Yeremiya 50 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 50:1-46

Uthenga Wonena za Babuloni

1Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:

2“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina,

kweza mbendera ndipo ulengeze;

usabise kanthu, koma uwawuze kuti,

‘Babuloni wagwa;

mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi,

nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha.

Milungu yake yagwidwa ndi mantha

ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’

3Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni

ndi kusandutsa bwinja dziko lake.

Kumeneko sikudzakhalanso

munthu kapena nyama.

4“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”

akutero Yehova,

“anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda

onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.

5Adzafunsa njira ya ku Ziyoni

ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko.

Iwo adzadzipereka kwa Yehova

pochita naye pangano lamuyaya

limene silidzayiwalika.

6“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika;

abusa awo

anawasocheretsa mʼmapiri.

Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda

mpaka kuyiwala kwawo.

7Aliyense amene anawapeza anawawononga;

adani awo anati, ‘Ife si olakwa,

chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni

ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’

8“Thawaniko ku Babuloni;

chokani mʼdziko la Ababuloni.

Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.

9Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina

ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto

kudzamenyana ndi Babuloni.

Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni.

Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso,

yosapita padera.

10Motero Ababuloni adzafunkhidwa;

ndipo onse omufunkha adzakhuta,”

akutero Yehova.

11“Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika.

Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala.

Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu

ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.

12Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri.

Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa.

Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse.

Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.

13Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu

ndipo adzakhala chipululu chokhachokha.

Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya

chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.

14“Inu okoka uta,

konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse.

Muponyereni mivi yanu yonse

chifukwa anachimwira Yehova.

15Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja.

Nsanja zake zagwa.

Malinga ake agwetsedwa.

Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova.

Mulipsireni,

mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.

16Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense,

ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola.

Poona lupanga la ozunza anzawo,

aliyense adzabwerera kwa anthu ake;

adzathawira ku dziko la kwawo.

17“Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika

pothamangitsidwa ndi mikango.

Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo.

Wotsiriza anali Nebukadinezara

mfumu ya ku Babuloni

amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”

18Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake

monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.

19Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake

ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani;

adzadya nakhuta ku mapiri

a ku Efereimu ndi Giliyadi.

20Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”

akutero Yehova,

“anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli

koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe,

ndipo adzafufuza machimo a Yuda,

koma sadzapeza ndi limodzi lomwe,

chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.

21“Lithireni nkhondo dziko la Merataimu

ndi anthu okhala ku Pekodi.

Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,”

akutero Yehova.

“Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.

22Mʼdziko muli phokoso la nkhondo,

phokoso la chiwonongeko chachikulu!

23Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera

uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi.

Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha

pakati pa mitundu ina!

24Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni,

ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu;

unapezeka ndiponso unakodwa

chifukwa unalimbana ndi Yehova.

25Yehova watsekula nyumba ya zida zake

ndipo watulutsa zida za ukali wake,

pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire

mʼdziko la Ababuloni.

26Mumenyane naye Babuloni mbali zonse.

Anthu ake muwawunjike

ngati milu ya tirigu.

Muwawononge kotheratu

ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.

27Iphani ankhondo ake onse.

Onse aphedwe ndithu.

Tsoka lawagwera

pakuti tsiku lawo lachilango lafika.

28Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni

akulengeza mu Yerusalemu

za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu.

Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.

29“Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni.

Muyitanenso onse amene amakoka mauta.

Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira;

musalole munthu aliyense kuthawa.

Muchiteni monga momwe

iye anachitira anthu ena.

Iyeyu ananyoza

Yehova, Woyera wa Israeli.

30Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake;

ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,”

akutero Yehova.

31“Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,”

akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,

“chifukwa tsiku lako lafika,

nthawi yoti ndikulange yakwana.

32Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa

ndipo palibe amene adzakudzutse;

ndidzayatsa moto mʼmizinda yake

umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”

33Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Anthu a ku Israeli akuzunzidwa,

pamodzi ndi anthu a ku Yuda,

ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa,

akukana kuwamasula.

34Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo

nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo,

koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”

35Yehova akuti,

“Imfa yalunjika pa Ababuloni,

pa akuluakulu ake

ndi pa anthu ake a nzeru!

36Imfa yalunjika pa aneneri abodza

kuti asanduke zitsiru.

Imfa yalunjika pa ankhondo ake

kuti agwidwe ndi mantha aakulu.

37Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake.

Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo

kuti asanduke ngati akazi.

Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake

kuti chidzafunkhidwe.

