Yesaya 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 1:1-31

11:1 1Sam 3:1; Hes 12:6; 2Fal 14:21; 16:1; 1Nya 3:12-13; 2Nya 26:22; 1Sam 22:1, 5; Oba 1:1; Nah 1:1; Isa 40:9; 44:26Maono kuhusu Yuda na Yerusalemu ambayo Isaya mwana wa Amozi aliyaona wakati wa utawala wa Uzia, Yothamu, Ahazi na Hezekia, wafalme wa Yuda.

Taifa Asi

21:2 Hag 1:12; Amu 11:10; Kum 4:26; Yer 42:5; Isa 23:4; 63:16; 65:2; Eze 24:3; Mik 1:2; Isa 63:16; Mal 1:6Sikieni, enyi mbingu! Sikilizeni, enyi dunia!

Kwa maana Bwana amesema:

“Nimewalisha watoto na kuwalea,

lakini wameniasi mimi.

31:3 Yer 4:22; 9:3-6; Hos 2:8; Ay 12:9; Mwa 42:27; Kum 32:28; Isa 42:25; Ay 12:9; Hos 4:1; Isa 48:8; Hos 4:6; 7:9Ngʼombe anamjua bwana wake,

naye punda anajua hori la mmiliki wake,

lakini Israeli hajui,

watu wangu hawaelewi.”

41:4 Yer 23:14; Eze 39:7; 2Fal 19:22; Isa 1:2; Za 14:3; Kum 32:15; Isa 5:19; 31:1; 5:18; 9:17; 14:20; Za 119:87Lo! Taifa lenye dhambi,

watu waliolemewa na uovu,

uzao wa watenda mabaya,

watoto waliozoelea upotovu!

Wamemwacha Bwana,

Wamemkataa kwa dharau

yeye Aliye Mtakatifu wa Israeli

na kumgeuzia kisogo.

51:5 Yer 2:20; 30:17; 44:16-17; 2:30; 5:3; Ebr 3:16; Isa 31:6; 44:16-17; Mit 20:30; Mao 2:11Kwa nini mzidi kupigwa?

Kwa nini kudumu katika uasi?

Kichwa chako chote kimejeruhiwa,

moyo wako wote ni mgonjwa.

61:6 Kum 28:35; Yer 8:22; 14:19; 30:17; Mao 2:13; Eze 34:4; Lk 10:34; 2Sam 14:2; Za 45:7; 104:15; 38:3; Isa 61:3; 53:5; 30:26Kutoka wayo wako wa mguu hadi kwenye utosi wa kichwa chako

hakuna uzima:

ni majeraha matupu na makovu

na vidonda vitokavyo damu,

havikusafishwa au kufungwa

wala kulainishwa kwa mafuta.

71:7 Kum 28:51; Amu 6:3-6; Isa 62:8; 2Fal 18:13; Law 26:34; 26:16; Yer 5:17; Za 109:11Nchi yenu imekuwa ukiwa,

miji yenu imeteketezwa kwa moto;

nchi yenu imeachwa tupu na wageni

mbele ya macho yenu,

imeharibiwa kama vile imepinduliwa na wageni.

81:8 Za 9:14; Isa 10:32; 30:17; 49:21; Ay 27:18Binti Sayuni ameachwa kama kipenu

katika shamba la mizabibu,

kama kibanda katika shamba la matikitimaji,

kama mji uliohusuriwa.

91:9 Rum 9:29; 2Fal 21:14; Mwa 45:7; 19:24; Isa 4:2; 6:13; 27:12; Yer 23:3; Yoe 2:32Kama Bwana Mungu Mwenye Nguvu Zote1:9 Bwana Mwenye Nguvu Zote hapa ni Yehova Sabaoth, yaani Bwana wa Majeshi; pia Warumi 9:29 na Yakobo 5:4.

asingelituachia walionusurika,

tungelikuwa kama Sodoma,

tungelifanana na Gomora.

101:10 Isa 30:9; 28:14; 5:24; 8:20; 13:19; Ufu 11:8; Mwa 13:13; Eze 16:49; Rum 9:29Sikieni neno la Bwana,

ninyi watawala wa Sodoma;

sikilizeni sheria ya Mungu wetu,

enyi watu wa Gomora!

111:11 Amo 6:4; Yer 6:20; Ebr 10:4; Za 50:8; 40:6; Ay 22:3; Isa 66:3; 1Sam 15:22; Mal 1:10Bwana anasema, “Wingi wa sadaka zenu,

ni kitu gani kwangu?

Ninazo sadaka za kuteketezwa nyingi kupita kiasi,

za kondoo dume na mafuta ya wanyama walionona.

Sipendezwi na damu za mafahali

wala za wana-kondoo na mbuzi.

121:12 Kut 23:17; Kum 31:11Mnapokuja kujihudhurisha mbele zangu,

ni nani aliyewataka ninyi mfanye hivyo,

huku kuzikanyaga nyua zangu?

131:13 Mit 15:8; 1Nya 23:31; Hag 2:14; Yer 18:15; 44:8; 1Fal 11:24; Mit 28:9; Yer 7:9; Isa 41:24; 66:3Acheni kuniletea sadaka zisizokuwa na maana!

Uvumba wenu ni chukizo kwangu.

Miandamo ya Mwezi, Sabato na makusanyiko ya ibada:

siwezi kuvumilia makusanyiko yenu maovu.

141:14 Za 69:3; Kut 12:16; Mal 3:14; Kum 16:1-7; Neh 10:33; Ay 7:12; Hes 28:11-29; Law 23:1-44Sikukuu zenu za Miandamo ya Mwezi, na sikukuu zenu zilizoamriwa:

moyo wangu unazichukia.

