Kulangidwa Kwa Babuloni
1Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,
muwafuwulire ankhondo;
muwakodole kuti adzalowe pa zipata
za anthu olemekezeka.
3Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;
ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira
amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4Tamvani phokoso ku mapiri,
likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!
Tamvani phokoso pakati pa maufumu,
ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!
Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera
kuchita nkhondo.
5Iwo akuchokera ku mayiko akutali,
kuchokera kumalekezero a dziko
Yehova ali ndi zida zake za nkhondo
kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;
lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7Zimenezi zinafowoketsa manja onse,
mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,
zowawa ndi masautso zidzawagwera;
adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.
Adzayangʼanana mwamantha,
nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9Taonani, tsiku la Yehova likubwera,
tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;
kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu
ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga
sizidzaonetsa kuwala kwawo.
Dzuwa lidzada potuluka,
ndipo mwezi sudzawala konse.
11Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,
anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.
Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,
ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.
Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13Tsono ndidzagwedeza miyamba
ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.
Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse
pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14Ngati mbawala zosakidwa,
ngati nkhosa zopanda wozikusa,
munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,
aliyense adzathawira ku dziko lake.
15Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa
adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;
nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva
ndipo sasangalatsidwa ndi golide,
kuti amenyane ndi Ababuloni.
18Adzapha anyamata ndi mauta awo;
sadzachitira chifundo ana
ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.
Anthu ake amawunyadira.
Koma Yehova adzawuwononga
ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20Anthu sadzakhalamonso
kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;
palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,
palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,
nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;
mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,
ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22Mu nsanja zake muzidzalira afisi,
mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.
Nthawi yake yayandikira
ndipo masiku ake ali pafupi kutha.
سقوط بابل
1اين است پيغامی كه اشعيا (پسر آموص) دربارهٔ بابل از خدا دريافت كرد:
2پرچم جنگ را بر تپهای بلند برافرازيد و سربازان را فرا خوانيد و دروازههای مجلل بابل را به آنها نشان دهيد تا به سوی آنها يورش برند. 3خداوند سپاه مقدس و شجاع خود را كه مشتاق خدمتش هستند فرا خوانده است تا كسانی را كه بر ايشان غضبناک است مجازات كند. 4صدايی در کوهها به گوش میرسد! اين صدا، صدای جمع شدن قومهای جهان است. خداوند قادر متعال آنها را برای جنگ آماده میكند. 5آنها را از سرزمينهای بسيار دور میآورد تا ايشان را همچون اسلحهای در دست بگيرد و توسط آنها سراسر خاک بابل را ويران كند و غضب خود را فرو نشاند. 6ناله كنيد، زيرا روز خداوند نزديک است روزی كه خدای قادر مطلق شما را هلاک كند. 7در آن روز، دستهای همه از ترس سست خواهد شد و دلها آب خواهد گرديد. 8همه هراسان خواهند شد و دردی شديد مانند درد زنی كه میزايد وجودشان را فرا خواهد گرفت. بر يكديگر نظر خواهند افكند و از ديدن صورتهای دگرگون شدهٔ يكديگر به وحشت خواهند افتاد. 9اينک روز هولناک خشم و غضب خداوند فرا میرسد! زمين ويران خواهد شد و گناهكاران هلاک خواهند گرديد. 10ستارگان آسمان نور نخواهند داشت، خورشيد هنگام طلوع تاريک خواهد شد و ماه روشنايی نخواهد بخشيد.
11خداوند میفرمايد: «من دنيا را به خاطر شرارتش، و بدكاران را به سبب گناهانشان مجازات خواهم كرد. تمام متكبران را خوار خواهم ساخت و همهٔ ظالمان را ذليل خواهم كرد. 12زندگان از طلای خالص نيز كميابتر خواهند بود. 13من، خداوند قادر متعال، در روز خشم طوفانی خود، آسمانها را خواهم لرزاند و زمين را از جای خود تكان خواهم داد.
14«بيگانگانی كه در بابل ساكن باشند به سرزمينهای خود خواهند رفت. آنان مانند گلهای پراكنده و آهويی كه مورد تعقيب شكارچی قرار گرفته باشد به وطن خود فرار خواهند كرد. 15هر كه گير بيفتد با شمشير يا نيزه كشته خواهد شد. 16اطفال كوچک در برابر چشمان والدينشان به زمين كوبيده خواهند شد؛ خانهها غارت و زنان بیعصمت خواهند گرديد.
17«من مادها را كه توجهی به طلا و نقره ندارند به ضد بابلیها برخواهم انگيخت تا بابلیها نتوانند با پيشكش كردن ثروت خود جان خود را نجات دهند. 18سپاهيان مهاجم بر جوانان و كودكان رحم نخواهند كرد و آنها را با تير و كمان هدف قرار خواهند داد. 19به اين ترتيب، خدا بابل را كه باشكوهترين ممالک و زينت فخر كلدانيان است مانند سدوم و عموره با خاک يكسان خواهد كرد. 20بابل ديگر هرگز آباد و قابل سكونت نخواهد شد. حتی اعراب چادرنشين نيز در آنجا خيمه نخواهند زد و چوپانان گوسفندان خود را در آن مكان نخواهند چرانيد. 21تنها حيوانات وحشی در آنجا به سر خواهند برد و روباهها در آن محل لانه خواهند كرد. جغدها در خانههای آنجا ساكن خواهند شد و بزهای وحشی در آنجا جست و خيز خواهند كرد. 22صدای زوزهٔ گرگها و شغالها از درون كاخهای زيبای بابل به گوش خواهد رسيد. آری، زمان نابودی بابل نزديک است!»