Yeremiya 46 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 46:1-28

1Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.

Uthenga Wonena za Igupto

2Kunena za Igupto:

Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,

3anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo,

ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!

4Mangani akavalo,

ndipo kwerani inu okwerapo!

Khalani pa mzere

mutavala zipewa!

Nolani mikondo yanu,

valani malaya anu ankhondo!

5Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani?

Achita mantha

akubwerera,

ankhondo awo agonjetsedwa.

Akuthawa mofulumirapo

osayangʼananso mʼmbuyo,

ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,”

akutero Yehova.

6Waliwiro sangathe kuthawa

ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka.

Akunka napunthwa ndi kugwa

kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.

7“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo,

ngati mtsinje wa madzi amkokomo?

8Igupto akusefukira ngati Nailo,

ngati mitsinje ya madzi amkokomo.

Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi;

ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’

9Tiyeni, inu akavalo!

Thamangani inu magaleta!

Tulukani, inu ankhondo,

ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango,

ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.

10Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse;

tsiku lolipsira, lolipsira adani ake.

Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi,

lidzaledzera ndi magazi.

Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe

mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.

11“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala

iwe namwali Igupto.

Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira;

palibe mankhwala okuchiritsa.

12Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako;

kulira kwako kwadzaza dziko lapansi.

Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana,

onse awiri agwa pansi limodzi.”

13Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:

14“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli.

Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi.

Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza,

chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’

15Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa?

Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.

16Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa.

Aliyense akuwuza mnzake kuti,

‘Tiyeni tibwerere kwathu,

ku dziko kumene tinabadwira,

tithawe lupanga la adani athu.’

17Kumeneku iwo adzafuwula kuti,

‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti,

Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’

18“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu,

imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse,

“wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena,

ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.

19Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo

inu anthu a ku Igupto,

pakuti Mefisi adzasanduka chipululu

ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.

20“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola,

koma chimphanga chikubwera

kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.

21Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye

ali ngati ana angʼombe onenepa.

Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi.

Palibe amene wachirimika.

Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira;

ndiyo nthawi yowalanga.

22Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa

pamene adani abwera ndi zida zawo,

abwera ndi nkhwangwa

ngati anthu odula mitengo.

23Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,”

akutero Yehova,

“ngakhale kuti ndi yowirira.

Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe,

moti sangatheke kuwerengeka.

24Anthu a ku Igupto achita manyazi

atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”

25Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira. 26Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.

27“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha;

usataye mtima, iwe Israeli.

Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali,

ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo.

Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere,

ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.

28Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha,

pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova.

“Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu

a ku mayiko kumene ndakupirikitsira,

Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu.

Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera;

sindidzakulekerera osakulanga.”

Nova Versão Internacional

Jeremias 46:1-28

Mensagem acerca do Egito

1Esta é a mensagem do Senhor que veio ao profeta Jeremias acerca das nações:

2Acerca do Egito:

Esta é a mensagem contra o exército do rei do Egito, o faraó Neco, que foi derrotado em Carquemis, junto ao rio Eufrates, por Nabucodonosor, rei da Babilônia, no quarto ano do reinado de Jeoaquim, filho de Josias, rei de Judá:

3“Preparem seus escudos, os grandes e os pequenos,

e marchem para a batalha!

4Selem os cavalos e montem!

Tomem posição e coloquem o capacete!

Passem óleo na ponta de suas lanças

e vistam a armadura!

5Mas o que vejo?

Eles estão apavorados,

estão se retirando,

seus guerreiros estão derrotados.

Fogem às pressas, sem olhar para trás;

há terror por todos os lados”, declara o Senhor.

6“O ágil não consegue fugir,

nem o forte escapar.

No norte, junto ao rio Eufrates,

eles tropeçam e caem.

7“Quem é aquele que se levanta como o Nilo,

como rios de águas agitadas?

8O Egito se levanta como o Nilo,

como rios de águas agitadas.

