато ко је нешто уштедео и складишта њихова,
тај ће то носити на Поток врба.
8Јер јаук се разлеже до границе с Моавом,
нарицање му је до Еглајима,
нарицање му је до Вир-Елима.
9Та, пуне су крви воде димонске,
а ја ћу још додати Димону
једног лава на моавске бегунце
и на преостале у земљи.“