38Chilala chilunjike pa madzi ake

kuti aphwe.

Babuloni ndi dziko la mafano,

ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.

39“Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko

ndipo kudzakhalanso akadzidzi.

Kumeneko sikudzapezekako anthu,

ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.

40Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora

pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,”

akutero Yehova,

“momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko;

anthu sadzayendanso mʼmenemo.

41“Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto;

mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri,

wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.

42Atenga mauta ndi mikondo;

ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo.

Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja.

Akwera pa akavalo awo,

ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo

iwe Babuloni.

43Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo,

ndipo yalobodokeratu.

Ikuda nkhawa,

ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.

44Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani

kupita ku msipu wobiriwira,

momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi.

Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine.

Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane?

Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”

45Nʼchifukwa chake imvani.

Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni.

Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo

ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.

46Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera,

ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.

New Russian Translation

Иеремия 50:1-46

Пророчество о Вавилоне

1Слово, которое Господь сказал через пророка Иеремию о Вавилоне и земле халдеев:

2– Объявите и возвестите среди народов,

поднимите знамя и возвестите,

не скрывайте, скажите:

«Вавилон будет взят;

опозорится Бел,

Меродах50:2 Бел и Меродах – имена вавилонского бога, которые переводятся как «господин». будет полон страха.

Будут опозорены его истуканы,

и наполнятся его идолы страхом».

3Двинется на него народ с севера

и опустошит его землю.

Никто не будет на ней жить:

разбегутся и люди, и звери.

4В те дни, в то время, –

возвещает Господь, –

народ Израиля вместе с народом Иудеи

пойдут, рыдая, искать Господа, своего Бога.

5Они будут расспрашивать о дороге к Сиону,

обратив к нему лица.

Они придут и соединятся

с Господом заветом вечным,

который не будет забыт никогда.

6Мой народ был как пропавшие овцы;

пастухи сбили их с пути

и позволили разбежаться по горам;

они бродили по горам и холмам

и забыли свое пристанище.

7Каждый, кто ни находил, пожирал их;

их враги говорили: «На нас нет вины,

ведь они согрешили против Господа,

истинного пастбища их,

против Господа, надежды их отцов».

8Бегите из Вавилона,

оставьте землю халдеев

и будьте как козлы,

что идут впереди отары.

9Я подниму и пошлю на Вавилон

собрание великих народов из северных земель.

Они встанут против него боевым строем

и захватят его с севера.

Стрелы их врагов как искусные воины,

что без добычи не возвращаются.

10Так земля халдеев будет разграблена;

все, кто придут ее грабить, насытятся вдоволь, –

возвещает Господь. –

11За то, что вы радовались и ликовали,

расхитители Моего наследия,

за то, что резвились, как телица на траве,

и ржали, как жеребцы,

12опозорена будет ваша мать,

обесславлена будет родившая вас.

Среди народов будет она меньшей:

пустыней, иссохшей землей, голой степью.

13Из-за гнева Господнего она не заселится,

и придет целиком в запустение.

Все, проходящие мимо Вавилона,

ужаснутся и поиздеваются

над всеми его ранами.

14Становитесь в строй вокруг Вавилона,

все, натягивающие луки.

Стреляйте в него! Не жалейте стрел,

потому что он согрешил против Господа.

15Со всех сторон поднимите на него крик.

Он сдается, его укрепления пали,

его стены разрушены!

Это Господня месть!

Отомстите Вавилону!

Как он поступал с другими,

так и вы поступите с ним.

16Истребите в Вавилоне сеятеля

и жнеца с серпом в пору жатвы.

Из-за страха перед мечом притеснителя

пусть каждый вернется к своему народу,

пусть каждый бежит в свою землю.

17Израиль – рассеявшаяся отара,

которую разогнали львы.

Первым, кто пожирал его,

был царь Ассирии,

а этот последний, разгрызший его кости, –

Навуходоносор, царь Вавилона.

18Поэтому так говорит Господь Сил, Бог Израиля:

– Я накажу царя Вавилона и его страну

так же, как Я наказал царя Ассирии.

19А Израиль Я верну на его пастбище,

и он будет пастись на Кармиле и в Башане;

он утолит свой голод на холмах

Ефрема и Галаада50:19 Кармил, Башан, холмы Ефрема и Галаад – эти районы отличались плодородием..

20В те дни, в то время, –

возвещает Господь, –

будут искать за Израилем вину,

но ее не окажется,

будут искать грехи за Иудой,

но ничего не найдут,

потому что Я прощу тех,

кого оставлю в живых.