Zimekuwa mzigo kwangu,

nimechoka kuzivumilia.

151:15 Ay 27:9; Kum 31:17; 1:45; Mik 3:4; Hos 4:2; Isa 57:17; 59:2; Kut 9:29; Yoe 3:21; 1Sam 8:18Mnaponyoosha mikono yenu katika maombi,

nitaficha macho yangu nisiwaone;

hata mkiomba maombi mengi

sitasikiliza.

Mikono yenu imejaa damu;

161:16 Yer 4:14; 25:5; Hes 19:11-16; Isa 52:11; Rut 3:3; Yak 4:8; Mt 27:24jiosheni na mkajitakase.

Yaondoeni matendo yenu maovu

mbele zangu!

Acheni kutenda mabaya,

171:17 Mik 6:8; Sef 2:3; Ay 22:9; Isa 33:5; Kut 22:22; Amo 5:14-15; Za 34:14; 72:1; Isa 11:4jifunzeni kutenda mema!

Tafuteni haki,

watieni moyo walioonewa.

Teteeni shauri la yatima,

wateteeni wajane.

181:18 1Sam 2:25; Isa 41:21; 55:7; Ufu 7:14; Za 51:7; Isa 43:9; 41:1; 43:26“Njooni basi tuhojiane,”

asema Bwana.

“Ingawa dhambi zenu ni kama rangi nyekundu,

zitakuwa nyeupe kama theluji;

ingawa ni nyekundu sana kama damu,

zitakuwa nyeupe kama sufu.

191:19 Ezr 9:12; Za 34:10; Ay 36:11; Isa 50:10; 62:9; Kum 30:15-16; Isa 58:14; 65:13; 30:32Kama mkikubali na kutii,

mtakula mema ya nchi,

201:20 Yer 17:27; Hes 23:19; Ay 15:22; 1Sam 12:15; Isa 3:25; 21:17; 34:16; 27:1; 65:12lakini kama mkikataa na kuasi,

mtaangamizwa kwa upanga.”

Kwa kuwa kinywa cha Bwana kimenena.

211:21 Isa 57:3-9; Yer 2:20; 3:2-9; 13:27; Eze 23:3; Hos 2:1-13; Amo 6:12; Isa 46:13; 59:14; Mit 6:17Tazama jinsi mji uliokuwa mwaminifu

umekuwa kahaba!

Mwanzoni ulikuwa umejaa unyofu,

haki ilikuwa inakaa ndani yake,

lakini sasa ni wauaji!

221:22 Za 119:119Fedha yenu imekuwa takataka,

divai yenu nzuri imechanganywa na maji.

231:23 Kum 19:14; Amo 5:8; Yer 5:28; Mik 2:1-2; 6:12; Kut 23:8; Isa 10:2; Eze 22:6-7; Isa 1:2; Mik 3:9; Amo 5:12; Hab 1:4Watawala wenu ni waasi,

rafiki wa wevi,

wote wanapenda rushwa

na kukimbilia hongo.

Hawatetei yatima,

shauri la mjane haliletwi mbele yao lisikilizwe.

241:24 Mwa 49:24; Isa 34:2, 8; 47:3; 59:17; 63:4; Yer 51:6; Eze 5:13; Kum 32:43Kwa hiyo Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote,

Mwenye Nguvu wa Israeli, asema hivi:

“Lo, nitapata faraja kutoka kwa adui zangu

na kujilipizia kisasi juu ya watesi wangu.

251:25 Yer 9:7; 6:29; Ufu 3:19; Isa 48:10; Kum 28:63; Za 78:38; 2Nya 29:15; Eze 22:22; Za 119:119Nitauelekeza mkono wangu dhidi yenu,

nitawasafisha takataka zenu zote

na kuwaondolea unajisi wenu wote.

261:26 Mik 4:8; Zek 8:3; Yer 31:23; 33:7; Kum 9:24; Mwa 32:28; Isa 32:16; 46:13; 4:3; 48:2Nitawarudishia waamuzi wenu kama ilivyokuwa siku za zamani,

nao washauri wenu kama ilivyokuwa mwanzoni.

Baadaye utaitwa,

Mji wa Haki,

Mji Mwaminifu.”

271:27 Isa 31:6; 59:20; 35:10; 41:14; 62:12; 63:4; 30:15; Hos 2:19; Eze 18:30Sayuni itakombolewa kwa haki,

wale waliomo ndani yake waliotubu kwa uaminifu.

281:28 Yer 4:18; 44:12; 2The 1:8-9; Isa 33:14; 43:27; 48:8; 16:2; Kum 32:18; 32:15; Za 9:5; Yer 16:4Lakini waasi na wenye dhambi wote wataangamizwa,

nao wanaomwacha Bwana wataangamia.

291:29 Eze 6:13; Hos 4:13; Isa 65:3; 42:17; 44:9; 57:5; Za 97:7; Yer 10:14; Za 97:7“Mtaaibika kwa sababu ya hiyo mialoni

ambayo mlifurahia,

mtafadhaika kwa sababu ya bustani

mlizozichagua.

301:30 Za 1:3Mtakuwa kama mwaloni wenye majani yanayonyauka,

kama bustani isiyokuwa na maji.

311:31 Isa 4:4; 5:24; 9:18-19; 24:6; 33:14; 66:15-16, 24; Yer 5:14; 7:20; Mal 3:2; Mt 25:41Mtu mwenye nguvu atatoweka kama majani makavu yawakayo moto,

na kazi yake kama cheche ya moto;

vyote vitaungua pamoja,

wala hakuna wa kuuzima huo moto.”