Ele diz: ‘Eu me levantarei e cobrirei a terra;

destruirei as cidades e os seus habitantes’.

9Ao ataque, cavalos!

Avancem, carros de guerra!

Marchem em frente, guerreiros!

Homens da Etiópia e da Líbia46.9 Hebraico: de Cuxe e de Fute., que levam escudos;

homens da Lídia, que empunham o arco!

10Mas aquele dia pertence ao Soberano,

ao Senhor dos Exércitos.

Será um dia de vingança,

para vingar-se dos seus adversários.

A espada devorará até saciar-se,

até satisfazer sua sede de sangue.

Porque o Soberano, o Senhor dos Exércitos,

fará um banquete na terra do norte, junto ao rio Eufrates.

11“Suba a Gileade em busca de bálsamo,

ó virgem, filha do Egito!

Você multiplica remédios em vão;

não há cura para você.

12As nações ouviram da sua humilhação;

os seus gritos encheram a terra,

quando um guerreiro

tropeçou noutro guerreiro e ambos caíram”.

13Esta é a mensagem que o Senhor falou ao profeta Jeremias acerca da vinda de Nabucodonosor, rei da Babilônia, para atacar o Egito:

14“Anunciem isto no Egito e proclamem-no em Migdol;

proclamem-no também em Mênfis e em Tafnes:

Assumam posição! Preparem-se!

Porque a espada devora aqueles que estão ao seu redor.

15Por que o deus Ápis fugiu?46.15 Ou Por que os seus guerreiros estão estirados no chão?

O seu touro não resistiu, porque o Senhor o derrubou.

16Tropeçam e caem, caem uns sobre os outros.

Eles dizem: ‘Levantem-se.

Vamos voltar para nosso próprio povo e para nossa terra natal,

para longe da espada do opressor.

17O faraó, rei do Egito,

é barulho e nada mais!

Ele perdeu a sua oportunidade’.

18“Juro pela minha vida”, declara o Rei,

cujo nome é Senhor dos Exércitos,

“ele virá como o Tabor entre os montes,

como o Carmelo junto ao mar.

19Arrumem a bagagem para o exílio,

vocês que vivem no Egito,

pois Mênfis será arrasada,

ficará desolada e desabitada.

20“O Egito é uma linda novilha,

mas do norte a ataca uma mutuca.

21Os mercenários em suas fileiras são como bezerros gordos.

Eles também darão meia volta e juntos fugirão;

não defenderão suas posições,

pois o dia da derrota deles está chegando,

a hora de serem castigados.

22O Egito silvará como uma serpente em fuga

à medida que o inimigo avança com grande força.

Virão sobre ele com machados,

como os homens que derrubam árvores.

23Eles derrubarão sua floresta”, declara o Senhor,

“por mais densa que seja.

São mais que os gafanhotos;

são incontáveis!

24A cidade46.24 Hebraico: filha. do Egito será envergonhada,

será entregue nas mãos do povo do norte”.

25O Senhor dos Exércitos, o Deus de Israel, diz: “Castigarei Amom, deus de Tebas46.25 Hebraico: No., o faraó, o Egito, seus deuses e seus reis, e também os que confiam no faraó. 26Eu os entregarei nas mãos daqueles que desejam tirar-lhes a vida; nas mãos de Nabucodonosor, rei da Babilônia, e de seus oficiais. Mais tarde, porém, o Egito será habitado como em épocas passadas”, declara o Senhor.

27“Quanto a você, não tema, meu servo Jacó!

Não fique assustado, ó Israel!

Eu o salvarei de um lugar distante;

e os seus descendentes, da terra do seu exílio.

Jacó voltará e ficará em paz e em segurança;

ninguém o inquietará.

28Não tema, meu servo Jacó!

Eu estou com você”, declara o Senhor.

“Destruirei completamente

todas as nações entre as quais eu o dispersei;

mas a você não destruirei completamente.

Eu o disciplinarei como você merece;

não serei severo demais”.