21Нападайте на землю Мератаим50:21 Мератаим («Двойной Бунт») – это вероятно название земли на юге Вавилона.

и на тех, кто живет в Пекоде50:21 Пекод («Наказание») – область к востоку от Тигра. Здесь используется игра слов: значения этих названий символизируют весь Вавилон и его судьбу..

Убивайте, истребляйте их до последнего50:21 На языке оригинала стоит слово, которое говорит о полном посвящении предметов или людей Господу, часто осуществлявшемся через их уничтожение. То же в ст. 26; 51:3., –

возвещает Господь. –

Исполните все, что Я повелел вам.

22Шум битвы слышен в стране,

шум лютой гибели!

23Как расколот и сокрушен

молот вселенной!

Каким ужасом стал Вавилон

среди народов!

24Я расставил тебе западню, Вавилон,

и ты попался, прежде чем это заметил.

Ты был найден и схвачен за то,

что был против Господа.

25Господь отворил Свое хранилище

и взял оружие Своего гнева,

так как Владыка, Господь Сил,

желает завершить Свои замыслы

в земле халдеев.

26Идите же против него отовсюду.

Открывайте его амбары;

собирайте в кучу все, что найдете,

и уничтожьте полностью,

не оставляйте ничего!

27Убивайте его воинов;

пусть шагают, как волы, на бойню!

Горе им! Настал их день,

пришло время расплаты!

28– Слышите! Беженцы и уцелевшие из Вавилона

идут рассказать на Сионе

как Господь, наш Бог, отомстил за Свой храм.

29– Призовите стрелков на Вавилон,

всех, кто натягивает лук.

Все встаньте лагерем вокруг него,

чтобы никто не спасся.

Воздайте ему за его дела;

поступите с ним так, как поступал он с вами.

Ведь он бросил вызов Господу,

Святому Израиля.

30За это его юноши падут на улицах,

все его воины умолкнут в тот день, –

возвещает Господь. –

31Я против тебя, гордец, –

возвещает Владыка, Господь Сил, –

так как день твой настал,

время твоей кары пришло.

32Гордец споткнется и упадет,

и никто его не поднимет;

Я зажгу огонь в его городах,

и он пожрет все, что вокруг него.

33Так говорит Господь Сил:

– Народ Израиля угнетен,

как и народ Иудеи.

Все взявшие их в плен крепко держат их,

отказываясь отпустить.

34Но их Искупитель могуч;

Его имя – Господь Сил.

Он обязательно вступится за Свой народ,

чтобы дать покой их земле

и тревогу – жителям Вавилона.

35Меч поразит халдеев, –

возвещает Господь, –

жителей вавилонских,

его вождей и мудрецов!

36Меч поразит его лжепророков –

они обезумеют.

Меч поразит его воинов –

они задрожат от страха.

37Меч поразит его коней и колесницы,

и всех иноземцев в его войсках –

станут они трусливы, как женщины.

Меч поразит его сокровища:

они будут разграблены.

38Поразит засуха его воды –

они пересохнут.

Ведь это – земля истуканов,

где сошли с ума от чудовищ-идолов.

39Поэтому поселятся в Вавилоне

звери пустыни и гиены,

и будут в нем жить совы.

Впредь не заселится он никогда

и будет необитаем из поколения в поколение.

40Как Бог низверг Содом и Гоморру

с их окрестными городами50:40 См. Быт. 18:20–19:29., –

возвещает Господь, –

так никто не будет жить и там,

ни один человек не поселится.

41Вот, движется войско с севера;

великий народ и множество царей

поднимаются с краев земли.

42Их оружие – лук и копье;

они свирепы и не знают пощады.

Шум от них – как рев моря,

когда они скачут на конях.

В боевом строю идут воины

против тебя, дочь Вавилона.

43Царь Вавилона услышал весть о них,

и руки его опустились.

Пронзила его боль,

охватили муки, как женщину в родах.

44– Словно лев, который выходит

из иорданской чащи

на роскошные пастбища,

Я во мгновение ока

изгоню жителей Вавилона из их земель

и поставлю над ними того, кого изберу.

Кто подобен Мне? Кто спросит с Меня?

Какой правитель может противостоять Мне?

45Слушайте же замысел Господа о Вавилоне

и намерения, которые Он задумал

о земле халдеев:

молодняк отар будет угнан прочь,

и погубит Он их пастбища.

46От шума взятия Вавилона вздрогнет земля;

его крик будет слышен среди народов.